< Exodus 11 >

1 The Lord told Moses, “There's one last plague I will bring down on Pharaoh and on Egypt. After that he will let you go, but when he does, he'll expel every one of you from the country.
Tsopano Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzalanga Farao pamodzi ndi Aigupto onse ndi mliri umodzi wotsiriza. Zikadzachitika izi iye adzakulolani kuti mutuluke mʼdziko lino. Ndithu pamene azidzakutulutsani adzachita ngati akukuyingitsani.
2 Now go and tell the Israelites, both men and women, to ask their Egyptian neighbors for silver and gold objects.”
Awuze anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa mnansi wake ziwiya zasiliva ndi golide.”
3 The Lord made the Egyptians look favorably on the Israelites. In fact, Moses himself was highly respected in Egypt by both Pharaoh's officials and the ordinary people.
Tsono Yehova anachititsa Aigupto kuti akomere mtima Aisraeli. Komanso Mose anali wotchuka kwambiri mʼdziko la Igupto, pamaso pa nduna za Farao ndi anthu onse.
4 Moses said, “This is what the Lord says: ‘Around midnight I will go through the whole of Egypt.
Tsono Mose anawuza Farao kuti, “Pakati pa usiku, Yehova adzayenda pakati pa anthu a ku Igupto.
5 Every firstborn son in the land of Egypt will die, from the firstborn of Pharaoh sitting on his throne to the firstborn of the servant girl working with a handmill, as well as all the firstborn of the cattle.
Ndipo mwana aliyense wamwamuna wachisamba adzafa, kuyambira mwana wamwamuna wa Farao amene amakhala pa mpando waufumu, mpaka mwana wamwamuna wachisamba wa mdzakazi wake amene ali naye pa mtondo, komanso ana oyamba a ziweto.
6 There will be loud cries of mourning all over Egypt, such as have never been before, and will never be again.
Kudzakhala kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, kumene sikunachitikepo ndipo sikudzachitikanso.
7 But among all the Israelites there won't even be the sound of a dog barking at them or their animals. That way you will know that the Lord distinguishes between Egypt and Israel.’
Koma pakati pa Aisraeli, ngakhale galu sadzawuwa munthu aliyense kapena chiweto!” Kotero mudzadziwa kuti Yehova ndiye wasiyanitsa pakati pa Igupto ndi Israeli.
8 All your officials will come to me, bowing down before me and saying, ‘Leave, and take everyone who follows you with you!’ After that I will leave.” Moses was very angry, and left Pharaoh.
Nduna zanu zonse zidzabwera kwa ine, kugwada pamaso panga ndi kunena kuti, “Pita iwe ndi anthu ako onse amene akukutsatirawa! Zimenezi zikadzachitika ine ndidzachoka.” Ndipo Mose anachoka kwa Farao atakwiya kwambiri.
9 The Lord said to Moses, “Pharaoh is refusing to listen to you so I can do even more miracles in Egypt.”
Yehova ananena kwa Mose kuti, “Farao adzakana kukumvera, kuti zodabwitsa zanga zichuluke mʼdziko la Igupto.”
10 Moses and Aaron did these miracles before Pharaoh, but the Lord gave Pharaoh a stubborn attitude, and he wouldn't let the Israelites leave his country.
Mose ndi Aaroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli atuluke mʼdziko lake.

< Exodus 11 >