< 2 Samuel 10 >

1 And it came to pass after this that the king of the children of Ammon died, and Hanun his son reigned in his stead.
Patapita nthawi, mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake Hanuni analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 And David said, I will shew kindness to Hanun the son of Nahash, as his father shewed kindness to me. And David sent to comfort him by the hand of his servants for his father. And David's servants came into the land of the children of Ammon.
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni,
3 And the princes of the children of Ammon said to Hanun their lord, Is it, in thine eyes, to honour thy father that David has sent comforters to thee? Is it not to search the city and to spy it out, and to overthrow it, that David has sent his servants to thee?
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni mbuye wawo kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi Davide sanawatumize anthuwa kuti adzaone mzinda wanu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 And Hanun took David's servants, and had the one half of their beards shaved off, and their raiment cut off in the midst, as far as their buttocks, and sent them away.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anameta munthu aliyense mbali imodzi ya ndevu zake, ndi kudula zovala zake pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera, ndipo anawabweza kwawo.
5 And they told [it] to David; and he sent to meet them, for the men were greatly ashamed. And the king said, Abide at Jericho until your beards be grown, and then return.
Atamufotokozera Davide zimenezi, iye anatuma amithenga kukakumana ndi anthuwo chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 And the children of Ammon saw that they had made themselves odious to David; and the children of Ammon sent and hired the Syrians of Beth-Rehob, and the Syrians of Zoba, twenty thousand footmen, and the king of Maacah [with] a thousand men, and the men of Tob twelve thousand men.
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, anakapeza ankhondo oyenda pansi aganyu okwanira 20,000 kuchokera ku Asiriya wa ku Beti Rehobu ndi Aramu-Zoba, komanso ankhondo 1,000 kwa mfumu Maaka ndiponso ankhondo 22,000 ochokera ku Tobu.
7 And David heard [of it], and he sent Joab, and all the host, the mighty men.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
8 And the children of Ammon came out, and put the battle in array at the entrance of the gate; and the Syrians of Zoba and of Rehob, and the men of Tob and Maacah were by themselves in the field.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene Aaramu a ku Aramu-Zoba ndi Rehobu ndi ankhondo a ku Tobu ndi Maaka anali kwa wokha ku malo wopanda mitengo.
9 And Joab saw that the front of the battle was against him before and behind; and he chose out of all the choice men of Israel, and put them in array against the Syrians;
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake, iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
10 and the rest of the people he gave into the hand of Abishai his brother that he might array them against the children of Ammon.
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
11 And he said, If the Syrians be too strong for me, then thou shalt help me; and if the children of Ammon be too strong for thee, then I will come and help thee.
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse. Koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
12 Be strong, and let us shew ourselves valiant for our people and for the cities of our God; and Jehovah do what is good in his sight.
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
13 And Joab drew near, and the people that were with him, unto the battle against the Syrians; and they fled before him.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
14 And when the children of Ammon saw that the Syrians fled, they fled before Abishai, and entered into the city. And Joab returned from the children of Ammon, and came to Jerusalem.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai ndi kulowa mu mzinda. Nkhondo itatha, Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
15 And when the Syrians saw that they were routed before Israel, they gathered themselves together.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anasonkhananso.
16 And Hadarezer sent, and drew forth the Syrians that were beyond the river; and they came to Helam; and Shobach the captain of the host of Hadarezer [went] before them.
Hadadezeri anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, iwo anapita ku Helamu motsogozedwa ndi Sobaki mkulu wa ankhondo a Hadadezeri.
17 And it was told David; and he gathered all Israel, and passed over the Jordan, and came to Helam. And the Syrians set themselves in array against David, and fought with him.
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani ndipo anapita ku Helamu. Aaramu anayima mʼmizere yawo yankhondo kukakumana ndi Davide ndipo anamenyana naye.
18 And the Syrians fled before Israel; and David slew of the Syrians seven hundred [in] chariots, and forty thousand horsemen, and smote Shobach the captain of their host, who died there.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 700 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Davide anaphanso Sobaki mtsogoleri wawo wankhondo ndipo anafera pomwepo.
19 And all the kings that were servants to Hadarezer saw that they were routed before Israel, and they made peace with Israel, and served them. And the Syrians feared to help the children of Ammon any more.
Mafumu onse amene anali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, iwo anachita mtendere ndi Aisraeli ndipo anakhala pansi pawo. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.

< 2 Samuel 10 >