< Psalms 96 >

1 Sing ye unto Jehovah a new song: sing unto Jehovah, all the earth.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Sing unto Jehovah, bless his name; publish his salvation from day to day.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Declare his glory among the nations, his wondrous works among all the peoples.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 For Jehovah is great and exceedingly to be praised; he is terrible above all gods.
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 For all the gods of the peoples are idols; but Jehovah made the heavens.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 Majesty and splendour are before him; strength and beauty are in his sanctuary.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Give unto Jehovah, ye families of peoples, give unto Jehovah glory and strength;
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Give unto Jehovah the glory of his name; bring an oblation and come into his courts;
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Worship Jehovah in holy splendour; tremble before him, all the earth.
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Say among the nations, Jehovah reigneth! yea, the world is established, it shall not be moved; he will execute judgment upon the peoples with equity.
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Let the heavens rejoice, and let the earth be glad; let the sea roar, and the fulness thereof;
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Let the field exult and all that is therein. Then shall all the trees of the forest sing for joy,
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 Before Jehovah, for he cometh; for he cometh to judge the earth: he will judge the world with righteousness, and the peoples in his faithfulness.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

< Psalms 96 >