< Psalms 29 >

1 A psalm of David. Honor the Lord, children of God, honor his glory and strength.
Salimo la Davide. Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
2 Honor the Lord for his glorious character, bow in reverence to the Lord in his brilliant holiness.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake, pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.
3 The Lord's voice sounds over the sea. The God of glory thunders. The Lord thunders over the vast ocean.
Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi; Mulungu waulemerero abangula, Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.
4 The Lord's voice is powerful; the Lord's voice is majestic;
Liwu la Yehova ndi lamphamvu; liwu la Yehova ndi laulemerero.
5 the Lord's voice shatters the cedars, even breaking the cedars of Lebanon.
Liwu la Yehova limathyola mikungudza; Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.
6 He makes the mountains of Lebanon skip like a calf, and Mount Hermon like a young wild ox.
Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe, Siriyoni ngati mwana wa njati:
7 The Lord's voice blazes out like lightning flashes.
Liwu la Yehova limakantha ngati kungʼanima kwa mphenzi.
8 The Lord's voice causes an earthquake in the desert; the desert of Kadesh shakes.
Liwu la Yehova limagwedeza chipululu; Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.
9 The Lord's voice makes the pregnant deer go into labor; it strips bare the forests. In his Temple all the worshipers shout, “Glory!”
Liwu la Yehova limapindapinda mibawa ndi kuyeretsa nkhalango. Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”
10 The Lord sits on his throne above the floodwaters; the Lord is the eternal King.
Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira, Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.
11 The Lord gives strength to his people; the Lord blesses them with peace.
Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake; Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

< Psalms 29 >