< Daniel 11 >

1 And I myself, in the first year of Darius the Mede, took my stand to support and defend him.
Ndipo chaka choyamba cha Dariyo Mmedi ine Mikayeli ndinabwera kumuthandiza ndi kumuteteza Gabrieli.
2 So now let me reveal the truth to you. There are still three kings to come to power in Persia, and then a fourth who will be far richer than all the others. When he becomes strong through his wealth, he will rally the whole kingdom against Greece.
“Ndipo tsopano ndikuwuza zoona: Mafumu ena atatu adzalamulira ku Peresiya, ndipo kenaka padzadzuka mfumu yachinayi imene idzakhala yolemera kwambiri kuposa onsewo. Popeza kuti idzakhala ndi mphamvu chifukwa cha chuma chake, idzadzutsa onse kuti alimbane ndi ufumu wa Grisi.
3 Then a mighty king will come to power. He will rule with great authority and do whatever he wants.
Kenaka mfumu yamphamvu idzafika imene idzalamulira ndi ufumu waukulu ndi kuchita zimene ifuna.
4 But as he extends his power his kingdom will be broken up, divided towards the four winds of heaven. It will not go to his descendants, and it will not be ruled as he ruled. It will be pulled up and given to others.
Koma ufumu wake ukadzafika pachimake, udzawonongedwa ndi kugawidwa mʼzigawo zinayi. Ufumuwo sudzaperekedwa kwa zidzukulu zake, ndipo olowa mʼmalo mwake sadzakhala ndi mphamvu monga anali nazo, chifukwa ufumu wake udzazulidwa ndi kuperekedwa kwa ena.
5 The king of the south will grow strong, but one of his officers will grow even stronger and will rule his kingdom with great authority.
“Mfumu ya kummwera idzakhala yamphamvu, koma mmodzi mwa akalonga ake adzakhala ndi mphamvu kuposa iyo; adzalamulira ufumu wake waukulu kwambiri.
6 Some years later they will form an alliance, and the daughter of the king of the south will be married to the king of the north to guarantee the peace treaty. However, she will not be able to keep her hold on power, nor will his power continue. She and her attendants will be betrayed, along with her child and husband. Later on, however,
Patapita zaka zingapo, mfumu ya kummwera ndi mfumu ya kumpoto adzachita pangano. Mwana wamkazi wa mfumu ya kummwera adzapita nakakwatiwa ndi mfumu ya kumpoto pokhazikitsa pangano la mtendere, koma ulamuliro wake pamodzi ndi wa mwana wake sudzakhalitsa. Mʼmasiku amenewo iye, mwamuna wake, mwana wake ndi atumiki ake, onse adzaperekedwa kwa adani.
7 a new king of the south from her family will take over. He will come to attack the army of the king of the north and enter his fortress. He will fight against them and will win.
“Mmodzi wochokera ku banja la mkaziyo adzadzuka nadzalamulira mʼmalo mwake. Iye adzamenyana ndi ankhondo a mfumu ya kumpoto ndi kulowa mʼmalo ake otetezedwa; adzachita nawo nkhondo ndi kupambana.
8 In addition he will take back with him to Egypt the idols of their gods, along with their expensive vessels of silver and gold. For some years he will leave the king of the north alone.
Iye adzalandanso milungu yawo, mafano awo achitsulo, ndi ziwiya zawo zamtengowapatali zasiliva ndi golide ndi kubwerera nazo ku Igupto. Adzaleka osayithira nkhondo mfumu ya kumpoto kwa zaka zingapo.
9 Then the king of the north will march into the kingdom of the king of the south but will have to retreat to his own land.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzathira nkhondo dziko la mfumu ya kummwera koma idzalephera ndi kubwerera kwawo.
10 However, his sons will prepare for war, assembling a huge number of troops. One of them will lead an advance that rushes forward like a river bursting its banks, crossing over and pressing forward to attack the enemy fortress.
Ana ake adzakonzekera nkhondo ndi kusonkhanitsa gulu lankhondo lalikulu, limene lidzathira nkhondo mfumu yakummwera ngati chigumula mpaka kumalo ake otetezedwa.
11 This will infuriate the king of the south, who will go out into battle against the large army assembled by the king of the north and will defeat it.
