< Proverbs 28 >

1 The wicked flee when no man pursueth; but the righteous are bold as a lion.
Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
2 By the transgression of a land many are the princes thereof; but by a man of understanding [and] of knowledge, [its] stability is prolonged.
Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
3 A poor man who oppresseth the helpless is a sweeping rain which leaveth no food.
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
4 They that forsake the law praise the wicked; but such as keep the law contend with them.
Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
5 Evil men understand not judgment; but they that seek Jehovah understand everything.
Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
6 Better is the poor that walketh in his integrity, than he that is perverse, double in ways, though he be rich.
Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
7 Whoso observeth the law is a son that hath understanding; but he that is a companion of profligates bringeth shame to his father.
Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
8 He that by usury and unjust gain increaseth his substance gathereth it for him that is gracious to the poor.
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9 He that turneth away his ear from hearing the law, even his prayer is an abomination.
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
10 Whoso causeth the upright to go astray in an evil way, shall himself fall into his own pit; but the perfect shall inherit good.
Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
11 A rich man is wise in his own eyes; but the poor that hath understanding searcheth him out.
Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
12 When the righteous triumph, there is great glory; but when the wicked rise, men conceal themselves.
Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
13 He that covereth his transgressions shall not prosper; but whoso confesseth and forsaketh [them] shall obtain mercy.
Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
14 Happy is the man that feareth always; but he that hardeneth his heart shall fall into evil.
Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
15 A roaring lion, and a ranging bear, is a wicked ruler over a poor people.
Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
16 The prince void of intelligence is also a great oppressor: he that hateth covetousness shall prolong [his] days.
Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
17 A man laden with the blood of [any] person, fleeth to the pit: let no man stay him.
Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
18 Whoso walketh in integrity shall be saved; but he that is perverted in [his] double ways, shall fall in one [of them].
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
19 He that tilleth his land shall be satisfied with bread; but he that followeth the worthless shall have poverty enough.
Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
20 A faithful man aboundeth with blessings; but he that maketh haste to be rich shall not be innocent.
Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
21 To have respect of persons is not good; but for a piece of bread will a man transgress.
Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22 He that hath an evil eye hasteth after wealth, and knoweth not that poverty shall come upon him.
Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
23 He that rebuketh a man shall afterwards find more favour than he that flattereth with the tongue.
Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
24 Whoso robbeth his father and his mother, and saith, It is no transgression, the same is the companion of a destroyer.
Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
25 He that is puffed up in soul exciteth contention; but he that relieth upon Jehovah shall be made fat.
Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
26 He that confideth in his own heart is a fool; but whoso walketh wisely, he shall be delivered.
Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
27 He that giveth unto the poor shall not lack; but he that withdraweth his eyes shall have many a curse.
Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28 When the wicked rise, men hide themselves; but when they perish, the righteous increase.
Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

< Proverbs 28 >