< 1 Chronicles 14 >

1 And Hiram king of Tyre sent messengers to David, and cedar trees, and masons, and carpenters, to build him a house.
Hiramu mfumu ya ku Turo inatumiza amithenga kwa Davide pamodzi ndi mitengo ya mkungudza ndiponso amisiri a miyala ndi amisiri a matabwa kuti adzamumangire nyumba yaufumu.
2 And David perceived that the Lord had confirmed him king over Israel, and that his kingdom was exalted over his people Israel.
Choncho Davide anazindikira kuti Yehova wamukhazikitsa kukhala mfumu ya Israeli ndipo wakuza kwambiri ufumu wake chifukwa cha anthu ake, Aisraeli.
3 And David took other wives in Jerusalem: and he beget sons, and daughters.
Davide anakwatira akazi ena ambiri ku Yerusalemu ndipo anabereka ana aamuna ndi aakazi ambiri.
4 Now these are the names of them that were born to him in Jerusalem: Samua, and Sobad, Nathan, and Solomon,
Mayina a ana amene anaberekera ku Yerusalemu anali awa: Samua, Sobabu, Natani, Solomoni,
5 Jebahar, and Elisua, and Eliphalet,
Ibihari, Elisua, Elipeleti,
6 And Noga, and Napheg, and Japhia,
Noga, Nefegi, Yafiya,
7 Elisama. and Baaliada, and Eliphalet.
Elisama, Beeliada ndi Elifeleti.
8 And the Philistines hearing that David was anointed king over all Israel, went all up to seek him: and David heard of it, and went out against them.
Afilisti atamva kuti Davide wadzozedwa kukhala mfumu ya dziko lonse la Israeli, iwo anapita mwamphamvu kukamusakasaka. Koma Davide atamva zimenezi anapita kukakumana nawo.
9 And the Philistines came and spread themselves in the vale of Raphaim.
Ndipo Afilisti anabwera ndi kulanda zinthu mʼChigwa cha Refaimu.
10 And David consulted the Lord, saying: Shall I go up against the Philistines, and wilt thou deliver them into my hand? And the Lord said to him: Go up, and I will deliver them into thy hand.
Davide anafunsa Mulungu kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Afilisti? Kodi mukawapereka mʼmanja mwanga?” Yehova anamuyankha kuti, “Pita, Ine ndidzawapereka mʼmanja mwako.”
11 And when they were come to Baalpharasim, David defeated them there, and he said: God hath divided my enemies by my hand, as waters are divided: and therefore the name of that place was called Baalpharasim.
Choncho Davide ndi anthu ake anapita ku Baala-Perazimu ndi kugonjetsa Afilistiwo. Iye anati, “Monga amasefukira madzi, Mulungu waphwanya adani anga ine ndikuona.” Motero anawatcha malowa Baala Perazimu.
12 And they left there their gods, and David commanded that they should be burnt.
Afilisti anasiya milungu yawo kumeneko ndipo Davide analamulira kuti itenthedwe ndi moto.
13 Another time also the Philistines made an irruption, and spread themselves abroad in the valley.
Nthawi inanso Afilisti anadzalanda katundu mu Chigwamo.
14 And David consulted God again, and God said to him: Go not up after them, turn away from them, and come upon them over against the pear trees.
Choncho Davide anafunsa Mulungu ndipo Mulunguyo anayankha kuti, “Usapite molunjika, koma uzungulire kumbuyo kwawo. Ukawathire nkhondo patsogolo pa mitengo ya mkandankhuku.
15 And when thou shalt hear the sound of one going in the tops of the pear trees, then shalt thou go out to battle. For God is gone out before thee to strike the army of the Philistines.
Mukakangomva phokoso pa msonga za mitengo ya mkandankhuku, mukapite kukamenyana nawo, chifukwa izi zikasonyeza kuti Mulungu ali patsogolo panu kukantha ankhondo a Afilisti.”
16 And David did as God had commanded him, and defeated the army of the Philistines, slaying them from Gabaon to Gazera.
Kotero Davide anachita zimene Mulungu anamulamulira ndipo anakantha ankhondo a Afilisti njira yonse kuchokera ku Gibiyoni mpaka ku Gezeri.
17 And the name of David became famous in all countries, and the Lord made all nations fear him.
Choncho mbiri ya Davide inafalikira dziko lonse, ndipo Yehova anachititsa kuti mayiko ena azimuopa.

< 1 Chronicles 14 >