< 2 Chronicles 14 >

1 And Abijah slept with his fathers, and they buried him in the city of David. And Asa his son reigned in his stead. In his days the land was quiet ten years.
Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.
2 And Asa did what was good and right in the sight of Jehovah his God;
Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.
3 and he took away the altars of the strange [gods] and the high places, and broke the columns, and cut down the Asherahs;
Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera.
4 and commanded Judah to seek Jehovah the God of their fathers, and to practise the law and the commandment.
Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake.
5 And he removed out of all the cities of Judah the high places and the sun-images; and the kingdom was quiet before him.
Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake.
6 And he built fortified cities in Judah, for the land had rest, and he had no war in those years; because Jehovah had given him rest.
Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.
7 And he said to Judah, Let us build these cities, and surround them with walls and towers, gates and bars, while the land is yet before us; for we have sought Jehovah our God; we have sought him, and he has given us rest on every side. And they built and prospered.
Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.
8 And Asa had an army that bore targets and spears: out of Judah three hundred thousand; and out of Benjamin, that bore shields and drew the bow, two hundred and eighty thousand: all these, mighty men of valour.
Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.
9 And Zerah the Ethiopian came out against him with a host of a thousand thousand, and three hundred chariots, and he came to Mareshah.
Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa.
10 And Asa went out against him, and they set the battle in array in the valley of Zephathah near Mareshah.
Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.
11 And Asa cried unto Jehovah his God, and said, Jehovah, it maketh no difference to thee to help, whether there be much or no power: help us, O Jehovah our God, for we rely on thee, and in thy name have we come against this multitude. Jehovah, thou art our God; let not man prevail against thee.
Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”
12 And Jehovah smote the Ethiopians before Asa and before Judah; and the Ethiopians fled.
Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa,
13 And Asa and the people that were with him pursued them to Gerar; and the Ethiopians were overthrown, that none of them was left alive; for they were crushed before Jehovah and before his army. And they carried away very much spoil.
ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo.
14 And they smote all the cities round about Gerar, for the terror of Jehovah came upon them; and they spoiled all the cities, for there was very much spoil in them.
Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko.
15 They smote also the tents of cattle, and carried away sheep and camels in abundance, and returned to Jerusalem.
Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 Chronicles 14 >