< 2 Samuel 14 >

1 Then Ioab the sonne of Zeruiah perceyued, that the Kings heart was toward Absalom,
Yowabu mwana wa Zeruya anadziwa kuti maganizo a mfumu ali pa Abisalomu.
2 And Ioab sent to Tekoah, and brought thence a subtile woman, and sayd vnto her, I pray thee, fayne thy selfe to mourne, and nowe put on mourning apparel, and anoynt not thy selfe with oyle: but be as a woman that had now long time mourned for the dead.
Kotero Yowabu anatuma munthu wina kupita ku Tekowa ndi kukatengako mkazi wanzeru. Yowabu anati kwa mkaziyo, “Ukhale ngati namfedwa. Uvale zovala zaumasiye ndipo usadzole mafuta ena aliwonse. Ukhale ngati mkazi amene wakhala akulira masiku ambiri.
3 And come to the King, and speake on this maner vnto him, (for Ioab taught her what she should say).
Kenaka upite kwa mfumu ndipo ukayankhule mawu awa.” Ndipo Yowabu anamuwuza mawu oti akanene.
4 Then the woman of Tekoah spake vnto the king, and fel downe on her face to the ground, and did obeysance, and sayd, Helpe, O King.
Mkazi wochokera ku Tekowa uja atapita kwa mfumu anadzigwetsa pansi, napereka ulemu kwa mfumu nati, “Thandizeni mfumu!”
5 Then the King sayd vnto her, What aileth thee? And she answered, I am in deede a widow, and mine husband is dead:
Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi chikukusautsa iwe nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mkazi wamasiye, mwamuna wanga anamwalira.
6 And thine handmayd had two sonnes, and they two stroue together in the fielde: (and there was none to part them) so the one smote the other, and slew him.
Ine wantchito wanu ndinali ndi ana aamuna awiri. Iwo anayamba kumenyana mʼmunda, ndipo panalibe woti awaleretse. Wina anakantha mnzakeyo mpaka kumupha.
7 And beholde, the whole familie is risen against thine handmayde, and they sayde, Deliuer him that smote his brother, that we may kill him for the soule of his brother whome hee slewe, that we may destroy the heire also: so they shall quenche my sparkle which is left, and shall not leaue to mine husband neither name nor posteritie vpon the earth.
Tsono banja lonse landiwukira ine, wantchito wanu. Iwo akuti, ‘Utipatse mwana amene anakantha mʼbale wakeyo kuti timuphe chifukwa cha moyo wa mʼbale wake amene anaphedwayo. Ife tidzaphanso mlowamʼmalo.’ Anthuwo adzapha mwana wanga amene wanditsalira, ndipo dzina la mwamuna wanga silidzakumbukika pakuti sipadzakhalanso mwana pa banja lathu.”
8 And the King said vnto the woman, Go to thine house, and I wil giue a charge for thee.
Mfumu inati kwa mkaziyo, “Pitani ku nyumba kwanu ndipo ine ndidzalamula mʼmalo mwanu.”
9 Then the woman of Tekoah said vnto the King, My lord, O King, this trespas be on me, and on my fathers house, and the King and his throne be giltlesse.
Koma mkazi wochokera ku Tekowayo anati kwa mfumu, “Mbuye wanga mfumu, kulakwa kukhale pa ine ndi banja la abambo anga ndipo mfumu ndi mpando wanu waufumu mukhale osalakwa.”
10 And the King sayde, Bring him to me that speaketh against thee, and he shall touche thee no more.
Mfumu inayankha kuti, “Ngati wina aliyense anene kanthu kwa iwe, umubweretse kwa ine, ndipo sadzakuvutitsanso.”
11 Then said she, I pray thee, let the King remember the Lord thy God, that thou wouldest not suffer many reuengers of blood to destroy, lest they slay my sonne. And he answered, As the Lord liueth, there shall not one heare of thy sonne fall to the earth.
Mkaziyo anati, “Mfumu ipemphe kwa Yehova Mulungu wake kuti aletse wobwezera imfa asaphenso wina kuti mwana wanga asawonongedwe.” Mfumu inati, “Pali Yehova wamoyo ngakhale tsitsi limodzi la pamutu pa mwana wako silidzathotholedwa.”
12 Then the woman said, I pray thee, let thine handmayde speake a worde to my lord the King. And he sayd, Say on.
Kenaka mkaziyo anati, “Lolani kuti wantchito wanu ayankhule mawu kwa inu mbuye wanga mfumu.” Iye anayankha kuti, “Yankhula.”
