< Lamentations 3 >

1 I am the man that hath seen affliction by the rod of his wrath.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 Me hath he led, and brought into darkness, and not into light.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 Surely against me hath he turned again and again his hand all the day.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 My flesh and my skin hath he wasted away, he hath broken my bones.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 He hath built against me, and encompassed [me] with gall and toil.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 He hath made me to dwell in dark places as those that have been long dead.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 He hath hedged me about that I cannot get out: he hath made my chain heavy.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Even when I cry and shout, he shutteth out my prayer.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 He hath inclosed my ways with hewn stone, he hath made my paths crooked.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 He is unto me [as] a bear lying in wait, a lion in secret places.
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 He hath turned aside my ways, and pulled me in pieces; he hath made me desolate.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 He hath bent his bow, and set me as a mark for the arrow.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 He hath caused the arrows of his quiver to enter into my reins.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 I am become a derision to all my people; their song all the day.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 He hath sated me with bitterness, he hath made me drunk with wormwood.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 He hath also broken my teeth with gravel stones, he hath covered me with ashes.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 And thou hast removed my soul far off from peace: I have forgotten prosperity.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 And I said, My strength is perished, and my hope in Jehovah.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 Remember thou mine affliction and my wandering, the wormwood and the gall.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 My soul hath [them] constantly in remembrance, and is humbled in me.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 — This I recall to heart, therefore have I hope.
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 It is of Jehovah's loving-kindness we are not consumed, because his compassions fail not;
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 they are new every morning: great is thy faithfulness.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Jehovah is my portion, saith my soul; therefore will I hope in him.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 Jehovah is good unto them that wait for him, to the soul [that] seeketh him.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 It is good that one should both wait, and that in silence, for the salvation of Jehovah.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 It is good for a man that he bear the yoke in his youth:
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 He sitteth solitary and keepeth silence, because he hath laid it upon him;
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 he putteth his mouth in the dust, if so be there may be hope;
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 he giveth his cheek to him that smiteth him; he is filled full with reproach.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 For the Lord will not cast off for ever;
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 but if he have caused grief, he will have compassion according to the multitude of his loving-kindnesses:
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 for he doth not willingly afflict or grieve the children of men.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 To crush under foot all the prisoners of the earth,
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 to turn aside the right of a man before the face of the Most High,
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 to wrong a man in his cause, — will not the Lord see it?
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 Who is he that saith, and there cometh to pass, what the Lord hath not commanded?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 Out of the mouth of the Most High doth not there proceed evil and good?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Wherefore doth a living man complain, a man for the punishment of his sins?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 Let us search and try our ways, and turn again to Jehovah.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Let us lift up our heart with [our] hands unto God in the heavens.
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 We have transgressed and have rebelled: thou hast not pardoned.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 Thou hast covered thyself with anger, and pursued us; thou hast slain, thou hast not spared.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 Thou hast covered thyself with a cloud, that prayer should not pass through.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Thou hast made us the offscouring and refuse in the midst of the peoples.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 All our enemies have opened their mouth against us.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Fear and the pit are come upon us, devastation and ruin.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Mine eye runneth down with streams of water for the ruin of the daughter of my people.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 Mine eye poureth down, and ceaseth not, without any intermission,
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 till Jehovah look down and behold from the heavens.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Mine eye affecteth my soul, because of all the daughters of my city.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 They that are mine enemies without cause have chased me sore like a bird.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 They have cut off my life in a pit, and cast a stone upon me.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 Waters streamed over my head; I said, I am cut off.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 I called upon thy name, Jehovah, out of the lowest pit.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Thou hast heard my voice: hide not thine ear at my sighing, at my cry.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Thou drewest near in the day that I called upon thee; thou saidst, Fear not.
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 Lord, thou hast pleaded the cause of my soul, thou hast redeemed my life.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 Jehovah, thou hast seen my wrong: judge thou my cause.
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 Thou hast seen all their vengeance, all their imaginations against me.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 Thou hast heard their reproach, O Jehovah, all their imaginations against me;
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 the lips of those that rise up against me and their meditation against me all the day.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Behold thou their sitting down and their rising up: I am their song.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 Render unto them a recompence, O Jehovah, according to the work of their hands;
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 give them obduracy of heart, thy curse unto them;
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 pursue them in anger, and destroy them from under the heavens of Jehovah.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< Lamentations 3 >