< 1 Samuel 26 >

1 Againe the Ziphims came vnto Saul to Gibeah, saying, Doeth not Dauid hide him selfe in the hill of Hachilah before Ieshimon?
Anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ku Gibeya nati, “Davide akubisala ku phiri la Hakila, limene limayangʼanana ndi Yesimoni.”
2 Then Saul arose, and went downe to the wildernes of Ziph, hauing three thousand chosen men of Israel with him, for to seeke Dauid in the wildernesse of Ziph.
Choncho Sauli ananyamuka pamodzi ndi ankhondo ake 3,000 napita ku chipululu cha Zifi kukafunafuna Davide ku chipululuko.
3 And Saul pitched in the hill of Hachilah, which is before Ieshimon by the way side. Now Dauid abode in the wildernesse, and he sawe that Saul came after him into the wildernesse.
Sauli anamanga msasa wake mʼmbali mwa njira yopita ku phiri la Hakila moyangʼanana ndi Yesimoni. Koma Davide anali mʼchipululumo. Davide ataona kuti Sauli amamulondola mpaka kumeneko,
4 (For Dauid had sent out spies, and vnderstood, that Saul was come in very deede)
iye anatumiza anthu okazonda ndipo anapeza kuti Sauli wafikadi ndithu.
5 Then Dauid arose, and came to the place where Saul had pitched, and when Dauid beheld the place where Saul lay, and Abner the sonne of Ner which was his chiefe captaine, (for Saul lay in the fort, and the people pitched round about him)
Tsono Davide ananyamuka napita kumalo kumene Sauli anamanga misasa. Iye anaona pamene Sauli ndi Abineri mwana wa Neri mkulu wa ankhondo anagona. Sauli anagona mʼkati mwa tenti ndipo asilikali anagona momuzungulira.
6 Then spake Dauid, and said to Ahimelech the Hittite, and to Abishai the sonne of Zeruiah, brother to Ioab, saying, Who will go downe with me to Saul to the hoste? Then Abishai said, I will goe downe with thee.
Ndipo Davide anafunsa Ahimeleki Mhiti ndi Abisai mwana wa Zeruya, mʼbale wa Yowabu kuti, “Ndani adzapita nane ku msasa kwa Sauli?” Abisai anayankha kuti, “Ine ndidzapita nanu.”
7 So Dauid and Abishai came downe to the people by night: and beholde, Saul lay sleeping within the fort, and his speare did sticke in the ground at his head: and Abner and the people lay round about him.
Choncho Davide ndi Abisai anapita ku misasa ya ankhondowo usiku. Atafika anangopeza Sauli ali gone mu msasa wake mkondo wake atawuzika pansi pafupi ndi mutu wake, Abineri ndi ankhondo onse anali atagona momuzungulira.
8 Then saide Abishai to Dauid, God hath closed thine enemie into thine hande this day: now therefore, I pray thee, let me smite him once with a speare to the earth, and I will not smite him againe.
Abisai anawuza Davide kuti, “Lero Mulungu wapereka mdani wanu mʼmanja mwanu. Tsopano ndiloleni ndimukhomere pansi ndi mkondo wangawu kamodzinʼkamodzi. Sindimulasa kawiri.”
9 And Dauid sayde to Abishai, Destroy him not: for who can lay his hand on the Lordes anoynted, and be giltlesse?
Koma Davide anamuyankha Abisai kuti, “Usamuphe! Ndani adzapha wodzozedwa wa Yehova ndi kupezeka wosalakwa?
10 Moreouer Dauid said, As the Lord liueth, eyther the Lord shall smite him, or his day shall come to dye, or he shall descend into battel, and perish.
Davide anati, Pali Yehova wamoyo, Yehova mwini ndiye adzamukanthe, mwina tsiku lake lomwalira lidzafika, kapena adzapita ku nkhondo nakaphedwa komweko.
11 The Lord keepe mee from laying mine hand vpon the Lordes anointed: but, I pray thee, take now the speare that is at his head, and the pot of water, and let vs goe hence.
Koma Yehova andiletse kuti ndisapweteke wodzozedwa wa Yehova. Tsopano tingotenga mkondo umene uli ku mutu kwakewo ndi botolo la madzilo ndipo tizipita.”
12 So Dauid tooke the speare and the pot of water from Sauls head, and they gate them away, and no man saw it, nor marked it, neither did any awake, but they were all asleepe: for the Lord had sent a dead sleepe vpon them.
Motero Davide anatenga mkondo ndi botolo lamadzi zimene zinali ku mutu kwa Sauli ndipo anachoka. Palibe amene anaona zimenezi kapena kudziwa, ndipo palibenso amene anadzuka. Onse anali mʼtulo, chifukwa Yehova anawagonetsa tulo tofa nato.
13 Then Dauid went vnto the other side, and stoode on the toppe of an hill a farre off, a great space being betweene them.
Pambuyo pake Davide anadutsa nakakwerera mbali ina ya phiri, ndi kuyimirira pamwamba pa phiri patali. Pakati pawo panali mpata waukulu.
