< Nahum 2 >

1 The one who scatters has come to attack you! Guard the fortresses! Watch the roads! Get yourselves ready! Call every soldier out!
Wodzathira nkhondo akubwera kudzalimbana nawe, Ninive. Tetezani malinga anu, dziyangʼanani ku msewu, konzekerani nkhondo, valani dzilimbe.
2 (For the Lord will restore the splendor of the people of Jacob as he will restore the splendor of Israel, for invaders have plundered them, and destroyed their land.)
Yehova adzabwezeretsa ulemerero wa Yakobo ngati ulemerero wa Israeli, ngakhale anthu owononga anawawononga kotheratu ndipo anawononganso mpesa wawo.
3 The shields of his chief soldiers are red; the warriors wear scarlet. His chariots flash like fire in the sunlight as he prepares for battle. Spears with their wooden shafts are held up and shaken.
Zishango za ankhondo ake ndi zofiira; asilikali ake avala zovala zofiirira. Zitsulo za pa magaleta zikunyezimira tsiku la kukonzekera kwake. Akuonetsa mikondo ya mkungudza yonoledwa.
4 Chariots race madly through the streets, rushing back and forth across the town squares. Bright as torches, they dash like lightning flashes.
Magaleta akuthamanga mʼmisewu akungothamangathamanga pa mabwalo. Akuoneka ngati miyuni yoyaka; akuthamanga ngati chingʼaningʼani.
5 He shouts orders to his officers. They stumble as they rush to attack the wall. The battering ram is set up.
Iye akuyitanitsa asilikali ake wolemekezeka, koma iwo akubwera napunthwa. Akuthamangira ku linga la mzinda; akuyimika chodzitchinjirizira pamalo pake.
6 The river gates are opened; the palace washes away.
Atsekula zipata zotchinga madzi a mu mtsinje ndipo nyumba yaufumu yagwa.
7 “Queen” Nineveh is stripped, and led away into exile, with her servant girls mourning like doves, and beating their breasts.
Zatsimikizika kuti mzinda utengedwa ndi kupita ku ukapolo. Akapolo aakazi akulira ngati nkhunda ndipo akudziguguda pachifuwa.
8 Nineveh is a leaky pool—its population is like water running away. “Stop! Stop” people shout, but nobody turns back.
Ninive ali ngati dziwe, ndipo madzi ake akutayika. Iwo akufuwula kuti, “Imani! Imani!” Koma palibe amene akubwerera.
9 Loot the silver! Loot the gold! There's an endless supply—an abundance of everything you could ever want.
Funkhani siliva! Funkhani golide! Katundu wake ndi wochuluka kwambiri, chuma chochokera pa zinthu zake zamtengowapatali!
10 Deserted, destroyed, devastated! Hearts faint, knees tremble, stomachs ache. Everyone's faces turn pale.
Iye wawonongedwa, wafunkhidwa ndipo wavulidwa! Mitima yasweka, mawondo akuwombana, anthu akunjenjemera ndipo nkhope zasandulika ndi mantha.
11 Where now is the lion's den? Where is the place where the young lions used to feed? Where is the lion, and the lioness, and the lion cub that were afraid of no one?
Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti, malo amene mikango inkadyetserako ana ake, kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako, ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 The lion tears apart meat for his cubs, and strangles prey for his lionesses. He fills his den with prey, his lair with carcasses.
Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake ndiponso kuphera nyama mkango waukazi, kudzaza phanga lake ndi zimene wapha ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
13 Watch out! For I am against you, declares the Lord Almighty. I will set fire to your chariots and they will go up in smoke. Your strong young men will be killed by the sword. I will stop you plundering other peoples. The demands of your ambassadors will no longer be heard.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikutsutsana nawe. Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo, ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono; sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi. Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”

< Nahum 2 >