< Psalms 116 >

1 I love the Lord because he listens to me, he hears my calls for help.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Because he pays attention to what I say I will pray to him as long as I live.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 I was caught in the snares of death; I was trapped by terrors of the grave. All I experienced was suffering and grief. (Sheol h7585)
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
4 Then I cried out to the Lord, “Lord, please save me!”
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 The Lord is so kind and good! Our God is so compassionate!
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 The Lord takes care of those who are powerless; when I was brought down he saved me.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 I can once again be at peace because the Lord has been good to me.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 For you have saved me from death, my eyes from crying, and my feet from stumbling.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Now I can walk with the Lord in the land of the living.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 I trusted in you, so I told you, “I'm suffering terribly!”
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 I was so upset that I said, “Everyone's a liar!”
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 What can I give the Lord in return for all he's done for me?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 I will lift up the cup of salvation and worship the Lord.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 I will keep my promises to the Lord so everyone can see.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 It hurts the Lord when those who trust in him die.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Lord, I really am your slave, serving you as my mother served you before me, yet you have set me free.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 I will offer a sacrifice of thanksgiving to you and I will worship you.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 I will keep my promises to the Lord so everyone can see,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 there in the house of the Lord, right in Jerusalem. Praise the Lord!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Psalms 116 >