“Kenaka mfumu yakummwera idzatuluka mokwiya ndi kumenya nkhondo ndi mfumu yakumpoto, imene idzasonkhanitsa gulu lalikulu la nkhondo, koma idzayigonjetsa.
12 After capturing such a large army, he will become very proud, and will kill thousands. But this triumph will not last long.
Gulu la nkhondoli likadzagwidwa, mfumu yakummwera idzayamba kudzikuza ndipo idzapha anthu miyandamiyanda, koma kupambanaku sikudzapitirira.
13 Years later the king of the north will once again raise an army, even larger than before, and will invade with this huge army, accompanied by plenty of supplies.
Popeza mfumu ya kumpoto idzasonkhanitsa gulu lina lankhondo, lochulukirapo kuposa loyamba; ndipo patapita zaka zingapo idzabwera ndi chigulu chachikulu cha nkhondo chokonzekeratu ndi zida.
14 At the same time many will rebel against the king of the south. Violent men from your own people will rebel in order to fulfill this vision, but they shall fail.
“Nthawi imeneyo ambiri adzawukira mfumu ya kummwera. Anthu achisokonezo pakati panu nawonso adzawukira pokwaniritsa masomphenya, koma sadzapambana.
15 Then the king of the north will come and build siege ramps and he will capture a city with strong defenses. The forces of the south will not be able to prevent it—even his best troops won't be able to resist the attack.
Kenaka mfumu ya kumpoto idzafika ndikuzinga mzinda powunda nthumbira za nkhondo ndipo idzagonjetsa mzinda wotetezedwa. Gulu lankhondo la kummwera lidzasowa mphamvu; ngakhale akatswiri awo ankhondo sadzakhala ndi mphamvu zogonjetsera ankhondo a kumpoto.
16 The invader will do whatever he wants; no one will be able to oppose him. He will stand in the Beautiful Land with the power to destroy it.
Mfumu ya kumpoto idzachita zofuna zake; palibe aliyense adzayigonjetse. Idzakhazikitsa ulamuliro wake mu Dziko Lokongola. Zonse zidzakhala mu ulamuliro wa mfumu yakumpoto ija.
17 He will be determined to come with all the power of his kingdom and will make a peace treaty with the king of the south. To secure this he will give him a daughter of women to marry in order to destroy the kingdom. But she will not be successful and will not support him.
Idzafika ndi mphamvu za ufumu wake wonse ndipo idzayesa kuchita pangano la mtendere ndi mfumu ya kummwera. Ndipo idzamupatsa mwana wake wamkazi kuti amukwatire ndi cholinga cholanda ufumu, koma zolinga zake sizidzatheka kapena kumuthandiza.
18 Then he will turn to attack the coastlands and will conquer many, but a commander will put a stop to his arrogant behavior, paying him back for it.
Kenaka idzatembenukira ku mayiko a mʼmbali mwa nyanja ndi kulanda mizinda yambiri, koma mtsogoleri wina wa nkhondo adzathetsa kudzikuza kwakeko ndipo adzabwezera chipongwecho kwa iye.
19 He will return to the fortresses of his own land, but he will stumble and fall, and will be gone.
Zikadzatha izi, mfumu idzabwerera ku malo otetezedwa a dziko la kwawo koma idzapunthwa ndi kugwa osapezekanso.
20 His successor will send out a tax collector to maintain royal wealth. However, in a short time he will die, but not violently or in battle.
“Mfumu imene idzatenga malo ake idzatumiza wokhometsa msonkho kuti chuma cha ufumu wake chichuluke. Komabe mʼzaka zochepa mfumuyo idzawonongedwa osati mu mkwiyo kapena ku nkhondo.
21 A contemptible person will follow him who will not be given royal majesty. He will take over peacably and assume control of the kingdom through deception.
“Mʼmalo mwake mudzalowa munthu wonyozeka amene si wa banja laufumu. Iye adzabwera pamene anthu akuganiza kuti ali pa mtendere, ndipo adzalanda ufumuwo mwa chinyengo.
22 Great armies will be swept away before him. They will be broken, as well as the prince of the agreement.
Kenaka adzagonetsa gulu lalikulu lankhondo kuphatikizapo Mkulu wa Ansembe wapangano.
