< Psalms 99 >

1 The Lord reigns; let the nations tremble! He sits on his throne above the cherubim; let the earth shake!
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 The Lord rules supreme in Zion, he is sovereign over all the nations.
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Let them praise his greatness, and respect him for who he is—for he is holy,
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 having kingly power. You love justice; you make impartial decisions. You have made sure everything is done in fairness and according to what's right.
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Give respect to the Lord our God! Bow down at his feet, for he is holy!
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Moses and Aaron were among his priests; Samuel also prayed to him. They called out to the Lord for help, and he answered them.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 He spoke to the people from the pillar of cloud, and they kept the laws and decrees he gave them.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 Lord our God, you answered them. You were a forgiving God to them, but you punished them when they did wrong.
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Honor the Lord our God, and worship at his holy mountain. For the Lord our God is holy!
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

< Psalms 99 >