< Job 10 >

1 My soul is weary of my life: I will give free course to my complaint; I will speak in the bitterness of my soul.
“Ine ndatopa nawo moyo wanga; choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.
2 I will say unto God, Do not condemn me; shew me wherefore thou strivest with me.
Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa, koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.
3 Doth it please thee to oppress, that thou shouldest despise the work of thy hands, and shine upon the counsel of the wicked?
Kodi mumakondwera mukamandizunza, kunyoza ntchito ya manja anu, chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?
4 Hast thou eyes of flesh? or seest thou as man seeth?
Kodi maso anu ali ngati a munthu? Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?
5 Are thy days as the days of a mortal? are thy years as a man's days,
Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu, kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,
6 That thou searchest after mine iniquity, and inquirest into my sin;
kuti Inu mufufuze zolakwa zanga ndi kulondola tchimo langa,
7 Since thou knowest that I am not wicked, and that there is none that delivereth out of thy hand?
ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?
8 Thy hands have bound me together and made me as one, round about; yet dost thou swallow me up!
“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu. Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?
9 Remember, I beseech thee, that thou hast made me as clay, and wilt bring me into dust again.
Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi, kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?
10 Hast thou not poured me out as milk, and curdled me like cheese?
Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale, suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?
11 Thou hast clothed me with skin and flesh, and knit me together with bones and sinews;
Munandikuta ndi khungu ndi mnofu ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?
12 Thou hast granted me life and favour, and thy care hath preserved my spirit;
Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu, ndipo munasamalira bwino moyo wanga.
13 And these things didst thou hide in thy heart; I know that this was with thee.
“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu, ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:
14 If I sinned, thou wouldest mark me, and thou wouldest not acquit me of mine iniquity.
Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.
15 If I were wicked, woe unto me! and righteous, I will not lift up my head, being [so] full of shame, and beholding mine affliction; —
Ngati ndili wolakwa, tsoka langa! Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga, pakuti ndagwidwa ndi manyazi ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.
16 And it increaseth: thou huntest me as a fierce lion; and ever again thou shewest thy marvellous power upon me.
Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.
17 Thou renewest thy witnesses before me and increasest thy displeasure against me; successions [of evil] and a time of toil are with me.
Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.
18 And wherefore didst thou bring me forth out of the womb? I had expired, and no eye had seen me.
“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe? Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.
19 I should be as though I had not been; I should have been carried from the womb to the grave.
Ndikanapanda kubadwa, kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!
20 Are not my days few? cease then and let me alone, that I may revive a little,
Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha? Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha
21 Before I go, and never to return, — to the land of darkness and the shadow of death;
ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,
22 A land of gloom, as darkness itself; of the shadow of death, without any order, where the light is as thick darkness.
ku dziko la mdima wandiweyani ndi chisokonezo, kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

< Job 10 >