< Matthew 14 >

1 At that time Herod the tetrarch heard of the fame of Jesus,
Pa nthawi imeneyo Mfumu Herode anamva za mbiri ya Yesu.
2 and said to his servants, This is John the baptist: he is risen from the dead, and because of this these works of power display their force in him.
Ndipo iye anati kwa antchito ake, “Uyu ndi Yohane Mʼbatizi; iye wauka kwa akufa! Ichi ndi chifukwa chake mphamvu zodabwitsa zikugwira ntchito mwa iye.”
3 For Herod had seized John, and had bound him and put him in prison on account of Herodias the wife of Philip his brother.
Pakuti Herode anamugwira Yohane ndi kumumanga ndipo anamuyika mʼndende chifukwa cha Herodia mkazi wa mʼbale wake Filipo.
4 For John said to him, It is not lawful for thee to have her.
Chifukwa Yohane anakhala akunena kwa iye kuti, “Sichololedwa kwa inu kutenga mkaziyo.”
5 And [while] desiring to kill him, he feared the crowd, because they held him for a prophet.
Herode anafuna kupha Yohane koma iye anaopa anthu chifukwa anamuyesa iye mneneri.
6 But when Herod's birthday was celebrated, the daughter of Herodias danced before them, and pleased Herod;
Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwa Herode, mwana wamkazi wa Herodia anavina pamaso pa anthu ndipo anasangalatsa kwambiri.
7 whereupon he promised with oath to give her whatsoever she should ask.
Kotero Herode analonjeza ndi lumbiro kumupatsa chilichonse chimene mwanayo angamupemphe.
8 But she, being set on by her mother, says, Give me here upon a dish the head of John the baptist.
Ndipo atamupangira amayi ake anati, “Mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
9 And the king was grieved; but on account of the oaths, and those lying at table with [him], he commanded [it] to be given.
Mfumuyo inamva chisoni koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo amene anali pa phwando lake analamulira kuti chofuna chake chipatsidwe;
10 And he sent and beheaded John in the prison;
ndipo anakadula mutu wa Yohane mʼndende.
11 and his head was brought upon a dish, and was given to the damsel, and she carried [it] to her mother.
Mutu wake anawubweretsa mʼmbale ndi kumupatsa mtsikanayo amene anawutengera kwa amayi ake.
12 And his disciples came and took the body and buried it, and came and brought word to Jesus.
Ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo wake ndi kukawuyika mʼmanda. Pomwepo iwo anapita kukamuwuza Yesu.
13 And Jesus, having heard it, went away thence by ship to a desert place apart. And the crowds having heard [of it] followed him on foot from the cities.
Yesu atamva zimene zinachitika, anachoka pa bwato mwachinsinsi kupita kumalo a yekha. Magulu a anthu atamva izi anamutsatira Iye poyenda pansi kuchokera ku mizinda.
14 And going out he saw a great crowd, and was moved with compassion about them, and healed their infirm.
Yesu atafika ku mtunda, ndi kuona gulu lalikulu la anthu, Iye anamva nawo chifundo ndipo anachiritsa odwala awo.
15 But when even was come, his disciples came to him saying, The place is desert, and [much of] the [day] time already gone by; dismiss the crowds, that they may go into the villages and buy food for themselves.
Kutayamba mdima, ophunzira anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kutchire ndipo kwayamba kale kuda. Awuzeni anthu azipita kuti afike ku midzi ndi kukadzigulira zakudya.”
16 But Jesus said to them, They have no need to go: give ye them to eat.
Yesu anawayankha kuti, “Sikofunika kuti azipita. Inuyo muwapatse kanthu kuti adye.”
17 But they say to him, We have not here save five loaves and two fishes.
Iwo anayankha kuti, “Tili ndi malofu asanu okha a buledi ndi nsomba ziwiri.”
18 And he said, Bring them here to me.
Koma Iye anati, “Bweretsani kwa Ine.”
19 And having commanded the crowds to recline upon the grass, having taken the five loaves and the two fishes, he looked up to heaven, and blessed: and having broken the loaves, he gave [them] to the disciples, and the disciples [gave them] to the crowds.
