< 1 Chronicles 18 >

1 And after this it came to pass that David smote the Philistines, and subdued them, and took Gath and its towns out of the hand of the Philistines.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Iye analanda Gati ndi midzi yake yozungulira mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 And he smote the Moabites; and the Moabites became David's servants, [and] brought gifts.
Davide anagonjetsanso Amowabu, nakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho kwa iye.
3 And David smote Hadarezer king of Zobah, at Hamath, as he went to establish his dominion by the river Euphrates.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mfumu ya Zoba, mpaka ku Hamati, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 And David took from him a thousand chariots, and seven thousand horsemen, and twenty thousand footmen; and David houghed all the chariot [horses], but reserved of them [for] a hundred chariots.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu okwera magaleta 7,000 pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 And the Syrians of Damascus came to help Hadarezer king of Zobah, and David smote of the Syrians twenty-two thousand men.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya ku Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 And David put [garrisons] in Syria of Damascus; and the Syrians became servants to David, [and] brought gifts. And Jehovah preserved David whithersoever he went.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 And David took the shields of gold that were on the servants of Hadarezer, and brought them to Jerusalem.
Davide anatenga zishango zagolide zimene ankanyamula akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 And from Tibhath, and from Chun, cities of Hadarezer, David took very much brass, of which Solomon made the brazen sea, and the pillars, and the vessels of brass.
Kuchokera ku Teba ndi Kuni, mizinda ya Hadadezeri, Davide anatengako mkuwa wambiri umene Solomoni anapangira chimbiya, zipilala ndi zida zosiyanasiyana zamkuwa.
9 And Tou king of Hamath heard that David had smitten all the forces of Hadarezer king of Zobah;
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri mfumu ya Zoba,
10 and he sent Hadoram his son to king David to inquire of his welfare, and to congratulate him, because he had fought against Hadarezer and smitten him; for Hadarezer was continually at war with Tou; [he sent] also all manner of vessels of gold and silver and bronze.
anatumiza mwana wake Hadoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Hadoramu anabweretsa ziwiya zosiyanasiyana zagolide, zasiliva ndi zamkuwa.
11 Them also king David dedicated to Jehovah, with the silver and the gold that he had brought from all the nations: from the Edomites, and from the Moabites, and from the children of Ammon, and from the Philistines, and from the Amalekites.
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko ena onse monga Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki.
12 And Abishai the son of Zeruiah smote of the Edomites in the valley of salt eighteen thousand.
Abisai mwana wa Zeruya anakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
13 And he put garrisons in Edom; and all they of Edom became servants to David. And Jehovah preserved David whithersoever he went.
Iye anayika maboma ku Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
14 And David reigned over all Israel, and executed judgment and justice to all his people.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
15 And Joab the son of Zeruiah was over the host; and Jehoshaphat the son of Ahilud was chronicler;
Yowabu, mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika;
16 and Zadok the son of Ahitub, and Abimelech the son of Abiathar, were the priests; and Shavsha was scribe;
Zadoki, mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Savisa anali mlembi;
17 and Benaiah the son of Jehoiada was over the Cherethites and the Pelethites; and the sons of David were the first at the king's hand.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti, ndipo ana a Davide anali alangizi a mfumu.

< 1 Chronicles 18 >