< 1 Chronicles 2 >

1 These are the sonnes of Israel, Reuben, Simeon, Leui and Iudah, Isshachar, and Zebulun,
Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
2 Dan, Ioseph, and Beniamin, Naphtali, Gad, and Asher.
Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
3 The sonnes of Iudah, Er, and Onan, and Shelah. these three were borne to him of ye daughter of Shua the Canaanite: but Er the eldest sonne of Iudah was euil in the sight of the Lord, and he slew him.
Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
4 And Thamar his daughter in law bare him Pharez, and Zerah: so al the sonnes of Iudah were fiue.
Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
5 The sonnes of Pharez, Hezron and Hamul.
Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
6 The sonnes also of Zerah were Zimri, and Ethan, and Heman, and Calcol, and Dara, which were fiue in all.
Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
7 And the sonne of Carmi, Achar that troubled Israel, transgressing in the thing excommunicate.
Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
8 The sonne also of Ethan, Azariah.
Mwana wa Etani anali Azariya.
9 And the sonnes of Hezron that were borne vnto him, Ierahmeel, and Ram and Chelubai.
Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
10 And Ram begate Aminadab, and Aminadab begate Nahshon prince of the children of Iudah,
Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
11 And Nahshon begate Salma, and Salma begate Boaz,
Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
12 And Boaz begate Obed, and Obed begate Ishai,
Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
13 And Ishai begate his eldest sonne Eliab, and Abinadab the second, and Shimma the third,
Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
14 Nathaneel the fourth, Raddai the fift,
wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
15 Ozem the sixt, and Dauid the seuenth.
wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
16 Whose sisters were Zeruiah and Abigail. And the sonnes of Zeruiah, Abishai, and Ioab, and Asahel.
Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
17 And Abigail bare Amasa: and the father of Amasa was Iether an Ishmeelite.
Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
18 And Caleb the sonne of Hezron begate Ierioth of Azubah his wife, and her sonnes are these, Iesher, and Shobab, and Ardon.
Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
19 And when Azubah was dead, Caleb tooke vnto him Ephrath, which bare him Hur.
Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
20 And Hur begate Vri, and Vri begate Bezaleel.
Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
21 And afterward came Hezron to the daughter of Machir the father of Gilead, and tooke her when hee was threescore yere olde, and shee bare him Segub.
Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
22 And Segub begate Iair, which had three and twentie cities in the land of Gilead.
Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
23 And Gesthur with Aram tooke the townes of Iair from them, and Kenath and the townes thereof, euen threescore cities. All these were the sonnes of Machir the father of Gilead.
(Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
24 And after that Hezron was dead at Caleb Ephratah, then Abiah Hezrons wife bare him also Ashur the father of Tekoa.
Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
25 And ye sonnes of Ierahmeel the eldest sone of Hezron were Ram the eldest, then Bunah, and Oren and Ozen and Ahiiah.
Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
26 Also Ierahmeel had another wife named Atarah, which was the mother of Onam.
Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
27 And the sonnes of Ram the eldest sonne of Ierahmeel were Maaz, and Iamin and Ekar.
Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
28 And the sonnes of Onam were Shammai and Iada. And the sonnes of Shammai, Nadab and Abishur.
Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
29 And the name of the wife of Abishur was called Abiahil, and shee bare him Ahban and Molid.
Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
30 The sonnes also of Nadab were Seled and Appaim: but Seled died without children.
Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
31 And the sonne of Appaim was Ishi, and the sonne of Ishi, Sheshan, and the sonne of Sheshan, Ahlai.
Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
32 And the sonnes of Iada the brother of Shammai were Iether and Ionathan: but Iether dyed without children.
Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
33 And the sonnes of Ionathan were Peleth and Zaza. These were the sonnes of Ierahmeel.
Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
34 And Sheshan had no sonnes, but daughters. And Sheshan had a seruant that was an Egyptian named Iarha.
Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
35 And Sheshan gaue his daughter to Iarha his seruant to wife, and she bare him Attai.
Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
36 And Attai begate Nathan, and Nathan begate Zabad,
Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
37 And Zabad begate Ephlal, and Ephlal begate Obed,
Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
38 And Obed begate Iehu, and Iehu begate Azariah,
Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
39 And Azariah begate Helez, and Helez begate Eleasah,
Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
40 And Eleasah begate Sisamai, and Sisamai begate Shallum,
Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
41 And Shallum begate Iekamiah, and Iekamiah begate Elishama.
Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
42 Also the sonnes of Caleb the brother of Ierahmeel, were Mesha his eldest sonne, which was the father of Ziph: and the sonnes of Mareshah the father of Hebron.
Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
43 And the sonnes of Hebron were Korah and Tappuah, and Rekem and Shema.
Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
44 And Shema begate Raham the father of Iorkoam: and Rekem begate Shammai.
Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
45 The sonne also of Shammai was Maon: and Maon was the father of Beth-zur.
Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
46 And Ephah a concubine of Caleb bare Haran and Moza, and Gazez: Haran also begate Gazez.
Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
47 The sonnes of Iahdai were Regem, and Iotham, and Geshan, and Pelet, and Ephah, and Shaaph.
Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
48 Calebs concubine Maachah bare Sheber and Tirhanah.
Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
49 She bare also Shaaph, the father of Madmannah, and Sheua the father of Machbenah, and the father of Gibea. And Achsah was Calebs daughter.
Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
50 These were the sonnes of Caleb the sone of Hur the eldest sonne of Ephrathah, Shobal the father of Kiriath-iearim.
Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
51 Salma the father of Beth-lehem, and Hareph the father of Beth-gader.
Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 And Shobal the father of Kiriath-iearim had sonnes, and he was the ouerseer of halfe Hammenoth.
Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
53 And the families of Kiriath-iearim were the Ithrites, and the Puthites, and the Shumathites, and ye Mishraites of them came the Zarreathites, and the Eshtaulites.
ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
54 The sonnes of Salma of Beth-lehem, and the Netophathite, the crownes of the house of Ioab, and halfe the Manahthites and the Zorites.
Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
55 And the families of the Scribes dwelling at Iabez, the Tirathites, the Shimmeathites, the Shuchathites, which are the Kenites, that came of Hammath the father of the house of Rechab.
ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.

< 1 Chronicles 2 >