Analamula anthu kuti akhale pansi pa udzu ndipo anatenga buledi musanu ndi nsomba ziwiri nayangʼana kumwamba, nayamika nagawa bulediyo. Kenaka anapereka bulediyo kwa ophunzira ake ndipo ophunzirawo anagawira anthu.
20 And all ate and were filled, and they took up what was over and above of fragments twelve hand-baskets full.
Onse anadya nakhuta ndipo ophunzira anatola zotsalira ndi kudzaza madengu khumi ndi awiri.
21 But those that had eaten were about five thousand men, besides women and children.
Chiwerengero cha amene anadya kupatulako amayi ndi ana chinali pafupifupi amuna 5,000.
22 And immediately he compelled the disciples to go on board ship, and to go on before him to the other side, until he should have dismissed the crowds.
Nthawi yomweyo anawawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita kutsidya lina pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita kwawo.
23 And having dismissed the crowds, he went up into the mountain apart to pray. And when even was come, he was alone there,
Atatha kuwawuza kuti azipita kwawo, Iye anakwera ku phiri yekha kukapemphera. Pamene kumada anali kumeneko yekha.
24 but the ship was already in the middle of the sea tossed by the waves, for the wind was contrary.
Pamenepo nʼkuti bwato litapita patali pangʼono kuchokera ku mtunda ndipo linavutika ndi mafunde chifukwa mphepo inkawomba mokumana nalo.
25 But in the fourth watch of the night he went off to them, walking on the sea.
Pa ora lachinayi usiku, Yesu anabwera kwa iwo akuyendabe pa nyanja.
26 And the disciples, seeing him walking on the sea, were troubled, saying, It is an apparition. And they cried out through fear.
Ophunzira atamuona akuyenda pa nyanja, anaopa nati, “Ndi mzukwa!” Ndipo analira chifukwa cha mantha.
27 But Jesus immediately spoke to them, saying, Take courage; it is I: be not afraid.
Koma Yesu nthawi yomweyo anawawuza kuti, “Limbani mtima! Ndine, musaope.”
28 And Peter answering him said, Lord, if it be thou, command me to come to thee upon the waters.
Petro anayankha nati, “Ambuye ngati ndinu, mundiwuze ndibwere kuli inuko pa madzipo.”
29 And he said, Come. And Peter, having descended from the ship, walked upon the waters to go to Jesus.
Iye anati, “Bwera.” Pamenepo Petro anatuluka mʼbwato ndipo anayenda pa madzi kupita kwa Yesu.
30 But seeing the wind strong he was afraid; and beginning to sink he cried out, saying, Lord, save me.
Koma ataona mphepo, iye anachita mantha ndipo anayamba kumira, nafuwula nati, “Ambuye ndipulumutseni!”
31 And immediately Jesus stretched out his hand and caught hold of him, and says to him, O thou of little faith, why didst thou doubt?
Ndipo mofulumira Yesu anatambasula dzanja lake namugwira iye, nati, “Iwe wachikhulupiriro chochepa, bwanji unakayika?”
32 And when they had gone up into the ship, the wind fell.
Ndipo atalowa mʼbwato mphepo inaleka.
33 But those in the ship came and did homage to him, saying, Truly thou art God's Son.
Pamenepo amene anali mʼbwato anamulambira Iye, nati, “Zoonadi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu.”
34 And having crossed over they came to the land of Gennesaret.
Atawoloka, anafika ku Genesareti.
35 And when the men of that place recognised him, they sent to that whole country around, and they brought to him all that were ill,
Anthu akumeneko atamuzindikira Yesu, iwo anatumiza mawu kwa onse ozungulira deralo. Anthu anabwera ndi odwala awo onse kwa Iye.
36 and besought him that they might only touch the hem of his garment; and as many as touched were made thoroughly well.
Ndipo anamupempha alole kuti akhudze mphonje ya mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachiritsidwa.

< Matthew 14 >