23 After making an alliance with him, he will act deceptively. He will come to power peacably, becoming strong though only having a few supporters.
Atatha kuchita naye pangano, iye adzachita monyenga, ndipo ngakhale adzakhale ndi anthu ochepa adzakhalabe ndi mphamvu.
24 He will invade the richest parts of the land and do what his fathers and forefathers never did—he will distribute plunder, spoil, and possessions. He will make plans to attack fortresses, but only for a time.
Mwadzidzidzi, iye adzazithira nkhondo zigawo zolemera kwambiri ndipo adzachita zimene makolo ake ngakhale agogo ake sanachitepo. Iye adzagawira zolanda, zofunkha ndi chuma kwa omutsatira. Adzachita chiwembu cholanda mizinda yotetezedwa koma kwa kanthawi kochepa.
25 Then he will draw on his strength and courage to gather a large army against the king of the south. The king of the south will prepare for war. Fighting back with a large and powerful army, but he will not be successful because of plots made against him.
“Mfumu ya kumpoto idzalimba mtima, ndipo idzasonkhanitsa gulu lalikulu la ankhondo kuti lithire nkhondo mfumu yakummwera. Mfumu yakummwera ndi gulu lake lankhondo lalikulu ndi lamphamvu idzathirana nkhondo ndi mfumu yakumpoto koma sidzapambana chifukwa cha ziwembu zimene adzamukonzera.
26 Those closest to him will destroy him. His army will be wiped out—many will fall in battle.
Amene amadya chakudya ndi mfumu adzamuukira; gulu lake lankhondo lidzagonjetsedwa, ndipo ambiri adzafera ku nkhondo.
27 The two kings, with evil intentions, will tell each other lies even as they sit together at the same table. But their scheming is pointless—the end will come at the time predicted.
Mafumu awiriwa mitima yawo idzalinga ku zoyipa. Azidzanamizana ali pa tebulo limodzi, koma zolinga zawo sizidzatheka chifukwa nthawi idzakhala isanakwane.
28 The king of the north will return to his own country with all the wealth he has looted. He will be determined to attack the people of the holy agreement, and do all he can to destroy it before returning to his own country.
Mfumu ya kumpoto idzabwerera ku dziko la kwawo ndi chuma chambiri, koma mtima wake udzafunitsitsa pangano lopatulika. Idzawononga panganolo ndipo kenaka idzabwerera ku dziko lake.
29 At the time predicted he will return to invade the south again, but this time it won't be like before.
“Patapita nthawi mfumu ya kumpoto idzabwereranso kummwera koma sidzapambana monga inachitira kale.
30 Ships from Cyprus will come to attack him, frightening him off so that he retreats. But this will make him mad, and he will attack the people of the holy agreement, recognizing those who abandon their commitment to the holy agreement.
Sitima zapamadzi zochokera ku mayiko a ku madzulo zidzalimbana naye, ndipo adzataya mtima. Kenaka idzabwerera mopsa mtima ndi kudzalimbana ndi chipembedzo cha anthu opatulika. Idzabwerera ndi kuchitira chifundo amene sadzasunga pangano loyera.
31 His forces will occupy and defile the Temple fortress. They will put a stop to the continual service, and set up a form of idolatry that causes devastation.
“Ankhondo ake adzayipitsa linga la Nyumba ya Mulungu ndipo adzathetsa nsembe za tsiku ndi tsiku. Kenaka adzakhazikitsa chonyansa chimene chabweretsa chiwonongeko.
32 The king will use flattery to corrupt those who break the solemn agreement, but the people who know their God will stand firm in their resistance.
Ndi mawu oshashalika mfumuyo idzakopa amene anaphwanya pangano, koma anthu amene amadziwa Mulungu wawo adzalimbika ndipo adzayikana mfumuyo kwathunthu.
33 Wise leaders of the people will teach many, though for a time they will be killed by sword and fire, or they will be imprisoned and robbed.
“Amene ndi anzeru adzalangiza ambiri. Koma patapita kanthawi adzaphedwa ndi lupanga kapena kutenthedwa, kapena kugwidwa kapena kulandidwa katundu.
