< 1 Chronicles 25 >

1 David and the leaders of the Levites chose men from the families of Asaph, Heman, and Jeduthun to serve by prophesying accompanied by lyres, harps, and cymbals. Here is the list of those who performed this service:
Davide ndi atsogoleri a asilikali anapatula ena mwa ana a Asafu, Hemani ndi Yedutuni ku utumiki wa uneneri pogwiritsa ntchito apangwe, azeze ndi ziwaya zamalipenga. Tsopano nawu mndandanda wa anthu amene ankagwira ntchito imeneyi:
2 From the sons of Asaph: Zaccur, Joseph, Nethaniah, and Asarelah. These sons of Asaph were under the supervision of Asaph, who prophesied under the supervision of the king.
Kuchokera kwa ana a Asafu: Zakuri, Yosefe, Netaniya ndi Asareli. Ana a Asafu amalamulidwa ndi Asafu ndipo amanenera moyangʼaniridwa ndi mfumu.
3 From the sons of Jeduthun: Gedaliah, Zeri, Jeshaiah, Shimei, Hashabiah, and Mattithiah, six in total, under the supervision of their father Jeduthun, who prophesied accompanied by the harp, giving thanks and praise to the Lord.
Kwa Yedutuni, kuchokera kwa ana ake: Gedaliya, Zeri, Yesaya, Simei, Hasabiya ndi Matitiya. Onse analipo 9 ndipo amayangʼaniridwa ndi Yedutuni abambo awo, amene amanenera pogwiritsa ntchito apangwe poyamika ndi kutamanda Yehova.
4 From the sons of Heman: Bukkiah, Mattaniah, Uzziel, Shebuel, Jerimoth, Hananiah, Hanani, Eliathah, Giddalti, Romamti-ezer, Joshbekashah, Mallothi, Hothir, and Mahazioth.
Kwa Hemani, kuchokera kwa ana ake: Bukiya, Mataniya, Uzieli, Subaeli ndi Yerimoti; Hananiya, Hanani, Eliata, Gidaliti ndi Romamiti-Ezeri; Yosibakasa, Maloti, Hotiri ndi Mahazioti.
5 All these sons of Heman, the king's seer, were given to him through the promises of God to honor him, for God gave Heman fourteen sons and three daughters.
Onsewa anali ana a Hemani mlosi wa mfumu. Iye anapatsidwa anawa potsata mawu a Mulungu akuti adzamukweza. Mulungu anapatsa Hemani ana aamuna 14 ndi ana aakazi atatu.
6 All of them were under the supervision of their fathers for the music of the house of the LORD with cymbals, harps, and lyres, for the service of the house of God. Asaph, Jeduthun, and Heman were under the supervision of the king.
Anthu onsewa ankayangʼaniridwa ndi makolo awo pa mayimbidwe a mʼNyumba ya Yehova. Iwowatu ankayimba ndi ziwaya zamalipenga, azeze ndi apangwe potumikira mʼNyumba ya Mulungu. Koma Asafu, Yedutuni ndi Hemani amayangʼaniridwa ndi mfumu.
7 Along with their relatives, all of them trained and skilled in singing to the LORD, they totaled 288.
Iwo pamodzi ndi abale awo onse ophunzitsidwa ndi aluso loyimbira Yehova chiwerengero chawo chinali 288.
8 They cast lots for whatever responsibility they had, the least important equal to the most important, the teacher to the student.
Angʼonoangʼono ndi akulu omwe, mphunzitsi ndi wophunzira yemwe anachita maere pa ntchito zawo.
9 The first lot, which was for Asaph, fell to Joseph, his sons, and his brother, 12 in total. The second fell to Gedaliah, his sons, and his brothers, 12 in total.
Maere woyamba amene anali a Asafu, anagwera Yosefe, ana ndi abale ake. 12 Maere achiwiri anagwera Gedaliya, ndi abale ake ndi ana ake. 12
10 The third fell to Zaccur, his sons, and his brothers, 12 in total.
Maere achitatu anagwera Zakuri, ana ake ndi abale ake. 12
11 The fourth fell to Izri, his sons, and his brothers, 12 in total.
Maere achinayi anagwera Iziri, ana ake ndi abale ake. 12
12 The fifth to Nethaniah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere achisanu anagwera Netaniya, ana ake ndi abale ake. 12
13 The sixth fell to Bukkiah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere achisanu ndi chimodzi anagwera Bukiya, ana ake ndi abale ake. 12
14 The seventh fell to Jesarelah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere achisanu ndi chiwiri anagwera Yesarela, ana ake ndi abale ake. 12
15 The eighth fell to Jeshaiah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere achisanu ndi chitatu anagwera Yeshaya, ana ake ndi abale ake. 12
16 The ninth fell to Mattaniah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere achisanu ndi chinayi anagwera Mataniya, ana ake ndi abale ake. 12
17 The tenth fell to Shimei, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a khumi anagwera Simei, ana ake ndi abale ake. 12
18 The eleventh fell to Azarel, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 11 anagwera Azareli, ana ake ndi abale ake. 12
19 The twelfth fell to Hashabiah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 12 anagwera Hasabiya, ana ake ndi abale ake. 12
20 The thirteenth fell to Shubael, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 13 anagwera Subaeli, ana ake ndi abale ake. 12
21 The fourteenth fell to Mattithiah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 14 anagwera Matitiya, ana ake ndi abale ake. 12
22 The fifteenth fell to Jerimoth, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 15 anagwera Yeremoti, ana ake ndi abale ake. 12
23 The sixteenth fell to Hananiah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 16 anagwera Hananiya, ana ake ndi abale ake. 12
24 The seventeenth fell to Joshbekashah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 17 anagwera Yosibakasa, ana ake ndi abale ake. 12
25 The eighteenth fell to Hanani, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 18 anagwera Hanani, ana ake ndi abale ake. 12
26 The nineteenth fell to Mallothi, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 19 anagwera Maloti, ana ake ndi abale ake. 12
27 The twentieth fell to Eliathah, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 20 anagwera Eliyata, ana ake ndi abale ake. 12
28 The twenty-first fell to Hothir, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 21 anagwera Hotiri, ana ake ndi abale ake. 12
29 The twenty-second fell to Giddalti, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 22 anagwera Gidaliti, ana ake ndi abale ake. 12
30 The twenty-third fell to Mahazioth, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 23 anagwera Mahazioti, ana ake ndi abale ake. 12
31 The twenty-fourth fell to Romamti-Ezer, his sons and his brothers, 12 in total.
Maere a 24 anagwera Romamiti-Ezeri, ana ake ndi abale ake 12.

< 1 Chronicles 25 >