< Psalms 22 >

1 To the chief Musician. Upon Aijeleth-Shahar. A Psalm of David. My God, my God, why hast thou forsaken me? [why art thou] far from my salvation, from the words of my groaning?
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide. Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya? Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe? Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?
2 My God, I cry by day, and thou answerest not; and by night, and there is no rest for me:
Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha, usikunso, ndipo sindikhala chete.
3 And thou art holy, thou that dwellest amid the praises of Israel.
Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu; ndinu matamando a Israeli.
4 Our fathers confided in thee: they confided, and thou didst deliver them.
Pa inu makolo athu anadalira; iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.
5 They cried unto thee, and were delivered; they confided in thee, and were not confounded.
Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa. Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.
6 But I am a worm, and no man; a reproach of men, and the despised of the people.
Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu, wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.
7 All they that see me laugh me to scorn; they shoot out the lip, they shake the head, [saying: ]
Onse amene amandiona amandiseka; amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti
8 Commit it to Jehovah — let him rescue him; let him deliver him, because he delighteth in him!
“Iyeyu amadalira Yehova, musiyeni Yehovayo amulanditse. Musiyeni Yehova amupulumutse popeza amakondwera mwa Yehovayo.”
9 But thou art he that took me out of the womb; thou didst make me trust, upon my mother's breasts.
Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga. Munachititsa kuti ndizikudalirani ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.
10 I was cast upon thee from the womb; thou art my God from my mother's belly.
Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu; kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.
11 Be not far from me, for trouble is near; for there is none to help.
Musakhale kutali ndi ine, pakuti mavuto ali pafupi ndipo palibe wina wondipulumutsa.
12 Many bulls have encompassed me; Bashan's strong ones have beset me round.
Ngʼombe zazimuna zandizungulira; ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.
13 They gape upon me with their mouth, [as] a ravening and a roaring lion.
Mikango yobangula pokadzula nyama, yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.
14 I am poured out like water, and all my bones are out of joint: my heart is become like wax; it is melted in the midst of my bowels.
Ine ndatayika pansi ngati madzi ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake. Mtima wanga wasanduka phula; wasungunuka mʼkati mwanga.
15 My strength is dried up like a potsherd, and my tongue cleaveth to my palate; and thou hast laid me in the dust of death.
Mphamvu zanga zauma ngati phale, ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada; mwandigoneka mʼfumbi la imfa.
16 For dogs have encompassed me; an assembly of evil-doers have surrounded me: they pierced my hands and my feet.
Agalu andizungulira; gulu la anthu oyipa landizinga. Alasa manja ndi mapazi anga.
17 I may count all my bones. They look, they stare upon me;
Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse; anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.
18 They part my garments among them, and cast lots upon my vesture.
Iwo agawana zovala zanga pakati pawo ndi kuchita maere pa zovala zangazo.
19 But thou, Jehovah, be not far [from me]; O my strength, haste thee to help me.
Koma Inu Yehova, musakhale kutali; Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.
20 Deliver my soul from the sword; my only one from the power of the dog;
Pulumutsani moyo wanga ku lupanga, moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.
21 Save me from the lion's mouth. Yea, from the horns of the buffaloes hast thou answered me.
Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango; pulumutseni ku nyanga za njati.
22 I will declare thy name unto my brethren, in the midst of the congregation will I praise thee.
Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga; ndidzakutamandani mu msonkhano.
23 Ye that fear Jehovah, praise him; all ye the seed of Jacob, glorify him; and revere him, all ye the seed of Israel.
Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni! Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni! Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!
24 For he hath not despised nor abhorred the affliction of the afflicted; neither hath he hid his face from him: but when he cried unto him, he heard.
Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza kuvutika kwa wosautsidwayo; Iye sanabise nkhope yake kwa iye. Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.
25 My praise is from thee, in the great congregation; I will pay my vows before them that fear him.
Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira. Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.
26 The meek shall eat and be satisfied; they shall praise Jehovah that seek him: your heart shall live for ever.
Osauka adzadya ndipo adzakhuta; iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda. Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!
27 All the ends of the earth shall remember and turn unto Jehovah, and all the families of the nations shall worship before thee:
Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye, ndipo mabanja a mitundu ya anthu adzawerama pamaso pake,
28 For the kingdom is Jehovah's, and he ruleth among the nations.
pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.
29 All the fat ones of the earth shall eat and worship; all they that go down to the dust shall bow before him, and he that cannot keep alive his own soul.
Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira; onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake; iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.
30 A seed shall serve him; it shall be accounted to the Lord for a generation.
Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye; mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.
31 They shall come, and shall declare his righteousness unto a people that shall be born, that he hath done [it].
Iwo adzalengeza za chilungamo chake kwa anthu amene pano sanabadwe pakuti Iye wachita zimenezi.

< Psalms 22 >