< Leviticus 21 >

1 The Lord said also to Moses: Speak to the priests the sons of Aaron, and thou shalt say to them: Let not a priest incur an uncleanness at the death of his citizens:
Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
2 But only for his kin, such as are near in blood, that is to say, for his father and for his mother, and for his son, and for his daughter, for his brother also,
Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
3 And for a maiden sister, who hath had no husband:
kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
4 But not even for the prince of his people shall he do any thing that may make him unclean.
Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
5 Neither shall they shave their head, nor their beard, nor make incisions in their flesh.
“‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
6 They shall be holy to their God, and shall not profane his name: for they offer the burnt offering of the Lord, and the bread of their God, and therefore they shall be holy.
Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
7 They shall not take to wife a harlot or a vile prostitute, nor one that has been put away from her husband: because they are consecrated to their God,
“‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
8 And offer the leaves of proposition. Let them therefore be holy, because I also am holy, the Lord, who sanctify them.
Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
9 If the daughter of a priest be taken in whoredom, and dishonour the name of her father, she shall be burnt with fire.
“‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
10 The high priest, that is to say, the priest, is the greatest among his brethren. upon whose head the oil of unction hath been poured, and whose hands have been consecrated for the priesthood, and who hath been vested with the holy vestments, shall not uncover his head, he shall not rend his garments:
“‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
11 Nor shall he go in at all to any dead person: not even for his father, or his mother, shall he be defiled:
Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
12 Neither shall he go out of the holy places, lest he defile the sanctuary of the Lord, because the oil of the holy unction of his God is upon him. I am the Lord.
Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
13 He shall take a virgin unto his wife:
“‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
14 But a widow or one that is divorced, or defiled, or a harlot, he shall not take, but a maid of his own people:
Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
15 He shall not mingle the stock of his kindred with the common people of his nation: for I am the Lord who sanctify him.
kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
16 And the Lord spoke to Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Say to Aaron: Whosoever of thy seed throughout their families, hath a blemish, he shall not offer bread to his God.
“Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
18 Neither shall he approach to minister to him: If he be blind, if he be lame, if he have a little, or a great, or a crooked nose,
Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
19 If his foot, or if his hand be broken,
munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
20 If he be crookbacked, or blear eyed, or have a pearl in his eye, or a continual scab, or a dry scurf in his body, or a rupture:
kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
21 Whosoever of the seed of Aaron the priest hath a blemish, he shall not approach to offer sacrifices to the Lord, nor bread to his God.
Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
22 He shall eat nevertheless of the loaves, that are offered in the sanctuary,
Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
23 Yet so that he enter not within the veil, nor approach to the altar, because he hath a blemish, and he must not defile my sanctuary. I am the Lord who sanctify them.
Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
24 Moses therefore spoke to Aaron, and to his sons and to all Israel, all the things that had been commanded him.
Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.

< Leviticus 21 >