< Judges 21 >

1 Now the men of Israel had sworn in Mizpah, saying, There shall not any of us give his daughter to the Benjaminites as wife.
Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”
2 And the people came to Bethel, and abode there till even before God, and lifted up their voices and wept bitterly,
Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri.
3 and said, Jehovah, God of Israel, why is it come to pass in Israel, that there should be this day one tribe lacking in Israel?
Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”
4 And it came to pass on the morrow, that the people rose early, and built there an altar, and offered up burnt-offerings and peace-offerings.
Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.
5 And the children of Israel said, Who is there among all the tribes of Israel that came not up with the congregation to Jehovah? For they had [made] a great oath concerning him that came not up to Jehovah to Mizpah, saying, He shall certainly be put to death.
Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.
6 And the children of Israel repented them for Benjamin their brother, and said, To-day is one tribe extirpated from Israel.
Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli.
7 What shall we do for wives for them that remain? since we have sworn by Jehovah that we will not give them of our daughters for wives.
Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire.
8 And they said, What one is there of the tribes of Israel that came not up to Mizpah to Jehovah? And behold, there came none to the camp from Jabesh-Gilead, to the congregation;
Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja.
9 for the people were numbered, and behold, there were none of the inhabitants of Jabesh-Gilead there.
Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.
10 And the assembly sent thither twelve thousand men of the most valiant and commanded them, saying, Go and smite the inhabitants of Jabesh-Gilead with the edge of the sword, and the women and the children.
Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.”
11 And this is the thing which ye shall do: ye shall utterly destroy every male, and every woman that hath lain with man.
Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.”
12 And they found among the inhabitants of Jabesh-Gilead four hundred young women that were virgins, who had known no man by lying with any male, and they brought them to the camp, to Shiloh, which is in the land of Canaan.
Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.
13 And the whole assembly sent to speak to the children of Benjamin that were at the cliff of Rimmon, and to proclaim peace to them.
Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha.
14 And Benjamin came again at that time; and they gave them the wives whom they had saved alive of the women of Jabesh-Gilead; but even so they found not enough for them.
Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.
15 And the people repented them for Benjamin, because Jehovah had made a breach in the tribes of Israel.
Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli.
16 And the elders of the assembly said, What shall we do for wives for them that remain? for the women have been destroyed out of Benjamin.
Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?”
17 And they said, There must be a possession for those of Benjamin that have escaped, that a tribe be not blotted out of Israel.
Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike.
18 But we cannot give them wives of our daughters, for the children of Israel have sworn, saying, Cursed be he that giveth a wife to the Benjaminites!
Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’
19 And they said, Behold, there is a feast of Jehovah from year to year in Shiloh, which is on the north side of Bethel, toward the sun-rising of the highway that goes up from Bethel to Shechem, and on the south of Lebonah.
Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’”
20 And they commanded the sons of Benjamin, saying, Go and lie in wait in the vineyards;
Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa
21 and see, and behold, if the daughters of Shiloh come out to dance in the dances, then come out of the vineyards, and catch you every man his wife of the daughters of Shiloh, and go to the land of Benjamin.
ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini.
22 And it shall be, when their fathers or their brethren come to complain to us, that we will say to them, Gratify us with them, because we did not take each man his wife in the war; for ye did not give them to them, that ye should now be guilty.
Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’”
23 And the children of Benjamin did so, and took wives, according to their number, of them that danced, whom they caught; and they went and returned to their inheritance, and built the cities, and dwelt in them.
Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.
24 And the children of Israel departed thence at that time, every man to his tribe and to his family, and they went out from thence every man to his inheritance.
Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.
25 In those days there was no king in Israel; every man did what was right in his own eyes.
Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.

< Judges 21 >