14 And Dauid cryed to the people, and to Abner the sonne of Ner, saying, Hearest thou not, Abner? Then Abner answered, and said, Who art thou that cryest to the King?
Davide anayitana gulu lankhondo ndi Abineri mwana wa Neri nawafunsa kuti, “Kodi sundiyankha ine Abineri?” Abineri anayankha kuti, “Ndiwe yani amene ukuyitana mfumu?”
15 And Dauid said to Abner, Art not thou a man? and who is like thee in Israel? wherefore then hast thou not kept thy lorde the King? for there came one of the folke in to destroy the King thy lord.
Davide anamufunsa Abineri kuti, “Kodi sindiwe mwamuna? Ndipo wofanana nawe ndani mu Israeli? Nʼchifukwa chiyani sunateteze mbuye wako mfumu? Munthu wina anabwera kumeneko.
16 This is not well done of thee: as the Lord liueth, ye are worthy to dye, because ye haue not kept your master the Lordes Anointed: and now see where the Kings speare is, and the pot of water that was at his head.
Chimene wachita iwe si chabwino. Pali Yehova wamoyo iwe ndi asilikali ako muyenera kufa chifukwa simunateteze mbuye wanu, wodzozedwa wa Yehova. Tayangʼanayangʼana. Uli kuti mkondo wa mfumu ndi botolo lamadzi zimene zinali kumutu kwa mfumu?”
17 And Saul knewe Dauids voyce, and sayde, Is this thy voyce, my sonne Dauid? And Dauid sayde, It is my voyce, my lorde O King.
Sauli anazindikira mawu a Davide ndipo anafunsa kuti, “Kodi amenewa ndi mawu ako Davide mwana wanga?” Davide anayankha, “Inde ndi anga, mbuye wanga mfumu.
18 And he sayde, Wherefore doeth my lorde thus persecute his seruant? for what haue I done? or what euill is in mine hand?
Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukundilonda ine mtumiki wanu? Kodi ine ndachita chiyani ndipo ndapezeka ndi cholakwa chotani?
19 Now therefore, I beseech thee, let my lord the King heare the wordes of his seruant. If the Lord haue stirred thee vp against me, let him smell the sauour of a sacrifice: but if the children of men haue done it, cursed be they before the Lord: for they haue cast me out this day from abiding in the inheritance of the Lord, saying, Goe, serue other gods.
Tsopano mbuye wanga mfumu tamverani mawu a mtumiki wanu. Ngati ndi Yehova wautsa mtima wanu kuti mundiwukire, ndiye alandire chipepeso. Koma ngati ndi anthu amene achita zimene, ndiye Yehova awatemberere popeza andipirikitsa lero kundichotsa mʼdziko la Yehova, namati, ‘Pita kapembedze milungu ina.’
20 Nowe therefore let not my blood fall to the earth before the face of the Lord: for the King of Israel is come out to seeke a flea, as one would hunt a partridge in the mountaines.
Tsopano musalole kuti magazi anga akhetsedwe kutali ndi Yehova pakuti mfumu ya Israeli yatuluka kudzafunafuna ine nsabwe, monga mmene munthu asakira nkhwali ku mapiri.”
21 Then sayde Saul, I haue sinned: come againe, my sonne Dauid: for I will doe thee no more harme, because my soule was precious in thine eyes this day: behold, I haue done foolishly, and haue erred exceedingly.
Ndipo Sauli anati, “Ine ndachimwa. Bwerera mwana wanga Davide. Sindidzakuchitanso choyipa popeza lero wauwona moyo wanga ngati wamtengowapatali. Taona, ndachita zauchitsiru ndipo ndachimwa kwambiri.”
22 Then Dauid answered, and saide, Beholde the Kings speare, let one of the yong men come ouer and set it.
Davide anayankha kuti, “Nawu mkondo wanu, mfumu. Tumani mmodzi wa anyamata anu abwere adzatenge.
23 And let the Lord rewarde euery man according to his righteousnesse and faithfulnesse: for the Lord had deliuered thee into mine handes this day, but I woulde not lay mine hand vpon the Lords anointed.
Yehova amadalitsa munthu aliyense wolungama ndi wokhulupirika. Yehova anakuperekani lero mʼmanja mwanga, koma ine sindinakhudze wodzozedwa wa Yehova.
24 And beholde, like as thy life was much set by this day in mine eyes: so let my life be set by in the eyes of the Lord, that he may deliuer me out of all tribulation.
Monga momwe ine lero ndachitira kuwuyesa moyo wanu ngati wamtengowapatali, momwemonso Yehova awuyese moyo wanga wamtengowapatali ndipo andipulumutse mʼmavuto anga onse.”
25 Then Saul said to Dauid, Blessed art thou, my sonne Dauid: for thou shalt doe great things, and also preuaile. So Dauid went his way, and Saul returned to his place.
Ndipo Sauli anawuza Davide kuti, “Yehova akudalitse iwe Davide mwana wanga. Udzachita zinthu zazikulu ndipo udzapambana.” Choncho Davide anayenda njira yake ndipo Sauli anabwerera kwawo.

< 1 Samuel 26 >