< Proverbs 30 >

1 These are the words of Agur, son of Jakeh. An oracle. This is what the man says, God, I'm really tired, I'm worn out.
Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa: Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa. Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.
2 I'm so stupid I'm not really a man; I can't even think like a human being.
“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse; ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.
3 I have not learned wisdom; I have no knowledge of the Holy One.
Sindinaphunzire nzeru, ndipo Woyerayo sindimudziwa.
4 Who has gone up to heaven, and come down? Who holds the winds in the palm of his hands? Who has wrapped up the waters in his cloak? Who has set the earth's boundaries? What is his name, and what is his son's name? Are you sure you don't know?
Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako? Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake? Ndani anamanga madzi mʼchovala chake? Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi? Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa! Ndipo mwana wake dzina lake ndani?
5 Every word God says has been proved true. He defends everyone who comes to him for protection.
“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika; Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.
6 Don't add anything to his words, or he will criticize you and you'll be shown to be a liar.
Usawonjezepo kanthu pa mawu ake, kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”
7 God, I want to request two things from you. Please don't refuse to let me have them before I come to die.
“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri musandimane zimenezo ndisanafe:
8 Keep me from being false, help me not to tell lies. Don't make me poor or rich; just provide me with the food I need.
Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo. Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma. Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku
9 Otherwise if I have plenty of money, I may give up on you, saying, “Who is the Lord?” while if I'm poor I may steal and bring the name of my God into disrepute.
kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani, nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’ Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba, potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”
10 Don't slander a servant to his master, or he will curse you and you'll suffer for it.
“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”
11 There are some who curse their fathers and do not bless their mothers.
“Alipo ena amene amatemberera abambo awo, ndipo sadalitsa amayi awo.
12 There are some who see themselves as pure but they're still filthy—they have not been washed.
Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima komatu sanachotse zoyipa zawo.
13 There are some who think themselves so high and mighty, and who look down on others.
Pali ena ndi odzitukumula kwambiri, amene amakweza zikope modzitukumula.
14 There are some who have teeth like swords, incisors like knives, ready to devour the poor from the earth, the needy from society.
Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi. Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”
15 The leech has two daughters who cry out, “Give me! Give me!” There are three things that are never satisfied, four that never say, “Enough!”:
“Msundu uli ndi ana aakazi awiri iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’” “Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta, zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’
16 The grave, the womb that doesn't become pregnant, the earth thirsty for water, and the fire that never says, “Enough!” (Sheol h7585)
Manda, mkazi wosabala, nthaka yosakhuta madzi ndiponso moto womangoyakirayakira!” (Sheol h7585)
17 People who ridicule their fathers and despise obedience to the mother will have their eyes pecked out by wild ravens and eaten by young vultures.
Aliyense amene amanyoza abambo ake, ndi kunyozera kumvera amayi ake, makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.
18 These three things are amazingly hard for me, four things I just can't understand:
Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa, zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.
19 The way an eagle soars in the sky, the way a snake slides over a rock, the way a ship sails across the sea, the way a man and a woman fall in love.
Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga; mmene iyendera njoka pa thanthwe; mmene chiyendera chombo pa nyanja; ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.
20 This is the way of a woman who commits adultery: she eats, she wipes her mouth, and then says, “I haven't done anything wrong!”
Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo: Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”
21 Three things make the earth tremble, there are four things it can't support:
Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi, pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:
22 a slave becoming a king, a stupid person eating like a pig,
Kapolo amene wasanduka mfumu, chitsiru chimene chakhuta,
23 an unbearable woman getting married, and a maidservant taking her mistress's place.
mkazi wonyozeka akakwatiwa ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.
24 There are four things on earth that are small, but very wise:
Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi, komatu ndi zochenjera kwambiri:
25 Ants—they're not strong, but they work hard all summer storing up food.
Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu, komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;
26 Hyraxes—they don't have much power, but they make their homes in the rock.
mbira zili ngati anthu opanda mphamvu komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;
27 Locusts—they don't have a king, but they all march in line abreast.
dzombe lilibe mfumu, komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.
28 Lizards—you can catch them in your hands, but they live in the king's palace.
Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.
29 There are three things that are glorious to watch as they walk, four that look dignified as they move:
“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya, pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:
30 The lion, supreme among wild animals, who isn't frightened of anything.
Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse, ndipo suthawa kanthu kalikonse.
31 The strutting starling, the male goat, and a king with his army.
Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna, ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.
32 If you have been foolishly boasting about yourself, or if you've been planning to do something wrong, stop and put your hand over your mouth.
“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha, kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa, ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!
33 Just as churning milk produces butter, and twisting someone's nose makes it bleed, so stirring up anger causes arguments.
Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa, ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka, ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

< Proverbs 30 >