< Leviticus 13 >

1 The Lord told Moses and Aaron,
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
2 “Anyone who has a swelling, a rash, or a spot on the skin that may be an infectious skin disease must be taken to Aaron the priest or to one of his descendants.
“Munthu akakhala ndi chithupsa, kapena mʼbuko, kapena chikanga pa thupi lake chimene chitha kusanduka nthenda ya khate, abwere naye munthuyo kwa Aaroni wansembe kapena kwa mmodzi mwa ana ake amene ndi ansembe.
3 The priest will inspect whatever is on the skin. If the hair there has turned white and if the issue seems to be more than something on the surface, it is a serious skin disease, and the priest who inspects it will declare the person unclean.
Tsono wansembe ayangʼanitsitse nthendayo pa khungupo, ndipo ngati ubweya wa pamalo pamene pali nthendapo wasanduka woyera, komanso kuti nthendayo yazama mʼkati kupitirira khungu, ndiye kuti nthendayo ndi khate. Wansembe akamuonetsetsa alengeze kuti ndi wodetsedwa.
4 But if the spot is only a white discoloration and doesn't seem to be more than superficial, and if the hair on the spot has not turned white, the priest will place the person in isolation for seven days.
Ngati chikanga cha pa khungulo chikuoneka choyera, ndipo kuya kwake sikukuonekera kuti kwapitirira khungu ndi ubweya wake pamalopo sunasanduke woyera, wansembe amuyike wodwalayo padera kwa masiku asanu ndi awiri.
5 On the seventh day the priest will conduct another inspection, and if he discovers that the spot hasn't changed and hasn't spread on the skin, the priest must place the person in isolation for another seven days.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso bwino wodwalayo. Ndipo ngati waona kuti nthendayo sinasinthe ndipo sinafalikire pa khungu, amuyikenso wodwalayo padera kwa masiku ena asanu ndi awiri.
6 On the seventh day after this the priest will inspect it again. If the spot has faded and has not spread on the skin, the priest will declare the person clean since it was a rash. They must wash their clothes and will be clean.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembeyo amuonenso bwino munthuyo, ndipo ngati nthendayo yazima ndi kusafalikira pa khungu, wansembe amutchule munthuyo kuti ndi woyera. Umenewo unali mʼbuko chabe. Choncho munthuyo achape zovala zake ndipo adzakhala woyera.
7 However, if the rash does spread after the person has been inspected by the priest and has been declared clean, the person must go back to be inspected again.
Koma ngati mʼbukowo ufalikira pakhungu atakadzionetsa kale kwa wansembe ndipo wansembeyo nʼkulengeza kuti munthuyo ndi woyeretsedwa, ndiye kuti apitenso kukadzionetsa kwa wansembeyo.
8 If the priest discovers that the rash has spread, he must declare the person unclean because it is certainly a skin disease.
Wansembe amuonetsetsenso munthuyo, ndipo ngati mʼbukowo wafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa ndi kuti nthendayo ndi khate.
9 Anyone who develops an infectious skin disease must be taken to the priest.
“Ngati munthu aliyense ali ndi nthenda ya pakhungu yoyipitsa thupi, wodwalayo abwere naye kwa wansembe.
10 The priest will inspect them, and if there is a white swelling on the skin and the hair there has turned white, and there is an open wound in the swelling,
Wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati ali ndi chithupsa chamaonekedwe woyera pa khungupo chimene chasandutsa ubweya wa pamalopo kukhala woyera, ndipo ngati pali zilonda pa chotupacho,
11 it is a serious skin disease and the priest must declare them unclean. He doesn't need to place the person in isolation because they are unclean.
limenelo ndi khate lachikhalire la pa khungu, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Asamutsekere munthu woteroyo pakuti ndi wodetsedwa kale.
12 However, if the skin disease affects all their skin so that it covers their skin from head to toe, everywhere the priest can see,
“Ndipo ngati, mʼkuona kwa wansembe, khate lija lafalikira pa khungu lonse moti lamugwira thupi lonse kuyambira kumutu mpaka kumapazi,
13 the priest shall inspect them, and if the disease has covered their entire body, he will declare the person clean. As it has all turned white, they are clean.
wansembe amuonetsetse munthuyo, ndipo ngati khatero lagwira thupi lake lonse, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Popeza kuti thupi lonse lasanduka loyera, munthuyo ndi woyeretsedwa.
14 But if when someone's inspected an open wound is found, they will be unclean.
Koma pa tsiku limene zilonda zidzaoneka pa iye, munthuyo adzakhala wodetsedwa.
