< Ezekiel 28 >

1 And the word of Jehovah came unto me, saying,
Yehova anandiyankhula nati:
2 Son of man, say unto the prince of Tyre, Thus saith the Lord Jehovah: Because thy heart is lifted up, and thou hast said, I am a god, I sit [in] the seat of God, in the heart of the seas, (and thou art a man, and not God, ) and thou settest thy heart as the heart of God:
“Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu; ndimakhala pa mpando wa mulungu pakati pa nyanja.’ Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu, ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.
3 behold, thou art wiser than Daniel! nothing secret is obscure for thee;
Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli. Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.
4 by thy wisdom and by thine understanding thou hast gotten thee riches, and hast gotten gold and silver into thy treasures;
Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako unadzipezera chuma ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva mʼnyumba zosungira chuma chako.
5 by thy great wisdom thou hast by thy traffic increased thy riches, and thy heart is lifted up because of thy riches.
Ndi nzeru zako zochitira malonda unachulukitsa chuma chako ndipo wayamba kunyada chifukwa cha chuma chakocho.
6 Therefore thus saith the Lord Jehovah: Because thou hast set thy heart as the heart of God,
“‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Popeza umadziganizira kuti ndiwe mulungu,
7 therefore behold, I will bring strangers upon thee, the terrible of the nations; and they shall draw their swords against the beauty of thy wisdom, and they shall tarnish thy brightness.
Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza, kuti adzalimbane nawe. Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako, ndipo adzawononga kunyada kwakoko.
8 They shall bring thee down to the pit, and thou shalt die the deaths of those that are slain in the heart of the seas.
Iwo adzakuponyera ku dzenje ndipo udzafa imfa yoopsa mʼnyanja yozama.
9 Wilt thou then say before him that slayeth thee, I am God? but thou shalt be a man, and not God, in the hand of him that pierceth thee.
Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’ pamaso pa iwo amene akukupha? Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu, mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.
10 Thou shalt die the deaths of the uncircumcised, by the hand of strangers: for I have spoken [it], saith the Lord Jehovah.
Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe mʼmanja mwa anthu achilendo. Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’”
11 And the word of Jehovah came unto me, saying,
Yehova anandiyankhula kuti:
12 Son of man, take up a lamentation upon the king of Tyre, and say unto him, Thus saith the Lord Jehovah: Thou, who sealest up the measure of perfection, full of wisdom and perfect in beauty,
“Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, “‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni, wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.
13 thou wast in Eden, the garden of God. Every precious stone was thy covering: the sardius, the topaz, and the diamond, the chrysolite, the onyx, and the jasper, the sapphire, the carbuncle, and the emerald, and gold. The workmanship of thy tambours and of thy pipes was in thee: in the day that thou wast created were they prepared.
Iwe unkakhala ngati mu Edeni, munda wa Mulungu. Miyala yokongola ya mitundu yonse: rubi, topazi ndi dayimondi, kirisoliti, onikisi, yasipa, safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako. Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide. Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.
14 Thou wast the anointed covering cherub, and I had set thee [so]: thou wast upon the holy mountain of God; thou didst walk up and down in the midst of stones of fire.
Ndinayika kerubi kuti azikulondera. Unkakhala pa phiri langa lopatulika, ndipo unkayendayenda pakati pa miyala ya moto.
15 Thou wast perfect in thy ways, from the day that thou wast created, till unrighteousness was found in thee.
Makhalidwe ako anali abwino kuyambira pamene unalengedwa mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.
16 By the abundance of thy traffic they filled the midst of thee with violence, and thou hast sinned; therefore have I cast thee as profane from the mountain of God, and have destroyed thee, O covering cherub, from the midst of the stones of fire.
Unatanganidwa ndi zamalonda. Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu ndi kumachimwa. Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika. Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa kukuchotsa ku miyala yamoto.
17 Thy heart was lifted up because of thy beauty; thou hast corrupted thy wisdom by reason of thy brightness: I have cast thee to the ground, I have laid thee before kings, that they may behold thee.
Unkadzikuza mu mtima mwako chifukwa cha kukongola kwako, ndipo unayipitsa nzeru zako chifukwa chofuna kutchuka. Kotero Ine ndinakugwetsa pansi kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.
18 By the multitude of thine iniquities, by the unrighteousness of thy traffic, thou hast profaned thy sanctuaries: and I have brought forth a fire out of the midst of thee — it hath consumed thee; and I have brought thee to ashes upon the earth, in the sight of all them that behold thee.
Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako. Motero unayipitsa malo ako achipembedzo. Choncho ndinabutsa moto pakati pako, ndipo unakupsereza, ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi pamaso pa anthu onse amene amakuona.
19 All they that know thee among the peoples shall be amazed at thee: thou art become a terror, and thou shalt never be any more.
Anthu onse amitundu amene ankakudziwa akuchita mantha chifukwa cha iwe. Watheratu mochititsa mantha ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’”
20 And the word of Jehovah came unto me, saying,
Yehova anandiyankhula nati:
21 Son of man, set thy face towards Zidon, and prophesy against it,
“Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti,
22 and say, Thus saith the Lord Jehovah: Behold, I am against thee, Zidon, and I will be glorified in the midst of thee; and they shall know that I [am] Jehovah, when I shall have executed judgments in her, and shall be hallowed in her.
‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni, ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe. Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti ndine woyera pakati pako.
23 And I will send into her the pestilence, and blood in her streets; and the wounded shall fall in the midst of her, by the sword upon her on every side: and they shall know that I [am] Jehovah.
Ndidzatumiza mliri pa iwe ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako. Anthu ophedwa ndi lupanga adzagwa mbali zonse. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
24 And there shall be no more a wounding sting for the house of Israel, nor any grieving thorn, among all that were round about them, that despised them: and they shall know that I [am] the Lord Jehovah.
“‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
25 Thus saith the Lord Jehovah: When I shall have gathered the house of Israel from the peoples among whom they are scattered, and shall be hallowed in them in the sight of the nations, then shall they dwell in their land which I have given to my servant Jacob.
“‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo.
26 They shall dwell in it in safety, and shall build houses and plant vineyards; and they shall dwell in safety, when I have executed judgments upon all those that despised them round about them: and they shall know that I [am] Jehovah their God.
Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’”

< Ezekiel 28 >