< Psalms 76 >

1 To the chief Musician. On stringed instruments. A Psalm of Asaph: a Song. In Judah is God known, his name is great in Israel;
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu. Mulungu amadziwika mu Yuda; dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.
2 And in Salem is his tent, and his dwelling-place in Zion.
Tenti yake ili mu Salemu, malo ake okhalamo mu Ziyoni.
3 There broke he the flashings of the bow, shield and sword and battle. (Selah)
Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka, zishango ndi malupanga, zida zankhondo. (Sela)
4 More glorious art thou, more excellent, than the mountains of prey.
Wolemekezeka ndinu, wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.
5 The stout-hearted are made a spoil, they have slept their sleep; and none of the men of might have found their hands.
Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma, Iwowo amagona tulo tawo totsiriza; palibe mmodzi wamphamvu amene angatukule manja ake.
6 At thy rebuke, O God of Jacob, both chariot and horse are cast into a dead sleep.
Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo, kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.
7 Thou, thou art to be feared, and who can stand before thee when once thou art angry?
Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa. Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?
8 Thou didst cause judgment to be heard from the heavens; the earth feared, and was still,
Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo, ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,
9 When God rose up to judgment, to save all the meek of the earth. (Selah)
pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze, kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko. (Sela)
10 For the fury of man shall praise thee; the remainder of fury wilt thou gird on thyself.
Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.
11 Vow and pay unto Jehovah your God: let all that are round about him bring presents unto him that is to be feared.
Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse; anthu onse omuzungulira abweretse mphatso kwa Iye amene ayenera kuopedwa.
12 He cutteth off the spirit of princes; [he] is terrible to the kings of the earth.
Iye amaswa mzimu wa olamulira; amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

< Psalms 76 >