< Proverbs 23 >

1 When you sit down for a meal with a ruler, look carefully at what is placed before you,
Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira, uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,
2 and cut down if you have a big appetite.
ngati ndiwe munthu wadyera udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.
3 Don't be greedy for his fancy food, for it's offered with deceptive motives.
Usasirire zakudya zake, pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.
4 Don't wear yourself out trying to get rich—be wise enough not to bother!
Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma, ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.
5 It disappears in the blink of an eye, suddenly growing wings and flying off into the sky like an eagle.
Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo. Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.
6 Don't accept meal invitations from miserly people; don't be greedy for their fancy food,
Usadye chakudya cha munthu waumbombo, usalakalake zakudya zake zokoma;
7 for what they're thinking inside is what they really are. They say, “Come on, eat and drink!”—but in their minds they don't really care about you.
paja iye ndi munthu amene nthawi zonse amaganizira za mtengo wake ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,” koma sakondweretsedwa nawe.
8 You'll vomit up the little pieces you've eaten, and your kind words of appreciation will be wasted.
Udzasanza zimene wadyazo ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.
9 Don't talk to stupid people because they'll ridicule your wise words.
Usayankhule munthu wopusa akumva, pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.
10 Don't move ancient boundary markers, and don't encroach on fields belonging to orphans,
Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,
11 for their Protector is powerful and he will plead their case against you.
paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu; iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.
12 Focus your mind on instruction; listen intently to words of knowledge.
Mtima wako uzikhala pa malangizo ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.
13 Don't keep from disciplining your children—a beating won't kill them.
Usaleke kumulangiza mwana; ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.
14 If you use physical correction you can save them from death. (Sheol h7585)
Ukamukwapula ndi tsatsa udzapulumutsa moyo wake. (Sheol h7585)
15 My son, if you think wisely then I'll be happy;
Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru, inenso mtima wanga udzakondwera.
16 I'll be delighted when you say what's right.
Mtima wanga udzakondwera pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.
17 Don't think enviously of sinners, but always remember to honor the Lord,
Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa, koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.
18 for there's definitely a future for you, and your hope will not be crushed.
Ndithu za mʼtsogolo zilipo ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.
19 Pay attention, my son, and be wise; make sure your mind concentrates on following the right way.
Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru, mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.
20 Don't join in with people who drink too much wine or who stuff themselves with meat.
Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.
21 For people who get drunk and overeat lose all they've got, and they spend so much time dozing that all they have left to wear is rags.
Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi ndipo aulesi adzavala sanza.
22 Pay attention to your father, and don't disregard your mother when she's old.
Mvera abambo ako amene anakubala, usanyoze amayi ako pamene akalamba.
23 Invest in truth—and don't sell it! Invest in wisdom, instruction, and understanding.
Gula choonadi ndipo usachigulitse; ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.
24 Children who do right make their fathers very happy; a wise son brings joy to his father.
Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu; Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Make your father and mother happy; bring joy to her who gave birth to you.
Abambo ndi amayi ako asangalale; amene anakubereka akondwere!
26 My son, give me your undivided attention, and cheerfully follow my example.
Mwana wanga, undikhulupirire ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.
27 A prostitute is like being trapped in a pit; an immoral woman is like getting stuck a narrow well,
Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama; ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.
28 Like a robber, she lies in wait ready to ambush men and make more of them unfaithful to their wives.
Amabisala ngati mbala yachifwamba, ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.
29 Who's in trouble? Who's in pain? Who's arguing? Who's complaining? Who's injured for no reason? Who's got bloodshot eyes?
Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni? Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo? Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?
30 —those who spend a long time drinking wine, those who are always trying some new cocktail.
Ndi amene amakhalitsa pa mowa, amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.
31 Don't let the look of wine tempt you—how red it is, how it sparkles in the cup, how smooth it feels as it goes down.
Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo, pamene akuwira mʼchikho pamene akumweka bwino!
32 In the end it bites like a serpent, it stings like a snake.
Potsiriza pake amaluma ngati njoka, ndipo amajompha ngati mphiri.
33 You'll hallucinate, seeing strange things, and your confused mind will make you say all kinds of craziness.
Maso ako adzaona zinthu zachilendo ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.
34 You'll stumble around like you're on the rolling ocean, you'll be tossed about like someone lying down at the top of a ship's mast, saying,
Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja, kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.
35 “People punched me, but it didn't hurt me; they beat me, but I didn't feel a thing. I've got to get up because I need another drink.”
Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe! Andimenya koma sindinamve kanthu! Kodi ndidzuka nthawi yanji? Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

< Proverbs 23 >