< Isaiah 12 >

1 At that time you will say, “I will praise you, Lord! Though you were angry with me, your anger is over, and now you comfort me.
Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
2 Look! God is my salvation! I will trust in him and I won't be afraid! For the Lord is my strength and song, and he has saved me!”
Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
3 With great happiness you will take water from the well of salvation.
Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4 At that time you will say: “Praise the Lord, shout out his name! Tell the nations what he has done—let them know of his wonderful character!
Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5 Sing to the Lord for all the glorious things he's done—let the whole world know!
Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6 Shout loudly and sing for joy, you people of Zion, for the Holy One of Israel is great, and is among you.”
Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

< Isaiah 12 >