< Job 32 >

1 And these three men ceased to answer Job, because he was righteous in his own eyes.
Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
2 Then was kindled the anger of Elihu the son of Barachel, the Buzite, of the family of Ram: against Job was his anger kindled, because he justified himself rather than God;
Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
3 and against his three friends was his anger kindled, because they found no answer, and [yet] condemned Job.
Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
4 But Elihu had waited till Job had finished speaking, because they were older than he.
Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
5 And Elihu saw that there was no answer in the mouth of the three men, and his anger was kindled.
Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
6 And Elihu the son of Barachel the Buzite answered and said, I am young, and ye are aged; wherefore I was timid, and feared to shew you what I know.
Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
7 I said, Let days speak, and multitude of years teach wisdom.
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
8 But there is a spirit which is in man; and the breath of the Almighty giveth them understanding.
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
9 It is not the great that are wise; neither do the aged understand judgment.
Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
10 Therefore I say, Hearken to me; I also will shew what I know.
“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 Lo, I waited for your words; I gave ear to your reasonings, until ye searched out what to say.
Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12 Yea, I gave you mine attention, and behold, there was none of you that confuted Job, that answered his words;
ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 That ye may not say, We have found out wisdom; God will make him yield, not man.
Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 Now he hath not directed [his] words against me; and I will not answer him with your speeches. ...
Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
15 They were amazed, they answered no more; words failed them.
“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
16 And I waited, for they spoke not, but stood still, and answered no more; —
Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 I will answer, I also in my turn, I also will shew what I know:
Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 For I am full of matter, the spirit within me constraineth me.
Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 Behold, my belly is as wine which hath no vent; like new flasks, it is ready to burst.
mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 I will speak, that I may find relief; I will open my lips and answer.
Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Let me not, I pray you, accept any man's person; neither will I give flattery to man.
Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
22 For I know not how to flatter; my Maker would soon take me away.
pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

< Job 32 >