15 When the priest discovers an open wound, he must declare the person unclean. The open wound is unclean; it is an infectious skin disease.
Wansembe aonetsetse zilondazo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zilondazo ndi zodetsedwa ndipo ili ndi khate.
16 But if the open wound heals and becomes white, the person must go back to the priest.
Koma zilondazo zikasinthika ndi kusanduka zoyera, munthuyo ayenera kupita kwa wansembe.
17 The priest will inspect them again, and if the wound has turned white, the priest is to declare the person clean; then they are clean.
Wansembe amuonetsetse ndipo ngati zilondazo zasanduka zoyera, wansembe amutchule wodwalayo kuti ndi woyera ndipo adzakhala woyera ndithu.
18 When a boil comes up on someone's skin and then it heals,
“Ngati pa khungu la munthu wodwalayo pali chithupsa chimene chinapola kale,
19 and a white swelling or a reddish-white spot appears in its place, they must show themselves to the priest.
ndipo pamalo pamene panali chithupsacho pakatuluka chotupa choyera kapena banga loyera mofiirira, munthuyo ayenera kukadzionetsa kwa wansembe.
20 The priest shall inspect it, and if it seems to be more than something on the surface, and if the hair there has turned white, the priest shall declare him unclean. It is a serious skin disease that has infected the boil.
Wansembe aonetsetse bwino ndipo ngati chikuoneka kuti chazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka woyera, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Imeneyo ndi nthenda ya khate imene yatuluka mʼchithupsacho.
21 However, if when the priest inspects it, it doesn't have white hair in it and doesn't seem to be more than superficial, and has faded, the priest is to place the person in isolation for seven days.
Koma ngati wansembe waonetsetsa napeza kuti palibe ubweya woyera ndipo chithupsacho sichinazame, koma chazimirira, wansembeyo amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
22 If then the spot has spread further on the skin, the priest will declare them unclean; it is a disease.
Ngati nthendayo ikufalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limeneli ndi khate.
23 But if the spot stays the same and doesn't spread, it's just the scar from the boil, and the priest will declare them clean.
Koma bangalo likakhala malo amodzi, wosafalikira, chimenecho ndi chipsera cha chithupsacho, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera.
24 If someone has a burn on their skin and where it's raw changes into a reddish-white or white spot,
“Munthu akakhala ndi bala lamoto pa khungu lake, ndipo chilonda cha balalo chikasanduka banga loyera mofiirira kapena loyera,
25 the priest must inspect it. If the hair in the spot has turned white and the spot seems to be more than something on the surface, it is a serious skin disease that has infected the burn, and the priest who inspects it will declare the person unclean. It is an infectious skin disease.
wansembe aonetsetse bangalo, ndipo ngati ubweya wa pa bangapo usanduka woyera, ndipo balalo lioneka kuti ndi lozama, limenelo ndi khate lomwe latuluka pa balalo. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate la pa khungu.
26 However, if when the priest inspects it, it doesn't have white hair in it and doesn't seem to be more than superficial, and has faded, the priest is to place the person in isolation for seven days.
Koma ngati wansembe waonetsetsa balalo ndipo palibe ubweya woyera, ndipo ngati balalo silinazame ndi kuti lazirala, wansembe amuyike padera wodwalayo kwa masiku asanu ndi awiri.
27 On the seventh day the priest will inspect the person again. If then the spot has spread further on the skin, the priest will declare them unclean; it is a serious skin disease.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe amuonenso wodwalayo, ndipo ngati bangalo lafalikira pa khungu, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Limenelo ndi khate.
28 But if the spot stays the same and hasn't spread on the skin, but has faded, it's the swelling from the burn, and the priest will declare them clean because it's just the scar from the burn.
Koma ngati bangalo likhala pa malo amodzi wosafalikira pa khungu, ndipo lazimirira, limenelo ndi thuza la bala lamoto, ndipo wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Chimenecho ndi chipsera chamoto.
29 If someone, man or woman, has a sore on the head or chin,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi nthenda kumutu kapena ku chibwano,
30 the priest shall inspect it, and if it appears to be more than superficial and the hair in it has become pale and thin, the priest must declare them unclean; it is an infection producing scabs, a serious disease of the head or chin.
wansembe aonetsetse balalo ndipo likaoneka kuti lazama, ndipo ubweya wa pamalopo wasanduka wachikasu ndi wonyololoka, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa. Zimenezo ndi mfundu zonyerenyetsa, khate lakumutu kapena ku chibwano.
