< Psalms 135 >

1 Praise the Lord! Praise the Lord's reputation! Praise the Lord, all you servants of the Lord
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 who worship in the house of the Lord, in the courts of our God.
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Praise the Lord, for the Lord is good; sing praises to his character because it is wonderful!
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 For the Lord has chosen Jacob for himself; Israel as his very own.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 I know how great the Lord is—our Lord is greater than all gods.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 The Lord does whatever he wants throughout heaven and earth, on the seas and in the ocean depths.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 He causes the clouds to rise all over the earth, he makes lightning flash and give rain, he sends the winds from his storehouses.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 He struck down the firstborn of Egypt, both human and animal.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 He did wonderful miracles among you in Egypt, against Pharaoh and all his servants.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 He struck down many nations, he killed powerful kings, such as
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihon, king of the Amorites, Og, king of Bashan, and all the kings who ruled in Canaan.
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 He handed over their lands to Israel, his special people, for them to possess.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Your reputation, Lord, stands forever; you, Lord, are remembered for all generations.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 The Lord will vindicate his people; he will show compassion to those who follow him.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 The idols of the foreign nations are only objects of silver and gold, made by human hands.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 They have mouths, but can't speak; they have eyes, but can't see.
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 They have ears, but can't hear; they can't even breathe!
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Those who make idols will become just like them, and so will everyone who trusts in them.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 People of Israel, praise the Lord! Descendants of Aaron, praise the Lord!
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Levites, praise the Lord! Everyone who worships the Lord, praise the Lord!
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Praise the Lord from Zion, for he lives in Jerusalem! Praise the Lord!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalms 135 >