13 Then the woman sayde, Wherefore then hast thou thought such a thing against the people of God? or why doeth the King, as one which is faultie, speake this thing, that he will not bring againe his banished?
Mkaziyo anati, “Nʼchiyani tsono chimene mwaganiza kuchitira zimenezi anthu a Mulungu? Pamene mfumu yanena izi, kodi sikudzitsutsa yokha, pakuti mfumu sinayitanitse mwana amene anamupirikitsa?
14 For we must needes dye, and we are as water spilt on the ground, which cannot be gathered vp againe: neither doeth God spare any person, yet doeth he appoynt meanes, not to cast out from him, him that is expelled.
Koma poti madzi akatayika sawoleka, ndiye tonsefe tiyenera kufa ndithu. Koma Mulungu safuna kuti moyo wa munthu utayike kotero anakonza njira yakuti wopirikitsidwayo asakhale wotayikiratu.
15 Nowe therefore that I am come to speake of this thing vnto my lord the King, the cause is that the people haue made me afrayd: therefore thine handmayde sayd, Nowe will I speake vnto the King: it may be that the King will perfourme the request of his handmayde.
“Tsopano ine ndabwera kudzanena izi kwa inu mbuye wanga mfumu chifukwa anthu andichititsa mantha. Mdzakazi wanu anaganiza kuti, ‘Ndikayankhula kwa mfumu, mwina adzachita zimene mdzakazi wake adzamupempha.
16 For the King wil heare, to deliuer his handmayde out of the hande of the man that woulde destroy mee, and also my sonne from the inheritance of God.
Mwina mfumu idzavomereza kupulumutsa mdzakazi wake mʼdzanja la munthu amene akufuna kupha ine pamodzi ndi mwana wanga kutichotsa pa cholowa chimene Mulungu anatipatsa.’
17 Therefore thine handmaid sayd, The word of my lord the King shall now be comfortable: for my lorde the King is euen as an Angel of God in hearing of good and bad: therefore the Lord thy God be with thee.
“Ndipo tsopano mtumiki wanu akuti, ‘Lolani mawu a mbuye wanga mfumu abweretse mpumulo kwa ine, pakuti mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu pozindikira chabwino ndi choyipa. Yehova Mulungu wanu akhale nanu.’”
18 Then the King answered, and said vnto the woman, Hide not from me, I pray thee, the thing that I shall aske thee. And the woman sayde, Let my lord the King now speake.
Kenaka mfumu inati kwa mkaziyo, “Usandibisire chilichonse pondiyankha chimene ndidzakufunsa.” Mkaziyo anati, “Mbuye wanga mfumu yankhulani.”
19 And the King said, Is not the hand of Ioab with thee in all this? Then the woman answered, and sayd, As thy soule liueth, my lord the King, I will not turne to the right hande nor to the left, from ought that my lorde the King hath spoken: for euen thy seruant Ioab bade mee, and he put all these wordes in the mouth of thine handmayde.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi zimenezi sukuchita motsogozedwa ndi Yowabu?” Mkaziyo anayankha kuti, “Pali inu wamoyo, mbuye wanga mfumu, palibe munthu angakhotere kumanja kapena kumanzere pa chilichonse chimene mbuye wanga mfumu mwanena. Inde, ndi mtumiki wanu Yowabu amene wandilangiza ine kuchita zimenezi ndipo ndi amene anandipatsa mawu onsewa woti ine mtumiki wanu ndiyankhule.
20 For to the intent that I should chage the forme of speach, thy seruant Ioab hath done this thing: but my lord is wise according to the wisdome of an Angel of God to vnderstande all things that are in the earth.
Mtumiki wanu Yowabu anachita zimenezi kuti asinthe mmene zinthu zilili lero. Mbuye wanga muli ndi nzeru ngati za mngelo wa Mulungu. Mumadziwa zonse zimene zikuchitika mʼdziko.”
21 And the King sayde vnto Ioab, Beholde nowe, I haue done this thing: go then, and bring the yong man Absalom againe.
Mfumu inati kwa Yowabu, “Chabwino, ine ndichita zimenezi. Pita kamutenge Abisalomuyo.”
22 And Ioab fell to the grounde on his face, and bowed himselfe, and thanked the King. Then Ioab sayde, This day thy seruant knoweth, that I haue found grace in thy sight, my lord the King, in that the King hath fulfilled the request of his seruant.