31 However, if the priest inspects the scabby infection and it doesn't seem to be more than superficial and has no pale hair in it, the priest is to place the person in isolation for seven days.
Koma wansembe akaonetsetsa mfundu zonyerenyetsazo, ndipo zikaoneka kuti sizinazame ndi kuti palibe ubweya wakuda, wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku asanu ndi awiri.
32 On the seventh day the priest will inspect the person again and if the scabby infection has not spread and there is no pale hair in it, and it doesn't seem to be more than superficial,
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo, ndipo ngati sizinafalikire ndipo palibe ubweya wachikasu pamalopo ndiponso sizinazame,
33 then the person must shave themselves except for the scaly area. The priest is to place the person in isolation for another seven days.
wodwalayo ametedwe, koma pamene pali mfunduyo pasametedwe. Wansembe amuyike padera munthuyo kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
34 On the seventh day the priest will inspect the scabby infection, and if it has not spread on the skin and doesn't seem to be more than superficial, the priest is to pronounce the person clean. They must wash their clothes and will be clean.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri wansembe aonetsetsenso mfundu zonyerenyetsazo ndipo ngati sizinafalikire pa khungu ndi kuti sizinazame, wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyera. Tsono achape zovala zake, ndipo adzakhala woyera.
35 However, if the scabby infection has spread on the skin after been declared clean,
Koma mfundu zonyerenyetsazo zikafalikira pa khungu, wansembe atalengeza kuti ndi woyera,
36 the priest must inspect them, and if the scabby infection has indeed spread on the skin, the priest doesn't need to check for pale hair; the person is unclean.
wansembe amuonetsetsenso wodwalayo ndipo ngati mfunduzo zafalikira pa khungu, iye asalabadirenso zoyangʼana ngati ubweya uli wachikasu. Munthuyo ndi wodetsedwa.
37 But if the priest sees that the scabby infection hasn't changed, and black hair has grown in it, then it has healed. The person is clean, and the priest must declare it.
Koma ngati wansembe waonetsetsa kuti mfunduzo sizinasinthe ndipo ubweya wakuda wamera pa mfundupo, ndiye kuti wodwalayo wachira. Tsono wansembe alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa.
38 If someone, man or woman, has white spots on the skin,
“Mwamuna kapena mkazi akakhala ndi mawanga woyera pa khungu,
39 the priest shall inspect them, and if the spots appear a dull white, it's just a rash that has developed on the skin; the person is clean.
wansembe aonetsetse mawangawo, ndipo ngati ali otuwa, ndiye kuti ndi mibuko chabe yotuluka pa khungu. Munthuyo ndi woyera.
40 If a man loses his hair and goes bald, he is still clean.
“Tsitsi la munthu likayoyoka kumutu ndiye kuti ndi dazi limenelo koma munthuyo ndi woyeretsedwa.
41 If he has a receding hairline and he goes bald on his forehead, he is still clean.
Ngati tsitsi lake layoyoka chapamphumi ndiye kuti ndi dazi la pa chipumi limenelo koma munthuyo ndi woyera.
42 But if a reddish-white sore appears on his bald head or forehead, it is an infectious disease developing.
Koma ngati pa dazi la pamutu kapena la pa chipumi pakhala chithupsa choyera mofiirira, ndiye kuti ndi khate limenelo lochokera mu dazi la pamutu lija kapena pa chipumi lija.
43 The priest must inspect him, and if the swelling of the sore on his bald head or forehead looks reddish-white like a skin disease,
Tsono wansembe amuonetsetse wodwalayo ndipo ngati chithupsa cha pa dazi lapankhongo kapena pa dazi lapachipumicho ndi choyera mofiirira monga nthenda ya khate imaonekera,
44 then he is has an infectious disease; he is unclean. The priest must declare him unclean because of the infection on his head.
ndiye kuti munthuyo ali ndi khate, motero ndi wodetsedwa. Wansembe alengeze kuti munthuyo ndi wodetsedwa chifukwa cha chithupsa cha pamutu pakepo.
45 Anyone who has such diseases must wear clothes that are torn and let their hair remain uncombed. They must cover their faces and shout out, ‘Unclean, unclean!’
“Munthu wa khate lotere avale sanza, tsitsi lake alilekerere, aphimbe mlomo wake wapamwamba ndipo azifuwula kuti, ‘Ndine wodetsedwa, ndine wodetsedwa!’
