< Psalms 48 >

1 For the music director. A psalm of the sons of Korah. The Lord is supreme! He deserves praise in the city of our God on his holy mountain.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Mount Zion is high and beautiful, bringing happiness to all the earth; on the northern side is the city of the great King.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 God himself is in the city's fortresses; he is recognized as its defender.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 Look at what happened when foreign kings joined forces and came to attack the city.
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 As soon as they saw it they were astonished and ran away terrified.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 They shook all over, and were in agonizing pain like a woman giving birth,
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 just as the strong east wind wrecks the ships from Tarshish.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 Just as we had heard, but now we have seen the city of the Lord Almighty. This is the city of our God; he makes it secure forever. (Selah)
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 God, we recall your trustworthy love as we worship in the Temple.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 As is fitting for your reputation, God, praises to you stretch all around the world. What you do is always right!
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Let the people of Mount Zion be glad; let the people of Judah celebrate because your judgments are always fair!
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Go and take a look at Zion. Count the towers as you walk around.
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Inspect the fortifications. Examine the citadels, so you can describe everything to the next generation, telling them:
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 “This is who our God is. He is our God forever and ever. He himself will lead us until the very end.”
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

< Psalms 48 >