< Nehemiah 7 >

1 And it came to pass when the wall was built, and I had set up the doors, that the doorkeepers and the singers and the Levites were appointed.
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 And I gave my brother Hanani, and Hananiah the ruler of the citadel, charge over Jerusalem; for he was a faithful man and feared God above many.
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 And I said to them that the gates of Jerusalem should not be opened until the sun was hot, and that they should shut the doors and bar them while they stood by; and that there should be appointed watches of the inhabitants of Jerusalem, every one in his watch, and every one over against his house.
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 Now the city was large and great; but the people in it were few, and no houses were built.
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 And my God put into my heart to gather together the nobles, and the rulers, and the people, for registration by genealogy. And I found a genealogical register of those that had come up at the first, and I found written in it:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 These are the children of the province that went up out of the captivity of those that had been carried away, whom Nebuchadnezzar the king of Babylon had carried away, and who came again to Jerusalem and to Judah, every one to his city;
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 those who came with Zerubbabel, Jeshua, Nehemiah, Azariah, Raamiah, Nahamani, Mordecai, Bilshan, Mispereth, Bigvai, Nehum, Baanah. The number of the men of the people of Israel:
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 The children of Parosh, two thousand one hundred and seventy-two.
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 The children of Shephatiah, three hundred and seventy-two.
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 The children of Arah, six hundred and fifty-two.
Zidzukulu za Ara 652
11 The children of Pahath-Moab, of the children of Jeshua and Joab, two thousand eight hundred and eighteen.
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 The children of Elam, a thousand two hundred and fifty-four.
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 The children of Zattu, eight hundred and forty-five.
Zidzukulu za Zatu 845
14 The children of Zaccai, seven hundred and sixty.
Zidzukulu za Zakai 760
15 The children of Binnui, six hundred and forty-eight.
Zidzukulu za Binuyi 648
16 The children of Bebai, six hundred and twenty-eight.
Zidzukulu za Bebai 628
17 The children of Azgad, two thousand three hundred and twenty-two.
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 The children of Adonikam, six hundred and sixty-seven.
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 The children of Bigvai, two thousand and sixty-seven.
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 The children of Adin, six hundred and fifty-five.
Zidzukulu za Adini 655
21 The children of Ater of [the family of] Hezekiah, ninety-eight.
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 The children of Hashum, three hundred and twenty-eight.
Zidzukulu za Hasumu 328
23 The children of Bezai, three hundred and twenty-four.
Zidzukulu za Bezayi 324
24 The children of Hariph, a hundred and twelve.
Zidzukulu za Harifu 112
25 The children of Gibeon, ninety-five.
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 The men of Bethlehem and Netophah, a hundred and eighty-eight.
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 The men of Anathoth, a hundred and twenty-eight.
Anthu a ku Anatoti 128
28 The men of Beth-azmaveth, forty-two.
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 The men of Kirjath-jearim, Chephirah, and Beeroth, seven hundred and forty-three.
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 The men of Ramah and Geba, six hundred and twenty-one.
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 The men of Michmas, a hundred and twenty-two.
Anthu a ku Mikimasi 122
32 The men of Bethel and Ai, a hundred and twenty-three.
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 The men of the other Nebo, fifty-two.
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 The children of the other Elam, a thousand two hundred and fifty-four.
Ana a Elamu wina 1,254
35 The children of Harim, three hundred and twenty.
Zidzukulu za Harimu 320
36 The children of Jericho, three hundred and forty-five.
Zidzukulu za Yeriko 345
37 The children of Lod, Hadid, and Ono, seven hundred and twenty-one.
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 The children of Senaah, three thousand nine hundred and thirty.
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 The priests: the children of Jedaiah, of the house of Jeshua, nine hundred and seventy-three.
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 The children of Immer, a thousand and fifty-two.
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 The children of Pashhur, a thousand two hundred and forty-seven.
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 The children of Harim, a thousand and seventeen.
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 The Levites: the children of Jeshua [and] of Kadmiel, of the children of Hodvah, seventy-four.
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 The singers: the children of Asaph, a hundred and forty-eight.
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 The doorkeepers: the children of Shallum, the children of Ater, the children of Talmon, the children of Akkub, the children of Hatita, the children of Shobai, a hundred and thirty-eight.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 The Nethinim: the children of Ziha, the children of Hasupha, the children of Tabbaoth,
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 the children of Keros, the children of Sia, the children of Padon,
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 the children of Lebana, the children of Hagaba, the children of Salmai,
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 the children of Hanan, the children of Giddel, the children of Gahar,
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 the children of Reaiah, the children of Rezin, the children of Nekoda,
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 the children of Gazzam, the children of Uzza, the children of Phaseah,
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 the children of Besai, the children of Meunim, the children of Nephishesim,
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 the children of Bakbuk, the children of Hakupha, the children of Harhur,
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 the children of Bazlith, the children of Mehida, the children of Harsha,
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 the children of Barkos, the children of Sisera, the children of Thamah,
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 the children of Neziah, the children of Hatipha.
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 The children of Solomon's servants: the children of Sotai, the children of Sophereth, the children of Perida,
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 the children of Jaala, the children of Darkon, the children of Giddel,
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 the children of Shephatiah, the children of Hattil, the children of Pochereth-Hazzebaim, the children of Amon.
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 All the Nethinim, and the children of Solomon's servants, three hundred and ninety-two.
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 And these are they that went up from Tel-melah, Tel-harsha, Cherub-Addon and Immer; but they could not shew their father's house, nor their seed, whether they were of Israel.
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 The children of Delaiah, the children of Tobijah, the children of Nekoda, six hundred and forty-two.
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 And of the priests: the children of Hobaiah, the children of Koz, the children of Barzillai, who took a wife of the daughters of Barzillai the Gileadite and was called after their name.
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 These sought their genealogical register, but it was not found; therefore were they, as polluted, removed from the priesthood.
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 And the Tirshatha said to them that they should not eat of the most holy things, till there stood up the priest with Urim and Thummim.
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 The whole congregation together was forty-two thousand three hundred and sixty,
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 besides their servants and their maids, of whom there were seven thousand three hundred and thirty-seven; and they had two hundred and forty-five singing-men and singing-women.
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68 Their horses were seven hundred and thirty-six; their mules, two hundred and forty-five;
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 the camels, four hundred and thirty-five; the asses, six thousand seven hundred and twenty.
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 And some of the chief fathers gave to the work. The Tirshatha gave to the treasure a thousand darics of gold, fifty basons, five hundred and thirty priests' coats.
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 And [some] of the chief fathers gave to the treasure of the work twenty thousand darics of gold, and two thousand two hundred pounds of silver.
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 And that which the rest of the people gave was twenty thousand darics of gold, and two thousand pounds of silver, and sixty-seven priests' coats.
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 And the priests, and the Levites, and the doorkeepers, and the singers, and [some] of the people, and the Nethinim, and all Israel, dwelt in their cities. And when the seventh month came, and the children of Israel were in their cities,
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.

< Nehemiah 7 >