34 During this time of persecution they will receive a little help, and many who join them won't be sincere.
Pa nthawi yozunzikayi ena adzawathandiza pangʼono, koma ambiri othandizawo adzakhala achinyengo.
35 Some of the wise will be killed, so that they may be refined and purified and cleansed until the time of the end, for the predicted time is still to come.
Ena mwa anzeruwo adzaphedwa ndi cholinga chakuti ayengedwe, otsala mwa iwo ayeretsedwe ndi kukhala wopanda banga kufikira nthawi yomaliza, popeza idzafika ndithu nthawi imene Mulungu wayika.
36 The king will do whatever he wants, praising himself and considering himself greater than any god, even saying outrageous things against the God of gods. He will be successful until the time of anger has finished, for what has been decided will be accomplished.
“Mfumu ya kumpoto idzachita zimene ikufuna. Idzadzikweza ndi kudziyesa yopambana mulungu aliyense ndipo idzanenera za mwano Mulungu wa milungu. Iyo idzapambana mpaka nthawi yoti Mulungu ayilange mwa mkwiyo itakwana popeza chimene chatsimikizika chiyenera kuchitika.
37 He will have no time for the gods of his forefathers, nor for the one loved by women, nor for any other god, for he considers himself greater than any of these.
Mfumuyo idzanyoza milungu ya makolo ake ndiponso mulungu wokondedwa ndi akazi, sidzachitiranso ulemu mulungu aliyense, koma idzadzikweza yokha pamwamba pa onse.
38 Instead he will honor the god of fortresses—a god unknown to his forefathers—giving him offerings of gold and silver and precious stones and expensive gifts.
Mʼmalo mwa onsewo, idzachitira ulemu mulungu wachitetezo; mulungu wosadziwika ndi makolo ake. Iyo idzapereka kwa mulunguyo golide ndi siliva, ndi miyala yokongola, ndiponso mphatso za pamwamba kwambiri.
39 He will deal with strong fortresses with the help of this foreign god. He will give riches to those who acknowledge him, making them rulers over the people, and distributing the land at a price.
Anthu opembedza mulungu wachilendo adzakhala ngati linga lake. Idzalemekeza iwowa kwambiri, ndipo idzawayika kuti alamulire anthu ambiri. Idzawagawira dziko ngati malipiro awo.
40 At the time of the end the king of the south will attack him. But the king of the north will retaliate with force like a storm, with chariots and horsemen and many ships. He will advance, sweeping through many lands.
“Pa nthawi yomaliza mfumu yakummwera idzachita nkhondo ndi mfumu yakumpoto. Koma mfumu yakumpotoyi idzayikantha ndi magaleta ndi akavalo ndi sitima zapamadzi zambiri ngati mphepo yamkokomo. Idzalowa mʼmayiko ambiri ndikuwakokolola onse ngati madzi osefukira.
41 He will invade the Beautiful Land and kill many people there. However, Moab, Edom, and most of the Ammonites will escape his power.
Idzalowanso mʼDziko Lokongola ndipo anthu ambiri adzaphedwa. Koma Edomu, Mowabu ndi olamulira a Amoni adzapulumuka.
42 He will extend his attacks against different countries—even the land of Egypt will not be able to escape.
Idzathira nkhondo mayiko ambiri ndipo ngakhale Igupto sadzapulumuka.
43 He will acquire the gold and silver and riches of Egypt, ruling over them and also the Libyans and Ethiopians.
Idzalanda chuma cha golide, siliva, ndi zonse za mtengowapatali za ku Igupto, ndiponso anthu a ku Libiya ndi Akusi adzagonja kwa iwo.
44 But news from the east and the north will alarm him, and in a furious rage he will set out to destroy and exterminate many people.
Koma uthenga wochokera kummawa ndi kumpoto udzayiopsa, ndipo idzapita ndi ukali kukawononga ndi kutheratu anthu ambiri.
45 He will set up his royal camp between the sea and the beautiful holy mountain. But he will die with no one to help him.
Mfumuyo idzayimika matenti ake aufumu, pakati pa nyanja ndi phiri lokongola. Komabe mapeto ake mfumuyo idzaphedwa, ndipo palibe amene adzayithandize.”

< Daniel 11 >