< Job 3 >

1 After this Job began speaking, cursing the day of his birth.
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 He said,
Ndipo Yobu anati:
3 “Wipe out the day I was born, and the night when it was announced that a boy had been conceived.
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 Turn that day to darkness. God above should not remember it. Don't let light shine on it.
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 Take it back, darkness and death-shadow. A black cloud should overshadow it. It should be as terrifying as the darkness of an eclipse during the day.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 Blot out that night as if it never existed. Don't count it on the calendar. Don't let it have a day in any month.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 Let that night be childless, with no sounds of happiness heard.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 Those who place curses on certain days should curse it, those who have the power to raise Leviathan.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Its early morning stars should stay dark. Looking for light, may none come, may it not see the glimmer of dawn
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 for it did not shut my mother's womb to prevent me from seeing trouble.
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 Why wasn't I stillborn? Why didn't I die at birth?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Why was there a lap for me to lie on, or breasts for me to suck?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 For now I would be lying down in peace. I would be sleeping and at rest,
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 along with the kings of this world and their officials whose palaces now lie in ruins,
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 or with noblemen who collected gold and filled their houses with silver.
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Why wasn't I a miscarriage, buried in secret, a baby who never saw the light?
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 There in the grave the wicked give no more trouble, and those whose strength is gone have their rest.
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 There prisoners take it easy—they don't hear the commands of their oppressors.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 Both small and great are there, and slaves are freed from their masters.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 Why does God give life to those who are suffering, living bitterly miserable lives,
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 those who are waiting for death that does not come and who are looking for death more desperately than hunting for treasure?
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 They're so incredibly happy when the reach the grave!
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 Why is light given to someone who doesn't know where they're going, someone God has fenced in?
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 My groans are the bread I eat; my raging tears are the water I drink.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 For all that I feared has happened to me; everything that I dreaded has come upon me.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 I have no peace, no quiet, no rest. All that comes is rage.”
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

< Job 3 >