< Zechariah 4 >

1 And the angel who had been speaking with me returned, and he awakened me, like a man who is awakened from his sleep.
Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
2 And he said to me, “What do you see?” And I said, “I looked, and behold, a candlestick entirely in gold, and its lamp was at its top, and seven oil lamps of it were upon it, and there were seven funnels for the oil lamps that were at its top.
Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
3 And there were two olive trees upon it: one to the right of the lamp, and one to its left.”
Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
4 And I answered and spoke to the angel who was speaking with me, saying, “What are these, my lord?”
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
5 And the angel who was speaking with me answered, and he said to me, “Do you not know what these are?” And I said, “No, my lord.”
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
6 And he answered and spoke to me, saying: This is the word of the Lord to Zerubbabel, saying: Not by an army, nor by might, but in my spirit, says the Lord of hosts.
Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
7 What are you, great mountain, in the sight of Zerubbabel? You are among the plains. And he will lead out the primary stone, and he will give equal grace to its grace.
“Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
8 And the word of the Lord came to me, saying:
Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
9 The hand of Zerubbabel has founded this house, and his hands will complete it. And you will know that the Lord of hosts has sent me to you.
“Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
10 For who has despised the little days? And they will rejoice and will see the silver and lead stone in the hand of Zerubbabel. These are the seven eyes of the Lord, which roam quickly through all the earth.
“Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
11 And I responded and said to him, “What are these two olive trees to the right of the candlestick, and to its left?”
Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
12 And I responded a second time and said to him, “What are the two olive branches, which are next to the two golden ridges, in which are the pouring spouts of gold?”
Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
13 And he spoke to me, saying, “Do you not know what these are?” And I said, “No, my lord.”
Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
14 And he said, “These are the two sons of oil, who attend before the Sovereign of all the earth.”
Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”

< Zechariah 4 >