< 2 Samuel 22 >

1 And David spoke to Jehovah the words of this song in the day that Jehovah had delivered him out of the hand of all his enemies, and out of the hand of Saul.
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 And he said, Jehovah is my rock, and my fortress, and my deliverer;
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 God is my rock, in him will I trust — My shield, and the horn of my salvation, My high tower, and my refuge, My saviour: thou wilt save me from violence.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 I will call upon Jehovah, who is to be praised; So shall I be saved from mine enemies.
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 For the waves of death encompassed me, Torrents of Belial made me afraid.
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 The bands of Sheol surrounded me; The cords of death encountered me; (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
7 In my distress I called upon Jehovah, And I cried to my God; And he heard my voice out of his temple, And my cry [came] into his ears.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 Then the earth shook, and quaked; The foundations of the heavens trembled And shook because he was wroth.
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 There went up a smoke out of his nostrils, And fire out of his mouth devoured: Coals burned forth from it.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 And he bowed the heavens, and came down; And darkness was under his feet.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 And he rode upon a cherub, and did fly; And he was seen upon the wings of the wind.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 And he made darkness round about him a tent, Gatherings of waters, thick clouds of the skies.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 From the brightness before him Burned forth coals of fire.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 Jehovah thundered from the heavens, And the Most High uttered his voice.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 And he sent arrows, and scattered [mine enemies]; Lightning, and discomfited them.
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 And the beds of the sea were seen, The foundations of the world were uncovered At the rebuke of Jehovah, At the blast of the breath of his nostrils.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 He reached forth from above, he took me, He drew me out of great waters;
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 He delivered me from my strong enemy, From them that hated me; For they were mightier than I.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 They encountered me in the day of my calamity; But Jehovah was my stay.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 And he brought me forth into a large place; He delivered me, because he delighted in me.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 Jehovah hath rewarded me according to my righteousness, According to the cleanness of my hands hath he recompensed me.
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 For I have kept the ways of Jehovah, And have not wickedly departed from my God.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 For all his ordinances were before me, And his statutes, I did not depart from them,
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 And I was upright before him, And kept myself from mine iniquity.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 And Jehovah hath recompensed me according to my righteousness, According to my cleanness in his sight.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 With the gracious thou dost shew thyself gracious; With the upright man thou dost shew thyself upright;
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 With the pure thou dost shew thyself pure; And with the perverse thou dost shew thyself contrary.
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 And the afflicted people thou dost save; And thine eyes are upon the haughty, [whom] thou bringest down.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 For thou art my lamp, Jehovah; And Jehovah enlighteneth my darkness.
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 For by thee I have run through a troop; By my God have I leaped over a wall.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 As for God, his way is perfect; The word of Jehovah is tried: He is a shield to all that trust in him.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 For who is God, save Jehovah? And who is a rock, save our God?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 God is my strong fortress, And he maketh my way perfectly smooth.
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 He maketh my feet like hinds' [feet], And setteth me upon my high places.
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 He teacheth my hands to war, And mine arms bend a bow of brass.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 And thou didst give me the shield of thy salvation, And thy condescending gentleness hath made me great.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 Thou enlargedst my steps under me; And mine ankles did not slip.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 I pursued mine enemies, and destroyed them, And I turned not again till they were consumed.
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 And I have consumed them and have crushed them, and they rose not again; Yea, they fell under my feet.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 And thou girdedst me with strength to battle: Thou didst subdue under me those that rose up against me.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 And mine enemies didst thou make to turn their backs unto me, And those that hated me I destroyed.
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 They looked, and there was none to save — Unto Jehovah, and he answered them not.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 And I did beat them small as the dust of the earth, I trod them as the mire of the streets; I stamped upon them.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 And thou hast delivered me from the strivings of my people, Thou hast kept me to be head of the nations: A people I knew not doth serve me:
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 Strangers come cringing unto me: At the hearing of the ear, they obey me.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 Strangers have faded away, And they come trembling forth from their close places.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 Jehovah liveth; and blessed be my rock; And exalted be the God, the rock of my salvation,
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 The God who hath avenged me, And hath brought the peoples under me.
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 He brought me forth from mine enemies: Yea, thou hast lifted me up above them that rose up against me; From the man of violence hast thou delivered me.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 Therefore will I give thanks to thee, Jehovah, among the nations, And will sing psalms to thy name.
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 [It is he] who giveth great deliverances to his king, And sheweth loving-kindness to his anointed, To David, and to his seed for evermore.
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

< 2 Samuel 22 >