< 1 Samuel 18 >

1 After David finished speaking with Saul, Jonathan became great friends with David. He loved David as he loved himself.
Davide atatha kuyankhula ndi Sauli, mtima wa Yonatani unagwirizana ndi mtima wa Davide, ndipo iye ankamukonda Davide monga momwe ankadzikondera yekha.
2 From that time on Jonathan had David work for him and would not let him go back home.
Choncho Sauli anamusunga Davideyo kuyambira tsiku limenelo ndipo sanamulole kuti abwerere ku nyumba ya abambo ake.
3 Jonathan made a solemn agreement with David because he loved him as he loved himself.
Ndipo Yonatani anapanga pangano ndi Davide chifukwa ankamukonda monga momwe ankadzikondera.
4 Jonathan took off the robe he was wearing and gave it to David, together with his tunic, his sword, his bow, and his belt.
Yonatani anavula mkanjo umene anavala ndipo anamupatsa Davide pamodzi ndi zovala za nkhondo, lupanga, uta ndi lamba.
5 David was successful in doing everything Saul asked him to do, so Saul made him an officer in the army. This pleased everyone, including Saul's other officers.
Davide ankapita kulikonse kumene Sauli ankamutuma kuti apite kukamenya nkhondo, ndipo ankapambana. Choncho Sauli anamupatsa udindo woyangʼanira gulu lankhondo. Ichi chinakondweretsa anthu onse ngakhalenso atsogoleri a nkhondo a Sauli.
6 When the soldiers returned home after David had killed the Philistine, the women of all the towns of Israel came out singing and dancing to meet King Saul, happily celebrating with tambourines and musical instruments.
Anthu akubwerera kwawo Davide atapha Mfilisiti uja, amayi anatuluka mʼmizinda yonse ya Israeli, akuyimba ndi kuvina kukachingamira mfumu Sauli. Ankayimba ndi kuvina mokondwa, kwinaku ngʼoma ndi zitoliro zikulira.
7 As they danced the women sang, “Saul has killed his thousands, and David his tens of thousands.”
Amayiwo ankalandizana nyimbo mokondwera namati: “Sauli wapha 1,000, Koma Davide wapha miyandamiyanda.”
8 What they were singing made Saul very angry as he didn't think it was right. He said to himself, “They've given David credit for killing tens of thousands, but only thousands to me. All that's left is to give him the kingdom!”
Koma Sauli anapsa mtima kwambiri ndipo mawu amenewa anamuyipira. Iye anati, “Iwo amuwerengera Davide miyandamiyanda, koma ine 1,000 okha. Nanga chatsalanso nʼchiyani kuti atenge? Si ufumu basi?”
9 From that time on Saul viewed David with suspicion.
Ndipo kuyambira tsiku limeneli Sauli ankamuchitira nsanje Davide.
10 The following day an evil spirit from God came on Saul with power, and he was ranting inside the house while David played the harp as he regularly did. Saul happened to be holding a spear,
Mmawa mwake mzimu woyipa uja unabwera mwamphamvu pa Sauli. Sauli anayamba kubwebweta mʼnyumba mwake. Davide ankamuyimbira zeze monga nthawi zonse. Sauli anali ndi mkondo mʼdzanja lake.
11 and he threw it at David, saying to himself, “I'll pin David to the wall.” But David managed to escape him twice.
Tsono anawuponya mkondowo, namati mu mtima mwake, “Ndimubaya Davide ndi kumukhomera ku khoma.” Koma Davide anawulewa kawiri konse.
12 Saul was afraid of David, because the Lord was with David, but he had given up on Saul.
Pambuyo pake Sauli amamuopa Davide chifukwa Yehova anali ndi Davideyo, nʼkumusiya Sauli.
13 So Saul sent David away and made him a commander of a thousand soldiers, leading them out and back as part of the army.
Kotero Sauli anamuchotsa Davide pamaso pake ndi kumuyika kukhala mtsogoleri wa ankhondo 1,000. Choncho Davide ankapita ndi kubwera akutsogolera ankhondowa.
14 David was very successful in everything he did, because the Lord was with him.
Davide ankapambana kwambiri pa chilichonse chimene amachita chifukwa Yehova anali naye.
15 When Saul saw how successful David was, he was even more afraid of him.
Sauli ataona momwe Davide ankapambanira, iye anamuopa kwambiri.
16 But everyone in Israel and Judah loved David, because of his leadership in the army.
Koma Aisraeli onse ndi anthu a Yuda ankamukonda Davide chifukwa ankawatsogolera pa nkhondo zawo.
17 One day Saul told David, “Here's my oldest daughter Merab. I will give her to you in marriage, but only if you prove to me you're a brave warrior and fight the battles of the Lord.” For Saul was thinking, “I don't need to be the one to kill him—let the Philistines do it!”
