< Nehemiah 10 >

1 And the subscribers were Nehemias, Athersatha the son of Hachelai, and Sedecias,
Amene anasindikiza chidindo anali awa: Nehemiya, bwanamkubwa uja, mwana wa Hakaliya. Zedekiya,
2 Saraias, Azarias, Jeremias,
Seraya, Azariya, Yeremiya
3 Pheshur, Amarias, Melchias,
Pasuri, Amariya, Malikiya,
4 Hattus, Sebenia, Melluch,
Hatusi, Sebaniya, Maluki,
5 Harem, Merimuth, Obdias,
Harimu, Meremoti, Obadiya,
6 Daniel, Genthon, Baruch,
Danieli, Ginetoni, Baruki,
7 Mosollam, Abia, Miamin,
Mesulamu, Abiya, Miyamini
8 Maazia, Belgia, Semeia: these were priests.
Maziya, Biligai ndi Semaya Awa anali ansembe.
9 And the Levites, Josue the son of Azanias, Bennui of the sons of Henadad. Cedmihel,
Alevi anali awa: Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa fuko la Henadadi, Kadimieli,
10 And their brethren, Sebenia, Oduia, Celita, Phalaia, Hanan,
ndi abale awo awa: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,
11 Micha, Rohob, Hasebia,
Mika, Rehobu, Hasabiya,
12 Zachur, Serebia, Sabania,
Zakuri, Serebiya, Sebaniya,
13 Odaia, Bani, Baninu.
Hodiya, Bani ndi Beninu.
14 The heads of the people, Pharos, Phahath Moab, Elam, Zethu, Bani,
Atsogoleri a anthu anali awa: Parosi, Pahati-Mowabu, Elamu, Zatu, Bani,
15 Bonni, Azgad, Bebai,
Buni, Azigadi, Bebai,
16 Adonia, Begoai, Adin,
Adoniya, Bigivai, Adini,
17 Ater, Hezecia, Azur,
Ateri, Hezekiya, Azuri,
18 Odaia, Hasum, Besai,
Hodiya, Hasumu, Bezayi
19 Hareph, Anathoth, Nebai,
Harifu, Anatoti, Nebayi,
20 Megphias, Mosollam, Hazir,
Magipiyasi, Mesulamu, Heziri
21 Mesizabel, Sadoc, Jeddua,
Mesezabeli, Zadoki, Yaduwa
22 Pheltia, Hanan, Anaia,
Pelatiya, Hanani, Ananiya,
23 Osee, Hanania, Hasub,
Hoseya, Hananiya, Hasubu
24 Alohes, Phalea, Sobec,
Halohesi, Piliha, Sobeki,
25 Rehum, Hasebna, Maasia,
Rehumu, Hasabiya, Maaseya,
26 Echaia, Hanan, Anan,
Ahiya, Hanani, Anani,
27 Melluch, Haran, Baana:
Maluki, Harimu ndi Baana.
28 And the rest of the people, priests, Levites, porters, and singing men, Nathinites, and all that had separated themselves from the people of the lands to the law of God, their wives, their sons, and their daughters.
Ife otsalafe, ndiye kuti ansembe, Alevi, alonda a ku Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu, onse amene anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina kuti atsate malamulo a Yehova, pamodzi ndi akazi athu, ana athu ndi onse amene ali ndi nzeru,
29 All that could understand promising for their brethren, with their chief men, and they came to promise, and swear that they would walk in the law of God, which he gave in the hand of Moses the servant of God, that they would do and keep all the commandments of the Lord our God, and his judgments and his ceremonies.
tikuphatikana ndi abale athu wolemekezeka, ndipo tikulonjeza molumbira kuti tidzayenda motsata malamulo a Mulungu amene anapereka kudzera mwa Mose mtumiki wa Mulungu. Tilonjeza kumvera ndi kutsata bwino mawu onse, miyambo yonse ndi malangizo onse a Yehova. Yehova atilange ngati sitidzachita zimenezi.
30 And that we would not give our daughters to the people of the land, not take their daughters for our sons.
“Ife tikulonjeza kuti sitidzapereka ana athu aakazi kuti akwatiwe ndi amuna a mayiko ena kapena kutenga ana awo aakazi kuti akwatiwe ndi ana athu aamuna.
31 And if the people of the land bring in things to sell, or any things for use, to sell them on the sabbath day, that we would not buy them of them on the sabbath, or on the holy day. And that we would leave the seventh year, and the exaction of every hand.
