< Luke 3 >

1 Now in the fifteenth year of the reign of Tiberius Caesar, Pontius Pilate being governor of Judea and Herod being tetrarch of Galilee, while his brother Philip was tetrarch of the region of Iturea and Trachonitis and Lysanias tetrarch of Abilene,
Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
2 during the high priesthood of Annas (also Caiaphas), the word of God came upon John the son of Zacharias in the wilderness.
Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
3 So he went into all the region around the Jordan, proclaiming a baptism of repentance for forgiveness of sins;
Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
4 as it is written in the book of the words of Isaiah the prophet, saying: “A voice calling out: ‘Prepare the way of the Lord in the wilderness, make His paths straight.
Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
5 Every ravine will be filled up, and every mountain and hill will be leveled; the crooked parts of the roads will be straightened out, and the rough parts will be smoothed out;
Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
6 and all flesh will see the salvation of God.’”
Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
7 Then he said to the crowds that were coming out to be baptized by him: “You sons of poisonous snakes! Who tipped you off to flee from the coming wrath?
Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
8 Well then, produce fruits befitting repentance, and don't even begin to say among yourselves, ‘We have Abraham as father,’ because I say to you that God is able to raise up children to Abraham from these stones!
Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
9 But even now the axe is being laid to the root of the trees; so then, every tree not producing good fruit is cut down and thrown into the fire.”
Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
10 So the people started asking him, “What then must we do?”
Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
11 In answer he said to them, “He who has two coats, let him share with him who has none; and he who has food should do likewise.”
Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
12 Well even tax collectors came to be baptized by him and said to him, “Teacher, what must we do?”
Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
13 So He said to them, “Don't charge more than what was determined to you.”
Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
14 So the soldiers started asking him too: “What about us? What must we do?” He said to them, “Don't extort or harass anyone, and be content with your wages.”
Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
15 Now as the people were expectant and all were reasoning in their hearts concerning John, whether he just might be the Messiah,
Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
16 John anticipated them all saying: “I indeed am baptizing you with water, but One mightier than I is coming, whose sandal straps I am not worthy to untie. He will baptize you with Holy Spirit and fire;
Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
17 whose winnowing shovel is in His hand, and He will thoroughly clean out His threshing floor and gather the wheat into His barn, but He will burn up the chaff with unquenchable fire.”
Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
18 (Indeed, with many other exhortations as well he kept on preaching to the people;
Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
19 but Herod the tetrarch—being reproved by him concerning Herodias, his brother's wife, as also about all the wicked things that Herod perpetrated—
Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
20 added this also to them all: he actually locked John up in his prison.)
Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
21 Now when all the people were baptized, Jesus, having been baptized also, was praying, when the heaven was opened
Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
22 and the Holy Spirit descended in bodily form like a dove and rested upon Him, and a Voice came out of heaven saying, “You are my beloved Son; in you I am always well pleased.”
Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
23 (Beginning His ministry at about thirty years of age, being (so it was supposed) a son of Joseph, Jesus Himself was of Eli,
Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
24 of Matthan, of Levi, of Melchi, of Janna, of Joseph,
mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
25 of Mattathiah, of Amos, of Nahum, of Esli, of Naggai,
mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
26 of Maath, of Mattathiah, of Semei, of Joseph, of Judah,
mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
27 of Joannan, of Rhesa, of Zerubbabel, of Shealtiel, of Neri,
mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
28 of Melchi, of Addi, of Cosam, of Elmodam, of Er,
mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
29 of Jose, of Eliezer, of Jorim, of Matthat, of Levi,
mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
30 of Simeon, of Judah, of Joseph, of Jonam, of Eliakim,
mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
31 of Melea, of Menan, of Mattatha, of Nathan, of David,
mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
32 of Jesse, of Obed, of Boaz, of Salmon, of Nahshon,
mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
33 of Amminadab, of Aram, of Joram, of Hezron, of Perez, of Judah,
mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
34 of Jacob, of Isaac, of Abraham, of Terah, of Nahor,
mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
35 of Serug, of Reu, of Peleg, of Eber, of Shela,
mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
36 of Cainan, of Arphaxad, of Shem, of Noah, of Lamech,
mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
37 of Methuselah, of Enoch, of Jared, of Mahalaleel, of Cainan,
mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
38 of Enosh, of Seth, of Adam, of God.)
mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

< Luke 3 >