< Psalms 14 >

1 For the music director. A psalm of David. Only fools tell themselves, “God doesn't exist.” They are completely immoral; they commit terrible sins; not a single one of them does anything good.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
2 The Lord watches from heaven to see whether anyone understands—if there's anyone who wants to come to God.
Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
3 They have all gone their own way, they are totally depraved; none of them does anything good, not even one.
Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
4 Won't these people who do evil ever learn? They consume my people as if they were eating bread, and refuse to pray to the Lord.
Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
5 Look, they will become terrified, because God is with those who live right.
Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
6 The wicked dismiss the plans of the poor people, but the Lord looks after them.
Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
7 If only the Lord's salvation would come from Zion! When the Lord restores his people, the people of Jacob will celebrate, and the people of Israel will be glad.
Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!

< Psalms 14 >