“Ngati anthu a mitundu ina abwera ndi zinthu za malonda, monga tirigu, kudzagulitsa pa tsiku la Sabata, sitidzawagula pa tsiku la Sabata kapena pa tsiku lina lililonse loyera. Pa chaka chilichonse cha chisanu ndi chiwiri tidzagoneka munda wosawulima ndipo tidzafafaniza ngongole zonse.
32 And we made ordinances for ourselves, to give the third part of a side every year for the work of the house of our God,
“Tikulonjezanso molumbira kuti chaka ndi chaka tizipereka magalamu anayi a siliva kuti zithandize ntchito ya ku Nyumba ya Mulungu wathu.
33 For the leaves of proposition, and for the continual sacrifice, and for a continual holocaust on the sabbaths, on the new moons, on the set feasts, and for the holy things, and for the sin offering: that atonement might be made for Israel, and for every use of the house of our God.
Ndalamayi izithandiza kulipirira buledi wa pa tebulo, chopereka cha chakudya cha nthawi zonse, zopereka zopsereza za nthawi zonse, zopereka za pa tsiku la Sabata, za pachikondwerero cha Mwezi Watsopano, za pa masiku a chikondwerero osankhika, zopereka za zinthu zopatulika, zopereka za nsembe yopepesera machimo a Aisraeli ndi ntchito ina iliyonse ya ku Nyumba ya Mulungu.
34 And we cast lots among the priests, and the Levites, and the people for the offering of wood, that it might be brought into the house of our God by the houses of our fathers at set times, from year to year: to burn upon the altar of the Lord our God, as it is written in the law of Moses:
“Ife ansembe, Alevi ndi anthu onse, tachita maere kuti tidziwe pamene banja lathu lililonse lidzabweretsa ku nyumba ya Mulungu wathu pa nthawi yoyikika ya chaka zopereka za nkhuni zoyaka pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wathu, monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo.”
35 And that we would bring the first fruits of our land, and the firstfruits of all fruit of every tree, from year to year, in the house of our Lord.
“Tilonjezanso kuti tidzabwera ndi zipatso zoyamba kucha za mʼminda yathu ndi zipatso zoyamba kucha za mtengo uliwonse wa zipatso chaka ndi chaka kuti tidzapereke ku Nyumba ya Mulungu wathu.”
36 And the firstborn of our sons, and of our cattle, as it is written in the law, and the firstlings of our oxen, and of our sheep, to be offered in the house of our God, to the priests who minister in the house of our God.
“Tidzabweranso nawo ku Nyumba ya Mulungu, kwa ansembe amene amatumikira ku Nyumba ya Mulungu ana athu aamuna oyamba kubadwa ndi ana angʼombe oyamba kubadwa monga zalembedwera mu Malamulo. Tidzaperekanso ana oyamba kubadwa a ziweto zathu ndi ana ankhosa oyamba kubadwa.”
37 And that we would bring the firstfruits of our meats, and of our libations, and the fruit of every tree, of the vintage also and of oil to the priests, to the storehouse of our God, and the tithes of our ground to the Levites. The Levites also shall receive the tithes of our works out of all the cities.
“Ndiponso ku zipinda za Nyumba ya Mulungu wathu, kwa ansembe tidzaperekanso mtanda wathu wa buledi wa ufa ndi mphatso zina monga zipatso za mtengo uliwonse, vinyo ndi mafuta. Tidzaperekanso kwa alevi chakhumi cha mbewu zathu pakuti alevi ndiwo amasonkhanitsa chakhumi mʼmidzi yathu yonse.
38 And the priest the son of Aaron shall be with the Levites in the tithes of the Levites, and the Levites shall offer the tithe of their tithes in the house of our God, to the storeroom into the treasure house.
Wansembe, mdzukulu wa Aaroni azikhala pamodzi ndi Alevi pamene akulandira chakhumi. Ndipo Alevi azibwera ndi chakhumicho ku nyumba ya Mulungu wathu, kuzipinda zosungiramo chuma.”
39 For the children of Israel and the children of Levi shall carry to the treasury the firstfruits of corn, of wine, and of oil: and the sanctified vessels shall be there, and the priests, and the singing men, and the porters, and ministers, and we will not forsake the house of our God.
Choncho Israeli, kuphatikiza zidzukulu za Alevi, azipititsa zopereka za tirigu, vinyo ndi mafuta ku zipinda zosungiramo katundu wopatulika, komanso kokhala ansembe amene akutumikira pamodzi ndi alonda a ku Nyumba ya Mulungu ndi anthu oyimba nyimbo. “Kwambiri ife sitidzaleka kusamala Nyumba ya Mulungu.”

< Nehemiah 10 >