< Psalms 43 >

1 Judge me, O God, and plead my cause against an ungodly nation; deliver me from the deceitful and unrighteous man.
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 For thou art the God of my strength: why hast thou cast me off? why go I about mourning because of the oppression of the enemy?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Send out thy light and thy truth: they shall lead me, they shall bring me to thy holy mount, and unto thy habitations.
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 Then will I go unto the altar of God, unto the God of the gladness of my joy: yea, upon the harp will I praise thee, O God, my God.
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Why art thou cast down, my soul? and why art thou disquieted within me? hope in God; for I shall yet praise him, [who is] the health of my countenance, and my God.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.

< Psalms 43 >