Yowabu anawerama pansi kupereka ulemu kwa mfumu. Yowabuyo anati, “Lero mtumiki wanu wadziwa kuti wapeza chifundo pamaso panu, mbuye wanga mfumu, chifukwa mwavomera pempho lakeli.”
23 And Ioab arose, and went to Geshur, and brought Absalom to Ierusalem.
Choncho Yowabu anapita ku Gesuri ndipo anamubweretsa Abisalomu ku Yerusalemu.
24 And the King sayde, Let him turne to his owne house, and not see my face. So Absalom turned to his owne house, and saw not the Kings face.
Koma mfumu inati, “Iye apite ku nyumba yake; asaone nkhope yanga.” Kotero Abisalomu anapita ku nyumba yake ndipo sanakumane ndi mfumu.
25 Nowe in all Israel there was none to be so much praysed for beautie as Absalom: from the sole of his foote euen to the toppe of his head there was no blemish in him.
Mʼdziko lonse la Israeli munalibe munthu amene anayamikidwa chifukwa cha maonekedwe ake wokongola ngati Abisalomu. Kuyambira kumutu mpaka ku mapazi ake, analibe chilema.
26 And when he polled his head, (for at euery yeeres ende he polled it: because it was too heauie for him, therefore he polled it) he weyghed the heare of his head at two hundreth shekels by the Kings weight.
Nthawi ina iliyonse akamameta tsitsi lake, ankameta pamene layamba kumulemera. Akatero amaliyeza, ndipo limalemera makilogalamu awiri pa sikelo yaufumu.
27 And Absalom had three sonnes, and one daughter named Tamar, which was a fayre woman to looke vpon.
Abisalomu anali ndi ana aamuna atatu ndi wamkazi mmodzi. Mwana wamkazi dzina lake linali Tamara, ndipo anali mkazi wokongola kwambiri.
28 So Absalom dwelt the space of two yeres in Ierusalem, and saw not the Kings face.
Abisalomu anakhala zaka ziwiri mu Yerusalemu osaonekera kwa mfumu.
29 Therefore Absalom sent for Ioab to sende him to the King, but he would not come to him: and when he sent againe, he would not come.
Kenaka Abisalomu anatumiza mawu kwa Yowabu, kumutuma kuti apite kwa mfumu, koma Yowabu anakana kubwera. Kotero anatumizanso mawu kachiwiri, koma Yowabu anakananso.
30 Therefore he sayde vnto his seruants, Beholde, Ioab hath a fielde by my place, and hath barley therein: go, and set it on fire: and Absaloms seruants set the field on fire.
Tsono Abisalomu anati kwa antchito ake, “Taonani, munda wa Yowabu uli pafupi ndi wanga ndipo muli barele mʼmenemo. Pitani mukawutenthe mundawo.” Ndipo antchito a Abisalomu anawutentha mundawo.
31 Then Ioab arose, and came to Absalom vnto his house, and sayd vnto him, Wherefore haue thy seruants burnt my field with fire?
Ndipo Yowabu anapita ku nyumba ya Abisalomu ndipo anati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani antchito ako atentha munda wanga?”
32 And Absalom answered Ioab, Beholde, I sent for thee, saying, Come thou hither, and I wil send thee to the King for to say, Wherefore am I come from Geshur? It had bene better for me to haue bene there still: nowe therefore let mee see the Kings face: and if there be any trespasse in me, let him kill me.
Abisalomu anati kwa Yowabu, “Taona, ine ndinatumiza mawu kwa iwe ndipo ndinati, ‘Bwera kuno kuti ndikutume kwa mfumu kukafunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani ine ndinabwera kuchokera ku Gesuri? Zikanakhala bwino ndikanakhala komweko!’ Tsono pano ndikufuna kuonana ndi mfumu, ndipo ngati ndili olakwa mfumuyo indiphe.’”
33 Then Ioab came to the King, and told him: and he called for Absalom, who came to the King, and bowed himselfe to the grounde on his face before the King, and the King kissed Absalom.
Choncho Yowabu anapita kwa mfumu ndipo anayiwuza zimenezi. Ndipo mfumu inamuyitanitsa Abisalomu, ndipo analowa nawerama kugunditsa nkhope yake pansi pamaso pa mfumu. Tsono mfumu inapsompsona Abisalomu.

< 2 Samuel 14 >