Tsiku lina Sauli anawuza Davide kuti, “Nayu Merabi mwana wanga wamkazi wamkulu. Ine ndakupatsa kuti umukwatire. Koma unditumikire molimba mtima pomenya nkhondo za Yehova.” Poteropo Sauli ankanena kuti, “Ndisamuphe ndi manja angawa koma aphedwe ndi Afilisti!”
18 “But who am I, and what status does my family have in Israel, for me to become the son-in-law of the king?” David replied.
Ndipo Davide anati kwa Sauli, “Ine ndine yani, ndipo abale anga kapena banja la abambo anga ndife yani mʼdziko la Israeli kuti ndikhale mpongozi wa mfumu?”
19 However, when the time came to give Merab, Saul's daughter, to David, she was given in marriage to Adriel of Meholah instead.
Koma pa nthawi yoti Merabi mwana wa Sauli akwatiwe ndi Davide, Sauli anamupereka kwa Adrieli wa ku Mehola kuti amukwatire.
20 Meanwhile Saul's daughter Michal had fallen in love with David, and when Saul was told, he was happy about it.
Koma Mikala mwana wamkazi wa Sauli anamukonda Davide ndipo Sauli atamva za zimenezi, anakondwera.
21 “I'll give her to David,” Saul thought. “She can be the bait so the Philistines can trap him.” So Saul said to David, “This is the second time you can become my son-in-law.”
Sauli ankaganiza kuti, “Ndimupatse amukwatire kuti akhale ngati msampha kwa Davideyo, ndipo adzaphedwe ndi Afilisti.” Choncho Sauli anawuza Davide kachiwiri, “Tsopano udzakhala mkamwini wanga.”
22 Saul gave these instructions to his servants, “Talk with David in private and tell him, ‘Look, the king is very happy with you, and all of us love you. Why not become the king's son-in-law?’”
Sauli analamulanso nduna zake kuti, “Muyankhuleni Davide mwamseri ndi kumuwuza kuti, ‘Taona, mfumu imakondwera nawe, ndipo nduna zake zonse zimakukonda. Tsono ukhale mkamwini wa mfumu.’”
23 Saul's servants spoke privately to David, but he replied, “Do you think it's nothing to become the king's son-in-law? I'm a poor man, and I'm not important.”
Iwo anakamuwuza Davide mawu amenewa, koma Davide anati, “Kodi inu mukuganiza kuti ndi chinthu chapafupi kukhala mpongozi wa mfumu? Ine ndine wosauka ndiponso wosatchuka.”
24 When Saul's servants explained to him what David had said,
Nduna za Sauli zinamuwuza zonse zimene anayankha Davide.
25 Saul told them, “Tell David, ‘The only dowry the king wants for the bride is one hundred foreskins of dead Philistine as a way of taking revenge on his enemies.’” Saul's plan was to have David be killed by the Philistines.
Sauli anayankha kuti, “Kamuwuzeni Davide kuti, ‘Mfumu sikufuna malowolo a mtundu wina uliwonse koma timakungu ta msonga za mavalo a Afilisti 100 kuti ilipsire adani ake.’” Maganizo a Sauli anali akuti Davide aphedwe ndi Afilisti.
26 When the servants reported what the king had said back to David, he was happy to become the king's son-in-law. While there was still time,
Nduna za Saulizo zitamuwuza Davide zimenezi, anakondwera kuti akhale mpongozi wa mfumu. Koma nthawi imene anapatsidwa isanathe,
27 David set off with his men and killed two hundred Philistines, and brought back their foreskins. They counted them all out before the king so that David could become the king's son-in-law. So Saul gave him his daughter Michal in marriage.
Davide ndi anyamata ake anapita ndi kukapha Afilisti 200. Iye anabwera ndi timakungu tija natipereka tonse kwa mfumu kuti akhale mpongozi wa mfumu. Kotero Sauli anapereka mwana wake wamkazi, Mikala, kwa Davide kuti amukwatire.
28 Saul realized that the Lord was with David and that his daughter Michal was in love with David,
Sauli atazindikira kuti Yehova anali ndi Davide ndiponso kuti mwana wake Mikala amamukonda Davide,
29 and so he became even more afraid of David, and was David's enemy for the rest of his life.
iye anapitirirabe kumuopa Davide ndi kumadana naye moyo wake wonse.
30 Whenever the Philistine commanders attacked, David was more successful in battle than all of Saul's officers, so that his reputation grew rapidly.
Nthawi zonse pamene atsogoleri a Afilisti ankatuluka kukamenya nkhondo, Davide ankapambana kuposa nduna zonse za Sauli. Choncho dzina lake linatchuka kwambiri.

< 1 Samuel 18 >