< Psalms 147 >

1 Praise ye Jah! for it is good. Sing psalms of our God; for it is pleasant: praise is comely.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 Jehovah doth build up Jerusalem: he gathereth the outcasts of Israel.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 He healeth the broken in heart, and bindeth up their wounds.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 He counteth the number of the stars; he giveth names to them all.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Great is our Lord, and of great power: his understanding is infinite.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 Jehovah lifteth up the meek; he abaseth the wicked to the earth.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Sing unto Jehovah with thanksgiving; sing psalms upon the harp unto our God:
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Who covereth the heavens with clouds, who prepareth rain for the earth, who maketh grass to grow upon the mountains;
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Who giveth to the cattle their food, to the young ravens which cry.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 He delighteth not in the strength of the horse, he taketh not pleasure in the legs of a man;
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 Jehovah taketh pleasure in those that fear him, in those that hope in his loving-kindness.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Laud Jehovah, O Jerusalem; praise thy God, O Zion.
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 For he hath strengthened the bars of thy gates; he hath blessed thy children within thee;
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 He maketh peace in thy borders; he satisfieth thee with the finest of the wheat.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 He sendeth forth his oracles to the earth: his word runneth very swiftly.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 He giveth snow like wool, scattereth the hoar frost like ashes;
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 He casteth forth his ice like morsels: who can stand before his cold?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 He sendeth his word, and melteth them; he causeth his wind to blow — the waters flow.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 He sheweth his word unto Jacob, his statutes and his judgments unto Israel.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 He hath not dealt thus with any nation; and as for [his] judgments, they have not known them. Hallelujah!
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psalms 147 >