< Joshua 20 >

1 And Jehovah spoke to Joshua, saying,
Pambuyo pake Yehova anati kwa Yoswa:
2 Speak to the children of Israel, saying, Appoint for yourselves the cities of refuge, whereof I spoke unto you through Moses,
“Uza Aisraeli kuti apatule mizinda yopulumukiramo, monga ine ndinakulangizira kudzera mwa Mose,
3 that the slayer who unwittingly without intent smiteth any one mortally may flee thither: and they shall be your refuge from the avenger of blood.
kuti aliyense amene wapha munthu mosazindikira osati mwadala azithawirako. Motero adzatetezedwa kwa wolipsira.
4 And he shall flee unto one of those cities and stand at the entrance of the city-gate, and shall declare his matter in the ears of the elders of that city; and they shall take him into the city unto them, and give him a place, that he may dwell among them.
Ngati munthu wathawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi, akafike pa malo oweruzira milandu amene ali pa chipata cha mzindawo ndipo akafotokoze mlandu wake pamaso pa akuluakulu a mzindawo. Kenaka iwo adzamulola kulowa mu mzinda wawo ndi kumupatsa malo woti akhale nawo.
5 And if the avenger of blood pursue after him, they shall not deliver the slayer up into his hand; for he smote his neighbour unwittingly, and hated him not previously.
Ngati munthu wolipsirayo amutsatira komweko atsogoleriwo asapereke munthu wakuphayo chifukwa anapha Mwisraeli mnzakeyo mosazindikira, osati mwachiwembu.
6 And he shall dwell in that city, until he have stood before the assembly in judgment, until the death of the high-priest that shall be in those days; then shall the slayer return, and come unto his own city, and unto his own house, unto the city from whence he fled.
Munthu wakuphayo adzakhalabe mu mzindawo mpaka atayimbidwa mlandu pamaso pa gulu lonse, ndiponso mpaka atamwalira mkulu wa ansembe amene akutumikira pa nthawiyo. Pamenepo munthuyo atha kubwereranso ku mudzi kwawo kumene anachoka mothawa kuja.”
7 And they hallowed Kedesh in Galilee in the hill-country of Naphtali, and Shechem in the hill-country of Ephraim, and Kirjath-Arba, that is, Hebron, in the hill-country of Judah.
Choncho iwo anapatula Kedesi mʼdera la Galileya ku mapiri a Nafutali, Sekemu ku mapiri a Efereimu, ndi Kiriati Ariba (ndiye Hebroni) ku mapiri a Yuda.
8 And beyond the Jordan from Jericho eastward, they assigned Bezer in the wilderness, in the plateau, out of the tribe of Reuben, and Ramoth in Gilead out of the tribe of Gad, and Golan in Bashan of the tribe of Manasseh.
Kummawa kwa Yorodani, mʼmapiri a chipululu a kummawa kwa Yeriko, anapatula Bezeri pakati pa dera la fuko la Rubeni. Anapatulanso Ramoti ku Giliyadi mʼdera la fuko la Gadi, ndiponso Golani ku Basani mʼdera la fuko la Manase.
9 These were the cities appointed for all the children of Israel, and for the stranger that sojourneth among them, that whosoever smiteth any one mortally without intent might flee thither, and not die by the hand of the avenger of blood, until he stood before the assembly.
Imeneyi ndiyo inali mizinda yopulumukiramo ya Aisraeli onse ngakhalenso mlendo wokhala pakati pawo. Munthu aliyense wopha mnzake mwangozi ankathawira ku mizinda imeneyi. Munthu wolipsira sankaloledwa kuti aphe munthu wothawayo ngati mlandu wake sunazengedwe pamaso pa gulu lonse.

< Joshua 20 >