46 They remain unclean as long as the infection lasts. They have to live alone somewhere outside the camp.
Munthu wodwalayo adzakhala wodetsedwa kwa nthawi yonse imene ali ndi nthendayo. Iye ayenera kumakhala payekha kunja kwa msasa.
47 The following regulations relate to any material that becomes affected by mold, such as wool or linen clothing,
“Nsalu iliyonse ikakhala ndi nguwi,
48 anything woven or knitted made from linen or wool, or anything made of leather:
kaya ndi chovala chopangidwa ndi nsalu yathonje kapena yaubweya, yoluka ndi thonje kapena ubweya, yachikopa kapena yopangidwa ndi chikopa,
49 If the spot is green or red on the material, whether it's leather, woven, or knitted or some other leather item, then it is infected with mold and must be shown to the priest.
ndipo ngati pamalo pamene pachita nguwiyo pali ndi maonekedwe obiriwira kapena ofiirira imeneyo ndi nguwi yoyipitsa chovala ndipo chovalacho chikaonetsedwe kwa wansembe.
50 The priest must inspect the mold and place the item in isolation for seven days.
Wansembeyo ayionetsetse nguwiyo ndipo chovalacho achiyike padera kwa masiku asanu ndi awiri.
51 On the seventh day the priest shall inspect it again, and if the patch of mold has spread in the material, whether it's leather, woven, or knitted or some other leather item, then it is a harmful mold; the article is unclean, whatever it is being used for.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri ayionetsetsenso nguwiyo ndipo ngati nguwiyo yafalikira pa chovalacho, chathonje kapena chaubweya, kapena pa chikopacho, kaya ndi cha ntchito ya mtundu wanji, imeneyo ndi nguwi yoopsa ndipo chovalacho ndi chodetsedwa.
52 The priest is to burn it, whether the affected item is wool or linen or leather. Because the mold is harmful, the article must be burned.
Wansembe atenthe chovala chathonje kapena chaubweya chija, ngakhalenso chinthu chachikopa chija popeza nguwiyo yachidetsa. Nguwiyo ndi yoopsa choncho chinthucho achitenthe.
53 However, if when the priest inspects it again it, the patch mold has not spread,
“Koma ngati wansembe akayangʼanitsitsa nguwiyo apeza kuti sinafalikire pa chovalacho kapena pa chinthu chilichonse chachikopa,
54 the priest shall order that the affected item is washed and placed in isolation for another seven days.
iye alamulire kuti chinthu choyipitsidwacho achichape. Akatero achiyike padera kwa masiku enanso asanu ndi awiri.
55 Once it has been washed, the priest is to inspect again it, and if the item with the mold hasn't changed how it looks, it is unclean. Though the mold hasn't spread, you must burn the item, whether the mold damage is on the inside or the outside.
Chovalacho chitachapidwa, wansembe achionenso ndipo ngati nguwiyo sinasinthe maonekedwe ake, ngakhale kuti sinafalikire, chovalacho ndi chodetsedwa ndithu. Muchitenthe, ngakhale kuti nguwiyo ili kumbuyo kapena kumaso kwa chinthucho.
56 If the priest inspects it and the patch of mold has faded after it has been washed, he is to cut out the affected part the material, whether it's leather, woven, or knitted.
Koma ngati wansembe aonetsetsa nʼkupeza kuti nguwi ija yathimbirira pa chovala chija kapena pa chinthu chachikopa chija atachichapa, ndiye angʼambeko chinthucho pa banga la nguwiyo.
57 However, if the mold comes back then it is spreading. In that case you must burn the affected item.
Koma ngati nguwiyo iwonekanso pa chovala chathonje kapena chaubweya ndiye kuti nguwiyo ikufalikira. Chilichonse chimene chili ndi nguwi chiyenera kutenthedwa.
58 If the mold disappears after washing, then have it washed again, and it will be clean.
Chovala chathonje kapena chaubweya, ngakhale chinthu china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, mukachichapa nguwi yake nʼkuchoka muchichapenso kawiri ndipo chidzakhala choyeretsedwa.”
59 These are the regulations regarding what needs to be done when mold contaminates wool or linen material, whether woven or knitted, or any leather item, as to declaring it clean or unclean.”
Amenewa ndiwo malamulo a nguwi yokhala pa chovala chaubweya kapena pa chovala chathonje, kapenanso pa chinthu chilichonse chopangidwa ndi chikopa kuti muzitha kulekanitsa choyeretsedwa ndi chodetsedwa.

< Leviticus 13 >