< 2 Chronicles 10 >

1 Then Rehoboam went to Shechem: for to Sheche came all Israel to make him king.
Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse anapita kumeneko kuti akamulonge ufumu.
2 And when Ieroboam the sonne of Nebat heard it, (which was in Egypt, whither he had fled from the presence of Salomon the King) he returned out of Egypt.
Yeroboamu mwana wa Nebati atamva zimenezi (Iye anali ku Igupto, kumene anapita pothawa mfumu Solomoni) anabwerako kuchokera ku Igupto.
3 And they sent and called him: so came Ieroboam and all Israel, and communed with Rehoboam, saying,
Kotero anthu anakayitana Yeroboamu ndipo iye ndi Aisraeli onse anapita kwa Rehobowamu ndi kumuwuza kuti,
4 Thy father made our yoke grieuous: nowe therefore make thou the grieuous seruitude of thy father, and his sore yoke, that he put vpon vs, lighter, and we will serue thee.
“Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma tsopano mutipeputsire ntchito yolemetsayi ndi goli lolemerali limene analiyika pa ife ndipo ifeyo tidzakutumikirani.”
5 And he sayde to them, Depart yet three dayes, then come againe vnto me. And the people departed.
Rehobowamu anayankha kuti, “Mukabwerenso pakapita masiku atatu.” Choncho anthuwo anachoka.
6 And King Rehoboam tooke counsel with the olde men that had stande before Salomon his father, while hee yet liued, saying, What counsell giue ye that I may answere this people?
Kenaka mfumu Rehobowamu anafunsira nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira abambo ake, Solomoni, pamene anali moyo. Iye anafunsa kuti, “Kodi inu mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu awa?”
7 And they spake vnto him, saying, If thou be kinde to this people, and please them, and speake louing words to them, they will be thy seruants for euer.
Iwo anayankha kuti, “Ngati inu muwakomera mtima anthu awa ndi kuwasangalatsa ndiponso kuwayankha mawu abwino, iwo adzakutumikirani nthawi zonse.”
8 But hee left the counsel of the ancient men that they had giuen him, and tooke counsell of the yong men that were brought vp with him, and waited on him.
Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakulu anamupatsa ndipo anakafunsira nzeru kwa anyamata amene anakula naye pamodzi komanso amamutumikira.
9 And he sayd vnto them, What counsel giue ye, that we may answere this people, which haue spoken to mee, saying, Make the yoke which thy father did put vpon vs, lighter?
Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ndi otani? Kodi tiwayankhe chiyani anthu amene akunena kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anayika pa ife?’”
10 And the yong men that were brought vp with him, spake vnto him, saying, Thus shalt thou answere the people that spake to thee, saying, Thy father made our yoke heauie, but make thou it lighter for vs: thus shalt thou say vnto them, My least part shalbe bigger then my fathers loines.
Anyamata amene anakula pamodzi naye anamuyankha kuti, “Anthu amene anena kwa inu kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma inu mupeputse goli lathu,’ muwawuze kuti, ‘Chala changa chachingʼono ndi chachikulu kuposa chiwuno cha abambo anga.
11 Now whereas my father did burden you with a grieuous yoke, I will yet increase your yoke: my father hath chastised you with roddes, but I will correct you with scourges.
Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
12 Then Ieroboam and all the people came to Rehoboam the third day, as the King had appointed saying, Come againe to me the third day.
Tsiku lachitatu Yeroboamu ndi anthu onse anabwerera kwa Rehobowamu monga ananenera mfumu kuti, “Mukabwerenso kwa ine pakapita masiku atatu.”
13 And the King answered them sharply: and King Rehoboam left the counsel of the ancient men,
Mfumu inawayankha mwankhanza, pokana malangizo a akuluakulu aja.
14 And spake to them after ye counsell of the yong men, saying, My father made your yoke grieuous, but I wil incease it: my father chastised you with rods, but I will correct you with scourges.
Iye anatsatira malangizo a anyamata ndipo anati, “Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
15 So the king hearkened not vnto the people: for it was the ordinance of God that the Lord might performe his saying, which hee had spoken by Ahiiah the Shilonite to Ieroboam the sonne of Nebat.
Kotero mfumu sinamvere anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Mulungu, kukwaniritsa mawu amene Yehova ananena kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
16 So when all Isarael sawe that the King would not heare them, the people answered the King, saying, What portion haue we in Dauid? for we haue none inheritance in the sonue of Ishai. O Israel, euery man to your tents: now see to thine owne house, Dauid. So all Israel departed to their tents.
Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kuwamvera, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, gawo lanji mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli! Pitani kwanu. Iwe Davide! Yangʼana banja lako.” Kotero Aisraeli onse anapita kwawo.
17 Howbeit Rehoboam reigned ouer the children of Israel, that dwelt in the cities of Iudah.
Koma Rehobowamu anakhala akulamulirabe Aisraeli amene amakhala mʼmizinda ya Yuda.
18 Then King Rehoboam sent Hadoram that was ouer the tribute, and the children of Israel stoned him with stones, that he died: then King Rehoboam made speede to get him vp to his charet, to flee to Ierusalem.
Mfumu Rehobowamu inatuma Hadoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli anamugenda miyala ndi kumupha. Koma mfumu Rehobowamu anakwera galeta lake ndi kuthawira ku Yerusalemu.
19 And Israel rebelled against the house of Dauid vnto this day.
Motero Israeli wakhala akuwukira banja la Davide mpaka lero lino.

< 2 Chronicles 10 >