< Numbers 34 >

1 And Jehovah spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Command the children of Israel, and say unto them, When ye come into the land of Canaan, this shall be the land that shall fall to you for an inheritance, the land of Canaan according to the borders thereof.
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 Then your south side shall be from the wilderness of Zin alongside of Edom, and your southern border shall be from the end of the salt sea eastward;
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 and your border shall turn from the south of the ascent of Akrabbim, and pass on to Zin, and shall end southward at Kadesh-barnea, and shall go on to Hazar-Addar, and pass on to Azmon.
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
5 And the border shall turn from Azmon unto the torrent of Egypt, and shall end at the sea.
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 And as west border ye shall have the great sea, and [its] coast. This shall be your west border.
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
7 And this shall be your north border: from the great sea ye shall mark out for you mount Hor;
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
8 from mount Hor ye shall mark out the entrance to Hamath, and the end of the border shall be toward Zedad;
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 and the border shall go to Ziphron, and shall end at Hazar-enan. This shall be your north border.
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 And ye shall mark out for you as eastern border from Hazar-enan to Shepham:
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 and the border shall go down from Shepham to Riblah, on the east side of Ain; and the border shall descend, and shall strike upon the extremity of the sea of Chinnereth eastward;
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 and the border shall go down to the Jordan, and shall end at the salt sea. This shall be your land according to the borders thereof round about.
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 And Moses commanded the children of Israel, saying, This is the land which ye shall take for yourselves as inheritance by lot, which Jehovah commanded to give to the nine tribes, and to the half tribe.
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 For the tribe of the children of the Reubenites according to their fathers' houses, and the tribe of the children of the Gadites according to their fathers' houses, have received, and half the tribe of Manasseh have received their inheritance;
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 the two tribes and the half tribe have received their inheritance on this side the Jordan of Jericho eastward, toward the sun-rising.
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
16 And Jehovah spoke to Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
17 These are the names of the men who shall divide the land unto you: Eleazar the priest, and Joshua the son of Nun.
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 And ye shall take one prince of every tribe, to divide the land.
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 And these are the names of the men: for the tribe of Judah, Caleb the son of Jephunneh;
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
20 and for the tribe of the children of Simeon, Samuel the son of Ammihud;
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
21 for the tribe of Benjamin, Elidad the son of Chislon;
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
22 and for the tribe of the children of Dan, a prince, Bukki the son of Jogli;
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 for the children of Joseph: for the tribe of the children of Manasseh, a prince, Hanniel the son of Ephod,
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 and for the tribe of the children of Ephraim, a prince, Kemuel the son of Shiphtan;
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 and for the tribe of the children of Zebulun, a prince, Elizaphan the son of Pharnach;
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 and for the tribe of the children of Issachar, a prince, Phaltiel the son of Azzan;
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 and for the tribe of the children of Asher, a prince, Ahihud the son of Shelomi;
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 and for the tribe of the children of Naphtali, a prince, Phedahel the son of Ammihud.
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 These are they whom Jehovah commanded to distribute to the children of Israel their inheritance in the land of Canaan.
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.

< Numbers 34 >