< 1 Chronicles 16 >

1 So they brought in the Arke of God, and set it in the middes of the Tabernacle that Dauid had pitched for it, and they offred burnt offrings and peace offrings before God.
Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.
2 And when Dauid had made an ende of offering the burnt offering and the peace offerings, hee blessed the people in the Name of the Lord.
Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.
3 And he dealt to euery one of Israel both man and woman, to euery one a cake of breade, and a piece of flesh, and a bottel of wine.
Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.
4 And he appointed certaine of the Leuites to minister before the Arke of the Lord, and to rehearse and to thanke and prayse the Lord God of Israel:
Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.
5 Asaph the chiefe, and next to him Zechariah, Ieiel, and Shemiramoth, and Iehiel, and Mattithiah, and Eliab, and Benaiah, and Obed Edom, euen Ieiel with instruments, violes and harpes, and Asaph to make a sound with cymbales,
Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,
6 And Benaiah and Iahaziel Priestes, with trumpets continually before the Arke of the couenant of God.
ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.
7 Then at that time Dauid did appoint at the beginning to giue thankes to the Lord by the hand of Asaph and his brethren.
Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:
8 Praise the Lord and call vpon his Name: declare his workes among the people.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
9 Sing vnto him, sing praise vnto him, and talke of all his wonderfull workes.
Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando; nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
10 Reioyce in his holy Name: let the hearts of them that seeke the Lord reioyce.
Nyadirani dzina lake loyera; ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
11 Seeke the Lord and his strength: seeke his face continually.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi zonse.
12 Remember his marueilous workes that he hath done, his wonders, and the iudgements of his mouth,
Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita, zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
13 O seede of Israel his seruant, O the children of Iaakob his chosen.
inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.
14 He is the Lord our God: his iudgements are throughout all the earth.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
15 Remember his couenant for euer, and the worde, which hee commanded to a thousand generations:
Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse, mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
16 Which he made with Abraham, and his othe to Izhak:
pangano limene anachita ndi Abrahamu, lonjezo limene analumbira kwa Isake.
17 And hath confirmed it to Iaakob for a Law, and to Israel for an euerlasting couenant,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo, kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
18 Saying, To thee will I giue the land of Canaan, the lot of your inheritance.
“Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani monga cholowa chimene udzachilandira.”
19 When ye were fewe in number, yea, a very fewe, and strangers therein,
Ali anthu owerengeka, ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
20 And walked about from nation to nation, and from one kingdome to another people,
iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina, ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
21 He suffered no man to do them wrong, but rebuked Kings for their sakes, saying,
Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze; chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
22 Touch not mine anoynted, and doe my Prophets no harme.
“Musakhudze odzozedwa anga; musawachitire choyipa aneneri anga.”
23 Sing vnto the Lord all the earth: declare his saluation from day to day.
Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi; lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
24 Declare his glory among the nations, and his wonderful workes among all people.
Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse, ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
25 For the Lord is great and much to be praised, and hee is to bee feared aboue all gods.
Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda; Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
26 For all the gods of the people are idoles, but the Lord made the heauens.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake, koma Yehova analenga kumwamba.
27 Prayse and glory are before him: power and beautie are in his place.
Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake; mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
28 Giue vnto the Lord, ye families of the people: giue vnto the Lord glory and power.
Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
29 Giue vnto the Lord ye glory of his Name: bring an offring and come before him, and worship the Lord in the glorious Sanctuarie.
perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake. Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake; pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
30 Tremble ye before him, al the earth: surely the world shalbe stable and not moue.
Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi! Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
31 Let the heauens reioyce, and let the earth be glad, and let them say among the nations, The Lord reigneth.
Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere; anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
32 Let the sea roare, and all that therein is: Let the field be ioyfull and all that is in it.
Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo; minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
33 Let the trees of the wood then reioyce at the presence of the Lord: for he commeth to iudge the earth.
Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba, idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova, pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
34 Prayse the Lord, for hee is good, for his mercie endureth for euer.
Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
35 And say ye, Saue vs, O God, our saluation, and gather vs, and deliuer vs from the heathen, that we may prayse thine holy Name, and glorie in thy praise.
Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu, mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina, kuti tiyamike dzina lanu loyera, kuti tikutamandeni.”
36 Blessed be the Lord God of Israel for euer and euer: and let all people say, So be it, and praise the Lord.
Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”
37 Then he left there before the Arke of the Lordes couenant Asaph and his brethren to minister continually before the Arke, that which was to be done euery day:
Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.
38 And Obed Edom and his brethren, three score and eight: and Obed Edom the sonne of Ieduthun, and Hosah were porters.
Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.
39 And Zadok the Priest and his brethren the Priestes were before the Tabernacle of ye Lord, in the hie place that was at Gibeon,
Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni
40 To offer burnt offrings vnto the Lord, vpon the burnt offring altar continually, in the morning and in the euening, euen according vnto all that is written in the law of the Lord, which hee commanded Israel.
kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.
41 And with them were Heman, and Ieduthun, and the rest that were chosen (which were appointed by names) to praise the Lord, because his mercie endureth for euer.
Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
42 Euen with them were Heman and Ioduthun, to make a sound with the cornets and with the cymbales, with excellent instruments of musicke: and the sonnes of Ieduthun were at the gate.
Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.
43 And all the people departed, euerie man to his house: and Dauid returned to blesse his house.
Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.

< 1 Chronicles 16 >