< Hosea 13 >

1 When Ephraim spoke, they were feared, for they were the leading tribe in Israel. But when they were guilty of Baal worship, they died.
Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
2 Now they constantly sin, making for themselves idols from molten metal. All of these idols are skillfully made from silver by their craftsmen. “Offer sacrifices to these idols,” say the people. “Kiss the bull calf idols.”
Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
3 Consequently they will be like the morning mist, like early morning dew, like chaff blowing away from the threshing floor, like smoke from a chimney.
Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
4 Yet I am the Lord your God who brought you out of the land of Egypt. You shall know no other gods but me. None can save you except me.
Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
5 I looked after you in the wilderness; in that dry desert land it was like pasture to them
Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
6 and they were satisfied. But when they were satisfied they became arrogant, and they forgot me.
Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
7 So I will be like a lion to them, like a leopard I will lie in wait beside the path.
Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
8 I will be like a mother bear whose cubs have been taken, I will rip out their hearts. I shall devour them like a lion, like a wild beast I will tear them apart.
Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
9 You have destroyed yourselves, Israel, for your only help is in me.
“Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 Where then is your king? Let him save you in all your cities! Where are your leaders who demanded a king and princes from me?
Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11 In my anger I give you a king, and in my fury I take one.
Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12 Ephraim's guilt is packed up; their sin will be eradicated.
Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 The pain of childbirth has come to them, trying to give birth to a son who is not “wise” because he is not in the right position when the time comes.
Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
14 I shall redeem them from the power of Sheol; I shall deliver them from death. Where, death, are your plagues? Where, Sheol, is your destruction? Compassion is hidden from my sight. (Sheol h7585)
“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol h7585)
15 Even though they flourish among the reeds, an east wind will come, a wind from the Lord that rises in the desert will dry up their springs and their wells will fail. It will rob from their treasury everything of value.
ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 Samaria will have to bear the consequences of their guilt, because they rebelled against her God. They will be slaughtered by the sword; their children will be dashed to the ground; their pregnant women will be ripped open.
Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”

< Hosea 13 >