< Proverbs 3 >

1 My son, forget not my teaching, and let thy heart observe my commandments;
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 for length of days, and years of life, and peace shall they add to thee.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Let not loving-kindness and truth forsake thee; bind them about thy neck, write them upon the tablet of thy heart:
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 and thou shalt find favour and good understanding in the sight of God and man.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Confide in Jehovah with all thy heart, and lean not unto thine own intelligence;
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 in all thy ways acknowledge him, and he will make plain thy paths.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Be not wise in thine own eyes; fear Jehovah, and depart from evil:
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 it shall be health for thy navel, and moisture for thy bones.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Honour Jehovah with thy substance, and with the first-fruits of all thine increase;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 so shall thy barns be filled with plenty, and thy vats shall overflow with new wine.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 My son, despise not the instruction of Jehovah, neither be weary of his chastisement;
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 for whom Jehovah loveth he chasteneth, even as a father the son in whom he delighteth.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Blessed is the man that findeth wisdom, and the man that getteth understanding.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 For the gain thereof is better than the gain of silver, and her revenue than fine gold.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 She is more precious than rubies; and all the things thou canst desire are not equal unto her.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Length of days is in her right hand; in her left hand riches and honour.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Her ways are ways of pleasantness, and all her paths are peace.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 She is a tree of life to them that lay hold upon her; and happy is he that retaineth her.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Jehovah by wisdom founded the earth; by understanding he established the heavens.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 By his knowledge the deeps were broken up, and the skies drop down the dew.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 My son, let them not depart from thine eyes; keep sound wisdom and discretion:
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 so shall they be life unto thy soul, and grace unto thy neck.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Then shalt thou walk in thy way securely, and thy foot shall not stumble;
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 when thou liest down, thou shalt not be afraid, but thou shalt lie down and thy sleep shall be sweet.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Be not afraid of sudden fear, neither of the destruction of the wicked, when it cometh;
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 for Jehovah shall be thy confidence, and he will keep thy foot from being taken.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Withhold not good from them to whom it is due, when it is in the power of thy hand to do it.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Say not unto thy neighbour, Go, and come again, and to-morrow I will give, when thou hast it by thee.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Devise not evil against thy neighbour, seeing he dwelleth securely by thee.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Strive not with a man without cause, if he have done thee no harm.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Envy not the man of violence, and choose none of his ways.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 For the perverse is an abomination to Jehovah; but his secret is with the upright.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 The curse of Jehovah is in the house of the wicked; but he blesseth the habitation of the righteous.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 He indeed scorneth the scorners; but he giveth grace unto the lowly.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 The wise shall inherit glory; but shame shall be the promotion of the foolish.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Proverbs 3 >