< Judges 16 >

1 And Samson went to Gazah, and saw there a harlot, and went in to her.
Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
2 [And it was told] the Gazathites, saying, Samson is come hither. And they surrounded [him], and laid wait for him all night at the gate of the city, and were quiet all the night, saying, In the morning light we will kill him.
Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
3 And Samson lay till midnight; and he arose at midnight, and seized the doors of the gate of the city, and the two posts, and tore them up with the bar, and put [them] upon his shoulders, and carried them up to the top of the mountain that is before Hebron.
Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
4 And it came to pass afterwards that he loved a woman in the valley of Sorek, whose name was Delilah.
Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
5 And the lords of the Philistines came up to her, and said to her, Persuade him, and see in what his great strength is, and with what we may prevail against him, that we may bind him to overpower him; and we will each give thee eleven hundred silver-pieces.
Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
6 Then Delilah said to Samson, Tell me, I pray thee, in what is thy great strength, and with what thou mightest be bound to overpower thee.
Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
7 And Samson said to her, If they should bind me with seven fresh cords which have not been dried, then should I be weak, and be as another man.
Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
8 Then the lords of the Philistines brought up to her seven fresh cords which had not been dried, and she bound him with them.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
9 Now she had liers in wait abiding in the chamber; and she said to him, The Philistines are upon thee, Samson! And he broke the cords, as a thread of tow is broken when it touches the fire; and his strength was not known.
Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
10 And Delilah said to Samson, Behold, thou hast mocked me and told me lies. Now tell me, I pray thee, with what thou mightest be bound.
Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
11 And he said to her, If they should bind me fast with new ropes, with which no work has been done, then should I be weak, and be as another man.
Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
12 And Delilah took new ropes, and bound him with them, and said to him, The Philistines are upon thee, Samson! Now there were liers in wait abiding in the chamber. And he broke them from off his arms like a thread.
Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
13 And Delilah said to Samson, Hitherto thou hast mocked me and told me lies. Tell me with what thou mightest be bound. And he said to her, If thou shouldest weave the seven locks of my head with the web.
Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
14 And she fastened it with the pin, and said to him, The Philistines are upon thee, Samson! And he awoke out of his sleep, and tore out the pin of the beam, and the web.
Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
15 Then she said to him, How canst thou say, I love thee, when thy heart is not with me? these three times hast thou mocked me, and hast not told me in what is thy great strength.
Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
16 And it came to pass when she pressed him daily with her words and urged him, that his soul was vexed unto death;
Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
17 and he told her all his heart, and said to her, There has not come a razor upon my head; for I am a Nazarite of God from my mother's womb; if I should be shaven, then my strength would go from me, and I should be weak, and be like all mankind.
Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
18 And Delilah saw that he had told her all his heart, and she sent and called for the lords of the Philistines, saying, Come up this time, for he has told me all his heart. And the lords of the Philistines came up to her, and brought the money in their hand.
Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
19 And she made him sleep upon her knees, and called a man, and she caused him to shave off the seven locks of his head; and she began to overpower him, and his strength went from him.
Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
20 And she said, The Philistines are upon thee, Samson! And he awoke out of his sleep, and thought, I will go out as at other times before, and disengage myself. And he knew not that Jehovah had departed from him.
Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
21 And the Philistines seized him, and put out his eyes, and brought him down to Gazah, and bound him with fetters of bronze; and he had to grind in the prison-house.
Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
22 But the hair of his head began to grow after he was shaved.
Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
23 Then the lords of the Philistines gathered together to sacrifice a great sacrifice to Dagon their god, and to rejoice; for they said, Our god has given Samson our enemy into our hands.
Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
24 And when the people saw him, they praised their god; for they said, Our god has given into our hands our enemy, and the destroyer of our country, even him who multiplied our slain.
Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
25 And it came to pass when their hearts were merry, that they said, Call for Samson, that he may make us sport. And they called for Samson out of the prison-house, and he played before them; and they set him between the pillars.
Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
26 And Samson said to the lad that held him by the hand, Let loose of me, and suffer me to feel the pillars upon which the house stands, that I may lean upon them.
Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
27 Now the house was full of men and women; and all the lords of the Philistines were there; and upon the roof there were about three thousand men and women, who looked on while Samson made sport.
Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
28 And Samson called to Jehovah, and said, Lord Jehovah, remember me, I pray thee, and strengthen me, I pray thee, only this once, O God, that I may take one vengeance upon the Philistines for my two eyes.
Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
29 And Samson took hold of the two middle pillars upon which the house stood (and he supported himself upon them), the one with his right hand and the other with his left.
Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
30 And Samson said, Let me die with the Philistines! And he bowed himself with might; and the house fell on the lords, and on all the people that were therein. So the dead that he slew at his death were more than those whom he had slain in his life.
ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
31 And his brethren came down, and all the house of his father, and took him, and brought him up, and buried him between Zoreah and Eshtaol in the sepulchre of Manoah his father. And he had judged Israel twenty years.
Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.

< Judges 16 >