< Job 8 >

1 Then Bildad the Shuhite spoke up and said,
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 “How much longer will you go on talking like this? The words coming out of your mouth are a lot of hot air!
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Does God pervert justice? Does the Almighty pervert what is right?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Your children must have sinned against him, and so they deserved the punishment he inflicted on them.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 But if you pray to God and ask for his help,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 if you live a clean life and do what is right, then he would act to make things right for you in your home.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Though you began with next to nothing, you will end up with so much!
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Why don't you ask what previous generations discovered, examine what our ancestors found out? We were born yesterday and don't know anything!
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Our days on earth fade as quickly as a passing shadow.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Won't they teach you and explain what they know?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Can papyrus grow where there is no marsh? Can reeds grow without water?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Even without being cut, while they are still flowering, they wither faster than grass.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 This is what happens to everyone who forgets God. The hopes of those who live without God come to nothing.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Their confidence is like holding on to a flimsy spider's web.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 They look to their home to provide security, but it provides no support. They try to hang onto it, but it doesn't last.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Those who live without God are like a luxuriant plant growing in the sun, spreading its shoots all over the garden.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 It twists its roots down through the stones, and holds on to rock.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 But when it's cut down, the place where it was disowns it, saying, ‘I never even saw you.’
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Its life is over, and others spring up from the earth to take its place.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Look, God doesn't reject someone who is innocent, and he doesn't support those who are guilty.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 He can make you laugh with happiness again and shout for joy.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Those who hate you will be put to shame, and the place where the wicked live will be destroyed.”
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >