< Genesis 39 >

1 And Joseph was brought down to Egypt; and Potiphar, a chamberlain of Pharaoh, the captain of the life-guard, an Egyptian, bought him of the hand of the Ishmaelites who had brought him down thither.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 And Jehovah was with Joseph, and he was a prosperous man; and he was in the house of his master the Egyptian.
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 And his master saw that Jehovah was with him, and that Jehovah made all that he did to prosper in his hand.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 And Joseph found favour in his eyes, and attended on him; and he set him over his house, and all that he had he gave into his hand.
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 And it came to pass from the time he had set him over his house and all that he had, that Jehovah blessed the Egyptian's house for Joseph's sake; and the blessing of Jehovah was on all that he had in the house and in the field.
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 And he left all that he had in Joseph's hand, and took cognizance of nothing with him, save the bread that he ate. And Joseph was of a beautiful form and of a beautiful countenance.
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 And it came to pass after these things, that his master's wife cast her eyes on Joseph, and said, Lie with me!
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 But he refused, and said to his master's wife, Behold, my master takes cognizance of nothing with me: what is in the house, and all that he has, he has given into my hand.
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 There is none greater in this house than I; neither has he withheld anything from me but thee, because thou art his wife; and how should I do this great wickedness, and sin against God?
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 And it came to pass as she spoke to Joseph day by day and he hearkened not to her, to lie with her [and] to be with her,
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 that on a certain day he went into the house to do his business, and there was none of the men of the house there in the house.
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 Then she caught him by his garment, saying, Lie with me! But he left his garment in her hand, and fled and ran out.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 And it came to pass, when she saw that he had left his garment in her hand and had fled forth,
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 that she called to the men of her house, and spoke to them, saying, See, he has brought in a Hebrew man to us, to mock us: he came in to me, to lie with me; and I cried with a loud voice;
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 and it came to pass when he heard that I lifted up my voice and cried, that he left his garment with me, and fled and went out.
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 And she laid his garment by her until his lord came home.
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 And she spoke to him according to these words, saying, The Hebrew bondman that thou hast brought to us came in to me to mock me;
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 and it came to pass as I lifted up my voice and cried, that he left his garment with me, and fled forth.
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 And it came to pass when his lord heard the words of his wife which she spoke to him, saying, After this manner did thy bondman to me, that his wrath was kindled.
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 And Joseph's lord took him and put him into the tower-house, [the] place where the king's prisoners were confined; and he was there in the tower-house.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 And Jehovah was with Joseph, and extended mercy to him, and gave him favour in the eyes of the chief of the tower-house.
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 And the chief of the tower-house committed to Joseph's hand all the prisoners that were in the tower-house; and whatever they had to do there he did.
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 The chief of the tower-house looked not to anything under his hand, because Jehovah was with him; and what he did, Jehovah made it prosper.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.

< Genesis 39 >